< 1 Samuel 30 >

1 And it cometh to pass, in the coming in of David and his men to Ziklag, on the third day, that the Amalekites have pushed unto the south, and unto Ziklag, and smite Ziklag, and burn it with fire,
Pa tsiku lachitatu, Davide ndi anthu ake anakafika ku Zikilagi. Tsono anapeza Aamaleki atawononga kale dera la Negevi ndi Zikilagi. Anathira nkhondo mzinda wa Zikilagi ndi kuwutentha ndi moto.
2 and they take captive the women who [are] in it; from small unto great they have not put any one to death, and they lead away, and go on their way.
Anatenga akazi ndi onse amene anali mʼmenemo akuluakulu ndi angʼono omwe kuti akakhale akapolo. Sanaphe aliyense koma anawatenga amoyo napita nawo.
3 And David cometh in — and his men — unto the city, and lo, burnt with fire, and their wives, and their sons, and their daughters have been taken captive!
Davide ndi anthu ake atafika ku Zikilagi anapeza kuti mzindawo watenthedwa ndi moto ndipo akazi awo, ana awo, amuna ndi akazi atengedwa ukapolo.
4 And David lifteth up — and the people who [are] with him — their voice and weep, till that they have no power to weep.
Kotero Davide ndi anthu ake analira mofuwula mpaka analibenso mphamvu zolirira.
5 And the two wives of David have been taken captive, Ahinoam the Jezreelitess, and Abigail wife of Nabal the Carmelite;
Akazi awiri a Davide, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli anatengedwanso.
6 and David hath great distress, for the people have said to stone him, for the soul of all the people hath been bitter, each for his sons and for his daughters; and David doth strengthen himself in Jehovah his God.
Davide anavutika kwambiri mu mtima mwake chifukwa anthu amakamba zoti amuponye miyala popeza aliyense anali ndi chisoni pokumbukira ana ake aamuna ndi aakazi. Koma Davide anapeza mphamvu mwa Yehova Mulungu wake.
7 And David saith unto Abiathar the priest, son of Ahimelech, 'Bring nigh, I pray thee, to me the ephod;' and Abiathar bringeth nigh the ephod unto David,
Kenaka Davide anawuza wansembe Abiatara, mwana wa Ahimeleki kuti, “Ndipatse efodi ija.” Abiatara anabwera nayo efodiyo.
8 and David asketh at Jehovah, saying, 'I pursue after this troop — do I overtake it?' And He saith to him, 'Pursue, for thou dost certainly overtake, and dost certainly deliver.'
Tsono Davide anapempha nzeru kwa Yehova nati, “Kodi ndilitsatire gulu lankhondoli? Kodi ndidzawapambana?” Yehova anayankha kuti, “Litsatire, iwe udzawapambana ndithu ndipo udzapulumutsa anthu ako.”
9 And David goeth on, he and six hundred men who [are] with him, and they come in unto the brook of Besor, and those left have stood still,
Davide pamodzi ndi anthu ake 600 aja ananyamuka nafika ku mtsinje wa Besori. Kumeneko anasiyako anthu ena.
10 and David pursueth, he and four hundred men, (and two hundred men stand still who have been too faint to pass over the brook of Besor),
Davide ndi anthu ake 400 anapitirira kuwalondola Aamaleki aja. Koma anthu ena 200 anatsala popeza anatopa moti sakanatha kuwoloka mtsinje wa Besori uja.
11 and they find a man, an Egyptian, in the field, and take him unto David, and give to him bread, and he eateth, and they cause him to drink water,
Anthu amene anali ndi Davide anapeza Mwigupto mʼmunda wina ndipo anabwera naye kwa Davide. Iwo anamupatsa madzi kuti amwe ndi chakudya kuti adye.
12 and give to him a piece of a bunch of dried figs, and two bunches of raisins, and he eateth, and his spirit returneth unto him, for he hath not eaten bread nor drunk water three days and three nights.
Anamupatsanso chidutswa cha keke yankhuyu ndi makeke awiri a mphesa zowumika kuti adye. Atadya anapezanso mphamvu popeza anakhala masiku atatu wosadya kapena kumwa kanthu kalikonse.
13 And David saith to him, 'Whose [art] thou? and whence [art] thou?' And he saith, 'An Egyptian youth I [am], servant to a man, an Amalekite, and my lord forsaketh me, for I have been sick three days,
Davide anafunsa kuti, “Kodi ndiwe yani, ndipo ukuchokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine Mwigupto, kapolo wa Mwamaleki. Mbuye wanga anandisiya nditayamba kudwala masiku atatu apitawo.
14 we pushed [to] the south of the Cherethite, and against that which [is] to Judah, and against the south of Caleb, and Ziklag we burned with fire.'
Ife tinathira nkhondo dera la kummwera kwa mayiko a Akereti, dera la Yuda, ndi dera la kummwera kwa mayiko a Kalebe. Mzinda wa Zikilagi tinawutentha ndi moto.”
15 And David saith unto him, 'Dost thou bring me down unto this troop?' and he saith, 'Swear to me by God — thou dost not put me to death, nor dost thou shut me up into the hand of my lord — and I bring thee down unto this troop.'
Davide anamupempha kuti, “Kodi unganditsogolere kumene kuli gulu lankhondoli?” Iye anayankha kuti, “Mukandilonjeza molumbira kuti simudzandipha kapena kundipereka kwa mbuye wanga, ine ndikulondolerani kumene kuli gululo.”
16 And he bringeth him down, and lo, they are spread out over the face of all the earth, eating, and drinking, and feasting, with all the great spoil which they have taken out of the land of the Philistines, and out of the land of Judah.
Mwigupto uja anaperekeza Davide. Tsono Aamaleki anali atamwazikana ponseponse. Iwo ankadya, kumwa ndi kuvina chifukwa cha zofunkha zambiri zimene anatenga ku dziko la Afilisti ndi ku dziko la Ayuda.
17 And David smiteth them from the twilight even unto the evening of the morrow, and there hath not escaped of them a man, except four hundred young men who have ridden on the camels, and are fled.
Tsono Davide anawakantha kuyambira madzulo atsikulo mpaka madzulo a tsiku linalo. Palibe anapulumuka kupatula anyamata 400 amene anakwera pa ngamira nʼkuthawa.
18 And David delivereth all that the Amalekites have taken; also his two wives hath David delivered.
Choncho Davide analanditsa zinthu zonse zimene Aamaleki aja anatenga. Anapulumutsanso akazi ake awiri aja.
19 And there hath not lacked to them [anything], from small unto great, and unto sons and daughters, and from the spoil, even unto all that they had taken to themselves, the whole hath David brought back,
Palibe chimene chinasowa anthu onse, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, mnyamata mpaka mtsikana anapulumutsidwa. Davide anapulumutsa chilichonse chimene anafunkha Aamaleki aja.
20 and David taketh the whole of the flock, and of the herd, they have led on before these cattle, and they say, 'This [is] David's spoil.'
Anapulumutsanso nkhosa ndi ngʼombe zonse. Tsono anthu ankakusa ziwetozo namati, “Izi ndizo zofunkha za Davide.”
21 And David cometh in unto the two hundred men who were too faint to go after David, and whom they cause to abide at the brook of Besor, and they go out to meet David, and to meet the people who [are] with him, and David approacheth the people, and asketh of them of welfare.
Davide anafika ku malo kumene kunali anthu 200 otopa kwambiri aja amene sanathe kutsagana naye koma anangokhala ku mtsinje wa Besori. Tsono ananyamuka kuti akumane ndi Davide pamodzi ndi anthu amene anali naye. Davide anawayandikira nawalonjera.
22 And every bad and worthless man, of the men who have gone with David, answereth, yea, they say, 'Because that they have not gone with us we do not give to them of the spoil which we have delivered, except each his wife and his children, and they lead away and go.
Tsono anthu ena oyipa mtima achabechabe mwa amene anatsagana ndi Davide aja anati, “Popeza awa sanapite nafe, sitiwapatsako zofunkha zimene tapulumutsazi, kupatula kuti aliyense atenge mkazi wake ndi ana ake azipita.”
23 And David saith, 'Ye do not do so, my brethren, with that which Jehovah hath given to us, and He doth preserve us, and doth give the troop which cometh against us into our hand;
Koma Davide anawayankha kuti, “Ayi, abale anga, musachite zimenezi ndi zinthu zimene Yehova watipatsa. Iye watisunga ndi kupereka mʼmanja mwathu gulu la ankhondo limene linabwera kudzalimbana nafe.
24 and who doth hearken to you in this thing? for as the portion of him who was brought down into battle, so also [is] the portion of him who is abiding by the vessels — alike they share.'
Ndani angakumvereni zimene mukunenazi? Gawo la munthu amene anapita kukamenya nkhondo likhale lofanana ndi la munthu amene anatsala pano kuyangʼanira katundu wathu. Pasakhale kusiyana kulikonse.”
25 And it cometh to pass from that day and forward, that he appointeth it for a statute and for an ordinance for Israel unto this day.
Choncho Davide anakhazikitsa ngati lamulo mʼchitidwe woterewu pakati pa Aisraeli kuyambira tsiku limenelo mpaka lero.
26 And David cometh in unto Ziklag, and sendeth of the spoil to the elders of Judah, to his friends, (saying, 'Lo, for you a blessing, of the spoil of the enemies of Jehovah),'
Davide atafika ku Zikilagi, anatumiza zina mwa zofunkhazo kwa akuluakulu a Yuda, amene anali abwenzi ake. Anati, “Nayi mphatso yanu yochokera pa zofunkha za adani a Yehova.”
27 to those in Beth-El, and to those in South Ramoth, and to those in Jattir,
Iye anatumiza mphatsozo kwa anthu a ku Beteli, Ramoti-Negavi, Yatiri,
28 and to those in Aroer, and to those in Siphmoth, and to those in Eshtemoa,
Aroeri, Sifimoti, Esitemowa
29 and to those in Rachal, and to those in the cities of the Jerahmeelites, and to those in the cities of the Kenites,
Rakala, mizinda ya fuko la Ayerahimeeli, mizinda ya fuko la Akeni,
30 and to those in Hormah, and to those in Chor-Ashan, and to those in Athach,
a ku Horima, Borasani, Ataki,
31 and to those in Hebron, and to all the places where David had gone up and down, he and his men.
Hebroni pamodzi ndi onse a kumalo kumene Davide ndi anthu ake anakhala akuyendayendako.

< 1 Samuel 30 >