< 1 Samuel 27 >

1 And David saith unto his heart, 'Now am I consumed one day by the hand of Saul; there is nothing for me better than that I diligently escape unto the land of the Philistines, and Saul hath been despairing of me — of seeking me any more in all the border of Israel, and I have escaped out of his hand.'
Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
2 And David riseth, and passeth over, he and six hundred men who [are] with him, unto Achish son of Maoch king of Gath;
Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
3 and David dwelleth with Achish in Gath, he and his men, each one with his household, [even] David and his two wives, Ahinoam the Jezreelitess, and Abigail wife of Nabal the Carmelitess.
Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
4 And it is declared to Saul that David hath fled to Gath, and he hath not added any more to seek him.
Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
5 And David saith unto Achish, 'If, I pray thee, I have found grace in thine eyes, they give to me a place in one of the cities of the field, and I dwell there, yea, why doth thy servant dwell in the royal city with thee?'
Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
6 And Achish giveth to him in that day Ziklag, therefore hath Ziklag been to the kings of Judah till this day.
Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
7 And the number of the days which David hath dwelt in the field of the Philistines [is] days and four months;
Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
8 and David goeth up and his men, and they push unto the Geshurite, and the Gerizite, and the Amalekite, (for they are inhabitants of the land from of old), as thou comest in to Shur and unto the land of Egypt,
Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
9 and David hath smitten the land, and doth not keep alive man and woman, and hath taken sheep, and oxen, and asses, and camels, and garments, and turneth back, and cometh in unto Achish.
Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
10 And Achish saith, 'Whither have ye pushed to-day?' and David saith, 'Against the south of Judah, and against the south of the Jerahmeelite, and unto the south of the Kenite.'
Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
11 Neither man nor woman doth David keep alive, to bring in [word] to Gath, saying, 'Lest they declare [it] against us, saying, Thus hath David done, and thus [is] his custom all the days that he hath dwelt in the fields of the Philistines.'
Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
12 And Achish believeth in David, saying, 'He hath made himself utterly abhorred among his people, in Israel, and hath been to me for a servant age-during.'
Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”

< 1 Samuel 27 >