< 1 Samuel 18 >
1 And it cometh to pass, when he finisheth to speak unto Saul, that the soul of Jonathan hath been bound to the soul of David, and Jonathan loveth him as his own soul.
Davide atatha kuyankhula ndi Sauli, mtima wa Yonatani unagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo iye ankamukonda Davide monga momwe ankadzikondera yekha.
2 And Saul taketh him on that day, and hath not permitted him to turn back to the house of his father.
Choncho Sauli anamusunga Davideyo kuyambira tsiku limenelo ndipo sanamulole kuti abwerere ku nyumba ya abambo ake.
3 And Jonathan maketh — also David — a covenant, because he loveth him as his own soul,
Ndipo Yonatani anapanga pangano ndi Davide chifukwa ankamukonda monga momwe ankadzikondera.
4 and Jonathan strippeth himself of the upper robe which [is] upon him, and giveth it to David, and his long robe, even unto his sword, and unto his bow, and unto his girdle.
Yonatani anavula mkanjo umene anavala ndipo anamupatsa Davide pamodzi ndi zovala za nkhondo, lupanga, uta ndi lamba.
5 And David goeth out whithersoever Saul doth send him; he acted wisely, and Saul setteth him over the men of war, and it is good in the eyes of all the people, and also in the eyes of the servants of Saul.
Davide ankapita kulikonse kumene Sauli ankamutuma kuti apite kukamenya nkhondo, ndipo ankapambana. Choncho Sauli anamupatsa udindo woyangʼanira gulu lankhondo. Ichi chinakondweretsa anthu onse ngakhalenso atsogoleri a nkhondo a Sauli.
6 And it cometh to pass, in their coming in, in David's returning from smiting the Philistine, that the women come out from all the cities of Israel to sing — also the dancers — to meet Saul the king, with tabrets, with joy, and with three-stringed instruments;
Anthu akubwerera kwawo Davide atapha Mfilisiti uja, amayi anatuluka mʼmizinda yonse ya Israeli, akuyimba ndi kuvina kukachingamira mfumu Sauli. Ankayimba ndi kuvina mokondwa, kwinaku ngʼoma ndi zitoliro zikulira.
7 and the women answer — those playing, and say, 'Saul hath smitten among his thousands, And David among his myriads.'
Amayiwo ankalandizana nyimbo mokondwera namati: “Sauli wapha 1,000, Koma Davide wapha miyandamiyanda.”
8 And it is displeasing to Saul exceedingly, and this thing is evil in his eyes, and he saith, 'They have given to David myriads, and to me they have given the thousands, and more to him [is] only the kingdom;'
Koma Sauli anapsa mtima kwambiri ndipo mawu amenewa anamuyipira. Iye anati, “Iwo amuwerengera Davide miyandamiyanda, koma ine 1,000 okha. Nanga chatsalanso nʼchiyani kuti atenge? Si ufumu basi?”
9 and Saul is eyeing David from that day and thenceforth.
Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.
10 And it cometh to pass, on the morrow, that the spirit of sadness [from] God prospereth over Saul, and he prophesieth in the midst of the house, and David is playing with his hand, as day by day, and the javelin [is] in the hand of Saul,
Mmawa mwake mzimu woyipa uja unabwera mwamphamvu pa Sauli. Sauli anayamba kubwebweta mʼnyumba mwake. Davide ankamuyimbira zeze monga nthawi zonse. Sauli anali ndi mkondo mʼdzanja lake.
11 and Saul casteth the javelin, and saith, 'I smite through David, even through the wall;' and David turneth round out of his presence twice.
Tsono anawuponya mkondowo, namati mu mtima mwake, “Ndimubaya Davide ndi kumukhomera ku khoma.” Koma Davide anawulewa kawiri konse.
12 And Saul is afraid of the presence of David, for Jehovah hath been with him, and from Saul He hath turned aside;
Pambuyo pake Sauli amamuopa Davide chifukwa Yehova anali ndi Davideyo, nʼkumusiya Sauli.
13 and Saul turneth him aside from him, and appointeth him to himself head of a thousand, and he goeth out an cometh in, before the people.
Kotero Sauli anamuchotsa Davide pamaso pake ndi kumuyika kukhala mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Choncho Davide ankapita ndi kubwera akutsogolera ankhondowa.
14 And David is in all his ways acting wisely, and Jehovah [is] with him,
Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye.
15 and Saul seeth that he is acting very wisely, and is afraid of him,
Sauli ataona momwe Davide ankapambanira, iye anamuopa kwambiri.
16 and all Israel and Judah love David when he is going out and coming in before them.
Koma Aisraeli onse ndi anthu a Yuda ankamukonda Davide chifukwa ankawatsogolera pa nkhondo zawo.
17 And Saul saith unto David, 'Lo, my elder daughter Merab — her I give to thee for a wife; only, be to me for a son of valour, and fight the battles of Jehovah;' and Saul said, 'Let not my hand be on him, but let the hand of the Philistines be upon him.'
Tsiku lina Sauli anawuza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkazi wamkulu. Ine ndakupatsa kuti umukwatire. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Yehova.” Poteropo Sauli ankanena kuti, “Ndisamuphe ndi manja angawa koma aphedwe ndi Afilisti!”
18 And David saith unto Saul, 'Who [am] I? and what my life — the family of my father in Israel — that I am son-in-law to the king?'
Ndipo Davide anati kwa Sauli, “Ine ndine yani, ndipo abale anga kapena banja la abambo anga ndife yani mʼdziko la Israeli kuti ndikhale mpongozi wa mfumu?”
19 And it cometh to pass, at the time of the giving of Merab daughter of Saul to David, that she hath been given to Adriel the Meholathite for a wife.
Koma pa nthawi yoti Merabi mwana wa Sauli akwatiwe ndi Davide, Sauli anamupereka kwa Adrieli wa ku Mehola kuti amukwatire.
20 And Michal daughter of Saul loveth David, and they declare to Saul, and the thing is right in his eyes,
Koma Mikala mwana wamkazi wa Sauli anamukonda Davide ndipo Sauli atamva za zimenezi, anakondwera.
21 and Saul saith, 'I give her to him, and she is to him for a snare, and the hand of the Philistines is on him;' and Saul saith unto David, 'By the second — thou dost become my son-in-law to-day.'
Sauli ankaganiza kuti, “Ndimupatse amukwatire kuti akhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo adzaphedwe ndi Afilisti.” Choncho Sauli anawuza Davide kachiwiri, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”
22 And Saul commandeth his servants, 'Speak unto David gently, saying, Lo, the king hath delighted in thee, and all his servants have loved thee, and now, be son-in-law to the king.'
Sauli analamulanso nduna zake kuti, “Muyankhuleni Davide mwamseri ndi kumuwuza kuti, ‘Taona, mfumu imakondwera nawe, ndipo nduna zake zonse zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’”
23 And the servants of Saul speak in the ears of David these words, and David saith, 'Is it a light thing in your eyes to be son-in-law to the king — and I a poor man, and lightly esteemed?'
Iwo anakamuwuza Davide mawu amenewa, koma Davide anati, “Kodi inu mukuganiza kuti ndi chinthu chapafupi kukhala mpongozi wa mfumu? Ine ndine wosauka ndiponso wosatchuka.”
24 And the servants of Saul declare to him, saying, 'According to these words hath David spoken.'
Nduna za Sauli zinamuwuza zonse zimene anayankha Davide.
25 And Saul saith, 'Thus do ye say to David, There is no delight to the king in dowry, but in a hundred foreskins of the Philistines — to be avenged on the enemies of the king;' and Saul thought to cause David to fall by the hand of the Philistines.
Sauli anayankha kuti, “Kamuwuzeni Davide kuti, ‘Mfumu sikufuna malowolo a mtundu wina uliwonse koma timakungu ta msonga za mavalo a Afilisti 100 kuti ilipsire adani ake.’” Maganizo a Sauli anali akuti Davide aphedwe ndi Afilisti.
26 And his servants declare to David these words, and the thing is right in the eyes of David, to be son-in-law to the king; and the days have not been full,
Nduna za Saulizo zitamuwuza Davide zimenezi, anakondwera kuti akhale mpongozi wa mfumu. Koma nthawi imene anapatsidwa isanathe,
27 and David riseth and goeth, he and his men, and smiteth among the Philistines two hundred men, and David bringeth in their foreskins, and they set them before the king, to be son-in-law to the king; and Saul giveth to him Michal his daughter for a wife.
Davide ndi anyamata ake anapita ndi kukapha Afilisti 200. Iye anabwera ndi timakungu tija natipereka tonse kwa mfumu kuti akhale mpongozi wa mfumu. Kotero Sauli anapereka mwana wake wamkazi, Mikala, kwa Davide kuti amukwatire.
28 And Saul seeth and knoweth that Jehovah [is] with David, and Michal daughter of Saul hath loved him,
Sauli atazindikira kuti Yehova anali ndi Davide ndiponso kuti mwana wake Mikala amamukonda Davide,
29 and Saul addeth to be afraid of the presence of David yet; and Saul is an enemy with David all the days.
iye anapitirirabe kumuopa Davide ndi kumadana naye moyo wake wonse.
30 And the princes of the Philistines come out, and it cometh to pass from the time of their coming out, David hath acted more wisely than any of the servants of Saul, and his name is very precious.
Nthawi zonse pamene atsogoleri a Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, Davide ankapambana kuposa nduna zonse za Sauli. Choncho dzina lake linatchuka kwambiri.