< 1 Kings 14 >

1 At that time was Abijah son of Jeroboam sick,
Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
2 and Jeroboam saith to his wife, 'Rise, I pray thee, and change thyself, and they know not that thou [art] wife of Jeroboam, and thou hast gone to Shiloh; lo, there [is] Ahijah the prophet; he spake unto me of [being] king over this people;
ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
3 and thou hast taken in thy hand ten loaves, and crumbs, and a bottle of honey, and hast gone in unto him; he doth declare to thee what becometh of the youth.'
Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
4 And the wife of Jeroboam doth so, and riseth, and goeth to Shiloh, and entereth the house of Ahijah, and Ahijah is not able to see, for his eyes have stood because of his age.
Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
5 And Jehovah said unto Ahijah, 'Lo, the wife of Jeroboam is coming to seek a word from thee concerning her son, for he is sick; thus and thus thou dost speak unto her, and it cometh to pass at her coming in, that she is making herself strange.'
Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
6 And it cometh to pass, at Ahijah's hearing the sound of her feet [as] she came in to the opening, that he saith, 'Come in, wife of Jeroboam, why is this — thou art making thyself strange? and I am sent unto thee [with] a sharp thing:
Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
7 Go, say to Jeroboam, Thus said Jehovah, God of Israel, Because that I have made thee high out of the midst of the people, and appoint thee leader over my people Israel,
Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
8 and rend the kingdom from the house of David, and give it to thee, — and thou hast not been as My servant David who kept My commands, and who walked after Me with all his heart, to do only that which [is] right in Mine eyes,
Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
9 and thou dost evil above all who have been before thee, and goest, and makest to thee other gods and molten images to provoke Me to anger, and Me thou hast cast behind thy back:
Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
10 'Therefore, lo, I am bringing in evil unto the house of Jeroboam, and have cut off to Jeroboam those sitting on the wall — shut up and left — in Israel, and have put away the posterity of the house of Jeroboam, as one putteth away the dung till its consumption;
“‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
11 him who dieth of Jeroboam in a city do the dogs eat, and him who dieth in a field do fowl of the heavens eat, for Jehovah hath spoken.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
12 'And thou, rise, go to thy house; in the going in of thy feet to the city — hath the lad died;
“Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
13 and all Israel have mourned for him, and buried him, for this one — by himself — cometh of Jeroboam unto a grave, because there hath been found in him a good thing towards Jehovah, God of Israel, in the house of Jeroboam.
Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
14 'And Jehovah hath raised up for Him a king over Israel who cutteth off the house of Jeroboam this day — and what? — even now!
“Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
15 And Jehovah hath smitten Israel as the reed is moved by the waters, and hath plucked Israel from off this good ground that He gave to their fathers, and scattered them beyond the River, because that they made their shrines, provoking Jehovah to anger;
Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
16 and He giveth up Israel because of the sins of Jeroboam that he sinned, and that he caused Israel to sin.'
Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
17 And the wife of Jeroboam riseth, and goeth, and cometh to Tirzah; she hath come in to the threshold of the house, and the youth dieth;
Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
18 and they bury him, and mourn for him do all Israel, according to the word of Jehovah, that he spake by the hand of His servant Ahijah the prophet.
Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
19 And the rest of the matters of Jeroboam, how he fought, and how he reigned, lo, they are written on the book of the Chronicles of the kings of Israel.
Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
20 And the days that Jeroboam reigned [are] twenty and two years, and he lieth with his fathers, and reign doth Nadab his son in his stead.
Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
21 And Rehoboam son of Solomon hath reigned in Judah; a son of forty and one years [is] Rehoboam in his reigning, and seventeen years he hath reigned in Jerusalem, the city that Jehovah chose to set His name there, out of all the tribes of Israel, and the name of his mother [is] Naamah the Ammonitess.
Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
22 And Judah doth the evil thing in the eyes of Jehovah, and they make Him zealous above all that their fathers did by their sins that they have sinned.
Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
23 And they build — also they — for themselves high places, and standing-pillars, and shrines, on every high height, and under every green tree;
Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
24 and also a whoremonger hath been in the land; they have done according to all the abominations of the nations that Jehovah dispossessed from the presence of the sons of Israel.
Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
25 And it cometh to pass, in the fifth year of king Rehoboam, gone up hath Shishak king of Egypt against Jerusalem,
Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
26 and he taketh the treasures of the house of Jehovah, and the treasures of the house of the king, yea, the whole he hath taken; and he taketh all the shields of gold that Solomon made.
Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
27 And king Rehoboam maketh in their stead shields of brass, and hath made [them] a charge on the hand of the heads of the runners, those keeping the opening of the house of the king,
Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
28 and it cometh to pass, from the going in of the king to the house of Jehovah, the runners bear them, and have brought them back unto the chamber of the runners.
Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
29 And the rest of the matters of Rehoboam, and all that he did, are they not written on the book of the Chronicles of the kings of Judah?
Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
30 And war hath been between Rehoboam and Jeroboam all the days;
Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
31 and Rehoboam lieth with his fathers, and is buried with his fathers, in the city of David, and the name of his mother [is] Naamah the Ammonitess, and reign doth Abijam his son in his stead.
Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.

< 1 Kings 14 >