< 1 Kings 13 >

1 And lo, a man of God hath come from Judah, by the word of Jehovah, unto Beth-El, and Jeroboam is standing by the altar — to make perfume;
Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
2 and he calleth against the altar, by the word of Jehovah, and saith, 'Altar! altar! thus said Jehovah, Lo, a son is born to the house of David — Josiah his name — and he hath sacrificed on thee the priests of the high places who are making perfume on thee, and bones of man are burnt on thee.'
Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
3 And he hath given on that day a sign, saying, 'This [is] the sign that Jehovah hath spoken, Lo, the altar is rent, and the ashes poured forth that [are] on it.'
Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
4 And it cometh to pass, at the king's hearing the word of the man of God that he calleth against the altar in Beth-El, that Jeroboam putteth forth his hand from off the altar, saying, 'Catch him;' and his hand is dried up that he hath put forth against him, and he is not able to bring it back unto him,
Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
5 and the altar is rent, and the ashes poured forth from the altar, according to the sign that the man of God had given by the word of Jehovah.
Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
6 And the king answereth and saith unto the man of God, 'Appease, I pray thee, the face of Jehovah thy God, and pray for me, and my hand doth come back unto me;' and the man of God appeaseth the face of Jehovah, and the hand of the king cometh back unto him, and it is as at the beginning.
Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
7 And the king speaketh unto the man of God, 'Come in with me to the house, and refresh thyself, and I give to thee a gift.'
Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
8 And the man of God saith unto the king, 'If thou dost give to me the half of thine house, I do not go in with thee, nor do I eat bread, nor do I drink water, in this place;
Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
9 for so He commanded me by the word of Jehovah, saying, Thou dost not eat bread nor drink water, nor turn back in the way that thou hast come.'
Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
10 And he goeth on in another way, and hath not turned back in the way in which he came in unto Beth-El.
Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
11 And a certain aged prophet is dwelling in Beth-El, and his son cometh and recounteth to him all the deed that the man of God hath done to-day in Beth-El, the words that he hath spoken unto the king, — yea, they recount them to their father.
Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
12 And their father saith unto them, 'Where [is] this — the way he hath gone?' and his sons see the way that the man of God hath gone who came from Judah.
Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
13 And he saith unto his sons, 'Saddle for me the ass,' and they saddle for him the ass, and he rideth on it,
Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
14 and goeth after the man of God, and findeth him sitting under the oak, and saith unto him, 'Art thou the man of God who hast come from Judah?' and he saith, 'I [am].'
ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
15 And he saith unto him, 'Come with me to the house, and eat bread.'
Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
16 And he saith, 'I am not able to turn back with thee, and to go in with thee, nor do I eat bread or drink with thee water in this place,
Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
17 for a word [is] unto me by the word of Jehovah, Thou dost not eat bread nor drink there water, thou dost not turn back to go in the way in which thou camest.'
Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
18 And he saith to him, 'I also [am] a prophet like thee, and a messenger spake unto me by the word of Jehovah, saying, Bring him back with thee unto thy house, and he doth eat bread and drink water;' — he hath lied to him.
Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
19 And he turneth back with him, and eateth bread in his house, and drinketh water.
Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
20 And it cometh to pass — they are sitting at the table — and a word of Jehovah is unto the prophet who brought him back,
Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
21 and he calleth unto the man of God who came from Judah, saying, 'Thus said Jehovah, Because that thou hast provoked the mouth of Jehovah, and hast not kept the command that Jehovah thy God charged thee,
Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
22 and turnest back and dost eat bread and drink water in the place of which He said unto thee, Thou dost not eat bread nor drink water — thy carcase cometh not in unto the burying-place of thy fathers.'
Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
23 And it cometh to pass, after his eating bread, and after his drinking, that he saddleth for him the ass, for the prophet whom he had brought back,
Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
24 and he goeth, and a lion findeth him in the way, and putteth him to death, and his carcase is cast in the way, and the ass is standing near it, and the lion is standing near the carcase.
Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
25 And lo, men are passing by, and see the carcase cast in the way, and the lion standing near the carcase, and they come and speak [of it] in the city in which the old prophet is dwelling.
Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
26 And the prophet who brought him back out of the way heareth and saith, 'It [is] the man of God who provoked the mouth of Jehovah, and Jehovah giveth him to the lion, and it destroyeth him, and putteth him to death, according to the word of Jehovah that he spake to him.'
Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
27 And he speaketh unto his sons saying, 'Saddle for me the ass,' and they saddle [it].
Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
28 And he goeth and findeth his carcase cast in the way, and the ass and the lion are standing near the carcase — the lion hath not eaten the carcase nor destroyed the ass.
Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
29 And the prophet taketh up the carcase of the man of God, and placeth it on the ass, and bringeth it back, and the old prophet cometh in unto the city to mourn and to bury him,
Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
30 and he placeth his carcase in his own grave, and they mourn for him, 'Oh, my brother!'
Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
31 And it cometh to pass, after his burying him, that he speaketh unto his sons, saying, 'At my death — ye have buried me in the burying-place in which the man of God is buried; near his bones place my bones;
Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
32 for the word certainly cometh to pass that he called by the word of Jehovah concerning the altar which [is] Beth-El, and concerning all the houses of the high places that [are] in cities of Samaria.'
Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
33 After this thing Jeroboam hath not turned from his evil way, and turneth back, and maketh of the extremities of the people priests of high places; he who is desirous he consecrateth his hand, and he is of the priests of the high places.
Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
34 And in this thing is the sin of the house of Jeroboam, even to cut [it] off, and to destroy [it] from off the face of the ground.
Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.

< 1 Kings 13 >