< 1 Chronicles 5 >

1 As to sons of Reuben, first-born of Israel — for he [is] the first-born, and on account of his profaning the couch of his father hath his birthright been given to the sons of Joseph son of Israel, and [he is] not to be reckoned by genealogy for the birthright,
Ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli (iye anali woyamba kubadwa, koma atagona ndi mkazi wamngʼono wa abambo ake, ulemu wake wokhala mwana woyamba unaperekedwa kwa ana a Yosefe. Kotero iye sanalembedwe pa mndandanda wa mayina ngati mwana woyamba kubadwa,
2 for Judah hath been mighty over his brother, and for leader above him, and the birthright [is] to Joseph.
ndipo ngakhalenso Yuda anali wamphamvu kwambiri pakati pa abale ake, ndi kuti wolamulira anachokera mwa iye, ulemu wa mwana woyamba kubadwa unaperekedwa kwa Yosefe)
3 Sons of Reuben, first-born of Israel: Hanoch, and Pallu, Hezron, and Carmi.
ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli ndi awa: Hanoki, Palu, Hezironi, ndi Karimi.
4 Sons of Joel: Shemaiah his son, Gog his son, Shimei his son,
Ana a Yoweli anali awa: Semaya, Gogi, Simei,
5 Micah his son, Reaiah his son, Baal his son,
Mika, Reaya, Baala,
6 Beerah his son, whom Tilgath-Pilneser king of Asshur removed; he [is] prince of the Reubenite.
ndiponso Beeri, amene Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri anamugwira ukapolo. Mtsogoleri wa fuko la Rubeni anali Beeri.
7 And his brethren, by their families, in the genealogy of their generations, [are] heads: Jeiel, and Zechariah,
Abale awo mwa mabanja awo, potsata mndandanda wa mʼbado wawo, ndi awa: Yeiyeli, mtsogoleri, Zekariya,
8 and Bela son of Azaz, son of Shema, son of Joel — he is dwelling in Aroer, even unto Nebo and Baal-Meon;
ndiponso Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoweli. Iwo ankakhala ku Aroeri mpaka ku Nebo ndi Baala-Meoni.
9 and at the east he dwelt even unto the entering in of the wilderness, even from the river Phrat, for their cattle were multiplied in the land of Gilead.
Iwo anakhala cha kummawa mpaka kukafika polowera mʼchipululu cha mbali ina ya Mtsinje wa Yufurate, chifukwa ziweto zawo zinaswana kwambiri mʼdziko la Giliyadi.
10 And in the days of Saul they have made war with the Hagarites, who fall by their hand, and they dwell in their tents over all the face of the east of Gilead.
Pa nthawi ya Sauli anachita nkhondo ndi Ahagiri ndi kuwagonjetsa. Tsono iwo anakhala mʼmatenti a Ahagiri ku dera lonse la kummawa kwa Giliyadi.
11 And the sons of Gad, over-against them have dwelt in the land of Bashan unto Salcah,
Anthu a fuko la Gadi anakhala moyandikana ndi fuko la Rubeni ku Basani mpaka ku Saleka:
12 Joel the head, and Shapham the second, and Jaanai and Shaphat in Bashan;
Mtsogoleri wawo ku Basani anali Yoweli, wachiwiri anali Safamu, kenaka Yanayi ndi Safati.
13 and their brethren of the house of their fathers [are] Michael, and Meshullam, and Sheba, and Jorai, and Jachan, and Zia, and Heber, seven.
Abale awo mwa mabanja awo anali awa: Mikayeli, Mesulamu, Seba, Yorayi, Yakani, Ziya ndi Eberi, onse ali asanu ndi awiri.
14 These [are] sons of Abihail son of Huri, son of Jaroah, son of Gilead, son of Michael, son of Jeshishai, son of Jahdo, son of Buz;
Amenewa ndiwo anali ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Giliyadi, mwana wa Mikayeli, mwana wa Yesisayi, mwana wa Yahido, mwana wa Buzi.
15 Ahi son of Abdiel, son of Guni, [is] head of the house of their fathers;
Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, anali mtsogoleri wa banja la makolo awo.
16 and they dwell in Gilead in Bashan, and in her small towns, and in all suburbs of Sharon, upon their outskirts;
Fuko la Gadi linakhala ku Giliyadi, ku Basani ndi midzi yozugulira, madera onse a msipu a ku Saroni mpaka kumene amalekezera.
17 all of them reckoned themselves by genealogy in the days of Jotham king of Judah, and in the days of Jeroboam king of Israel.
Mayina onsewa analembedwa potsata mndandanda wa mibado yawo pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu mfumu ya Yuda ndi Yeroboamu mfumu ya Israeli.
18 Sons of Reuben, and the Gadite, and the half of the tribe of Manasseh, of sons of valour, men bearing shield and sword, and treading bow, and taught in battle, [are] forty and four thousand and seven hundred and sixty, going out to the host.
Mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la Manase, anali ndi anthu 44, 760 okonzeka kulowa usilikali; anthu amatupi amphamvu, amene amatha kugwiritsa ntchito chishango ndi lupanga, amene amatha kugwiritsa ntchito uta, amene anaphunzitsidwa kumenya nkhondo.
19 And they make war with the Hagarites, and Jetur, and Naphish, and Nodab,
Iwo anachita nkhondo ndi Ahagiri, Yeturi, Nafisi ndi Nodabu.
20 and they are helped against them, and the Hagarites are given into their hand, and all who [are] with them, for they cried to God in battle, and He was entreated of them, because they trusted in Him.
Iwowo anathandizidwa polimbana nawo ndipo Mulungu anapereka Ahagiri mʼmanja mwawo; popeza iwo anafuwulira kwa Mulungu pa nkhondopo. Iye anayankha mapemphero awo chifukwa anamudalira.
21 And they take captive their cattle, of their camels fifty thousand, and of sheep two hundred and fifty thousand, and of asses two thousand, and of human beings a hundred thousand;
Choncho iwo analanda ziweto za Ahagiri: ngamira 50,000, nkhosa ndi mbuzi 250,000 ndi abulu 2,000. Ndiponso anagwira akapolo 100,000,
22 for many have fallen pierced, for of God [is] the battle; and they dwell in their stead till the removal.
enanso ambiri anaphedwa, chifukwa nkhondoyo inali ya Mulungu. Ndipo iwo anakhala mʼdzikomo mpaka pa nthawi ya ukapolo.
23 And the sons of the half of the tribe of Manasseh dwelt in the land, from Bashan unto Baal-Hermon, and Senir, and mount Hermon, they have multiplied.
Theka la fuko la Manase linkakhala ku dziko la kummawa kuyambira ku Basani mpaka ku Baala-Herimoni, kumene ndi ku Seniri (Phiri la Herimoni) ndipo anthuwo anali ochuluka kwambiri.
24 And these [are] heads of the house of their fathers, even Epher, and Ishi, and Eliel, and Azriel, and Jeremiah, and Hodaviah, and Jahdiel, men mighty in valour, men of name, heads to the house of their fathers.
Atsogoleri a mabanja awo anali awa: Eferi, Isi, Elieli, Azirieli, Yeremiya, Hodaviya ndi Yahidieli. Iwo anali asilikali olimba mtima, anthu otchuka, ndiponso atsogoleri a mabanja awo.
25 And they trespass against the God of their fathers, and go a-whoring after the gods of the peoples of the land whom God destroyed from their presence;
Koma iwo anali osakhulupirika kwa Mulungu wa makolo awo ndipo anadzipereka okha kwa milungu ya anthu okhala mʼdzikomo amene Mulungu anawawononga pamene iwowo ankafika.
26 and stir up doth the God of Israel the spirit of Pul king of Asshur, and the spirit of Tilgath-Pilneser king of Asshur, and he removeth them — even the Reubenite, and the Gadite, and the half of the tribe of Manasseh — and bringeth them in to Halah, and Habor, and Hara, and the river of Gozan unto this day.
Kotero Mulungu wa Israeli anayika mkwiyo mwa Puli mfumu ya Asuri (ameneyu ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri) amene anatenga fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase kupita nawo ku ukapolo. Iye anapita nawo ku Hala, Habori, Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, kumene ali mpaka lero lino.

< 1 Chronicles 5 >