< Song of Solomon 4 >

1 Mi frendesse, thou art ful fair; thin iyen ben of culueris, with outen that that is hid with ynne; thin heeris ben as the flockis of geete, that stieden fro the hil of Galaad.
Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga! Ndithudi, ndiwe wokongola! Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
2 Thi teeth ben as the flockis of clippid sheep, that stieden fro waischyng; alle ben with double lambren, and no bareyn is among tho.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene, zochokera kozisambitsa kumene. Iliyonse ili ndi ana amapasa; palibe imene ili yokha.
3 Thi lippis ben as a reed lace, and thi speche is swete; as the relif of an appil of Punyk, so ben thi chekis, with outen that, that is hid with ynne.
Milomo yako ili ngati mbota yofiira; pakamwa pako ndi pokongola kwambiri. Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
4 Thi necke is as the tour of Dauid, which is bildid with strengthis maad bifore for defense; a thousynde scheldis hangen on it, al armure of stronge men.
Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide, yomangidwa bwino ndi yosalala; pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000, zishango zonsezo za anthu ankhondo.
5 Thi twei tetis ben as twey kidis, twynnes of a capret, that ben fed in lilies,
Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala, ngati ana amapasa a nswala amene akudya pakati pa maluwa okongola.
6 til the dai sprynge, and shadewis ben bowid doun. Y schal go to the mounteyn of myrre, and to the litil hil of encense.
Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira ndipo mithunzi ikayamba kuthawa, ndidzapita ku phiri la mure ndi ku chitunda cha lubani.
7 My frendesse, thou art al faire, and no wem is in thee.
Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga; palibe chilema pa iwe.
8 My spousesse, come thou fro the Liban; come thou fro the Liban, come thou; thou schalt be corowned fro the heed of Amana, fro the cop of Sanyr and Hermon, fro the dennys of liouns, fro the hillis of pardis.
Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga, tiye tichoke ku Lebanoni, utsikepo pa msonga ya Amana, kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni, kuchoka ku mapanga a mikango ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
9 My sister spousesse, thou hast woundid myn herte; thou hast woundid myn herte, in oon of thin iyen, and in oon heer of thi necke.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima, iwe wanditenga mtima ndi kapenyedwe ka maso ako, ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
10 My sistir spousesse, thi tetis ben ful faire; thi tetis ben feirere than wyn, and the odour of thi clothis is aboue alle swete smellynge oynementis.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa! Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo, ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
11 Spousesse, thi lippis ben an hony coomb droppynge; hony and mylk ben vndur thi tunge, and the odour of thi clothis is as the odour of encence.
Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi; pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi. Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
12 Mi sister spousesse, a gardyn closid togidere; a gardyn closid togidere, a welle aseelid.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa; ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
13 Thi sendingis out ben paradis of applis of Punyk, with the fruytis of applis, cipre trees, with narde;
Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza; muli zipatso zokoma kwambiri, muli hena ndi nadi,
14 narde, and saffrun, an erbe clepid fistula, and canel, with alle trees of the Liban, myrre, and aloes, with alle the beste oynementis.
nadi ndi safiro, kalamusi ndi sinamoni, komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino. Mulinso mure ndi aloe ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
15 A welle of gardyns, a pit of wallynge watris, that flowen with fersnesse fro the Liban.
Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda, chitsime cha madzi oyenda, mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
16 Rise thou north wynd, and come thou, south wynd; blowe thou thorouy my gardyn, and the swete smellynge oynementis therof schulen flete.
Dzuka, iwe mphepo yakumpoto, ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera! Uzira pa munda wanga, kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse. Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.

< Song of Solomon 4 >