< Psalms 75 >

1 `To the ouercomere; leese thou not the salm of the song of Asaph. God, we schulen knouleche to thee, `we schulen knouleche; and we schulen inwardli clepe thi name.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 We schulen telle thi merueilis; whanne Y schal take tyme, Y schal deme riytfulnesses.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 The erthe is meltid, and alle that duellen ther ynne; Y confermede the pileris therof.
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 I seide to wickid men, Nyle ye do wickidli; and to trespassouris, Nyle ye enhaunce the horn.
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Nyle ye reise an hiy youre horn; nyle ye speke wickidnesse ayens God.
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 For nether fro the eest, nethir fro the west, nethir fro desert hillis; for God is the iuge.
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 He mekith this man, and enhaunsith hym; for a cuppe of cleene wyn ful of meddling is in the hoond of the Lord.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 And he bowide of this in to that; netheles the drast therof is not anyntischid; alle synneris of erthe schulen drinke therof.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 Forsothe Y schal telle in to the world; Y schal synge to God of Jacob.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 And Y schal breke alle the hornes of synneris; and the hornes of the iust man schulen be enhaunsid.
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

< Psalms 75 >