< Psalms 6 >
1 To the ouercomere in salmes, the salm of Dauid, `on the eiythe. Lord, repreue thou not me in thi stronge veniaunce; nether chastice thou me in thin ire.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Lord, haue thou merci on me, for Y am sijk; Lord, make thou me hool, for alle my boonys ben troblid.
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 And my soule is troblid greetli; but thou, Lord, hou long?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Lord, be thou conuertid, and delyuere my soule; make thou me saaf, for thi merci.
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 For noon is in deeth, which is myndful of thee; but in helle who schal knouleche to thee? (Sheol )
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
6 I traueilide in my weilyng, Y schal waische my bed bi ech nyyt; Y schal moiste, `ether make weet, my bedstre with my teeris.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 Myn iye is disturblid of woodnesse; Y waxe eld among alle myn enemyes.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Alle ye that worchen wickidnesse, departe fro me; for the Lord hath herd the vois of my wepyng.
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 The Lord hath herd my bisechyng; the Lord hath resseyued my preier.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 Alle my enemyes be aschamed, and be disturblid greetli; be thei turned togidere, and be thei aschamed ful swiftli.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.