< Psalms 48 >

1 The song of salm, of the sones of Chore. The Lord is greet, and worthi to be preisid ful myche; in the citee of oure God, in the hooli hil of hym.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 It is foundid in the ful out ioiyng of al erthe; the hil of Syon; the sidis of the north, the citee of the greet kyng.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 God schal be knowun in the housis therof; whanne he schal take it.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 For lo! the kyngis of erthe weren gaderid togidere; thei camen into o place.
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 Thei seynge so wondriden; thei weren disturblid, thei weren mouyd togidere, tremblyng took hem.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 There sorewis as of a womman trauelynge of child;
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 in a greet spirit thou schalt al to-breke the schippis of Tharsis.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 As we herden, so we sien, in the citee of the Lord of vertues, in the citee of oure God; God hath foundid that citee with outen ende.
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 God, we han resseyued thi mercy; in the myddis of thi temple.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 Aftir thi name, God, so thin heriyng is spred abrood in to the endis of erthe; thi riyt hond is ful of riytfulnesse.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 The hil of Sion be glad, and the douytris of Judee be fulli ioiful; for thi domes, Lord.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Cumpasse ye Syon, and biclippe ye it; telle ye in the touris therof.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Sette ye youre hertis in the vertu of him; and departe ye the housis of hym, that ye telle out in an other generacioun.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 For this is God, oure God, in to withouten ende, and in to the world of world; he schal gouerne vs in to worldis.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

< Psalms 48 >