< Psalms 47 >

1 To victorie, a salm to the sones of Chore. Alle ye folkis, make ioie with hondis; synge ye hertli to God in the vois of ful out ioiyng.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 For the Lord is hiy and ferdful; a greet kyng on al erthe.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 He made puplis suget to vs; and hethene men vndur oure feet.
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 He chees his eritage to vs; the fairnesse of Jacob, whom he louyde.
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 God stiede in hertli song; and the Lord in the vois of a trumpe.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Synge ye to oure God, synge ye; synge ye to oure kyng, synge ye.
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 For God is kyng of al erthe; synge ye wiseli.
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 God schal regne on hethene men; God sittith on his hooli seete.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 The princes of puplis ben gaderid togidere with God of Abraham; for the stronge goddis of erthe ben reisid greetli.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.

< Psalms 47 >