< Psalms 45 >

1 To the ouercomere for the lilies, the most loued song of lernyng of the sones of Chore. Myn herte hath teld out a good word; Y seie my workis `to the kyng. Mi tunge is `a penne of a writere; writynge swiftli.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Crist, thou art fairer in schap than the sones of men; grace is spred abrood in thi lippis; therfor God blessid thee withouten ende.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Be thou gird with thi swerd; on thi hipe most myytili.
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 Biholde thou in thi schaplynesse and thi fairnesse; come thou forth with prosperite, and regne thou. For treuthe, and myldenesse, and riytfulnesse; and thi riyt hond schal lede forth thee wondurfuli.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Thi scharpe arowis schulen falle in to the hertis of the enemyes of the kyng; puplis schulen be vndur thee.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 God, thi seete is in to the world of world; the yerde of thi rewme is a yerde of riyt reulyng, `ethir of equite.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Thou louedist riytfulnesse, and hatidist wickidnesse; therfor thou, God, thi God, anoyntide thee with the oile of gladnesse, more than thi felowis.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 Mirre, and gumme, and cassia, of thi clothis, of the `housis yuer;
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 of whiche the douytris of kyngis delitiden thee. A queen stood nyy on thi riyt side in clothing ouergildid; cumpassid with dyuersitee.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Douyter, here thou, and se, and bowe doun thin eere; and foryete thi puple, and the hows of thi fadir.
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 And the kyng schal coueyte thi fairnesse; for he is thi Lord God, and thei schulen worschipe hym.
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 And the douytris of Tire in yiftis; alle the riche men of the puple schulen biseche thi cheer.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 Al the glorye of that douyter of the kyng is with ynne in goldun hemmes;
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 sche is clothid aboute with dyuersitees. Virgyns schulen be brouyt to the kyng aftir hir; hir neiyboressis schulen be brouyt to thee.
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 Thei schulen be brouyt in gladnesse, and ful out ioiyng; thei schulen be brouyt in to the temple of the kyng.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Sones ben borun to thee, for thi fadris; thou schalt ordeyne hem princes on al erthe.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Lord, thei schulen be myndeful of thi name; in ech generacioun, and in to generacioun. Therfor puplis schulen knouleche to thee withouten ende; and in to the world of world.
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

< Psalms 45 >