< Psalms 44 >

1 `To victorie, lernyng to the sones of Chore. God, we herden with oure eeris; oure fadris telden to vs. The werk, which thou wrouytist in the daies of hem; and in elde daies.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Thin hond lost hethene men, and thou plauntidist hem; thou turmentidist puplis, and castidist hem out.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 For the children of Israel weldiden the lond not bi her swerd; and the arm of hem sauyde not hem. But thi riyt hond, and thin arm, and the liytnyng of thi cheer; for thou were plesid in hem.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Thou art thi silf, my kyng and my God; that sendist helthis to Jacob.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Bi thee we schulen wyndewe oure enemyes with horn; and in thi name we schulen dispise hem, that risen ayen vs.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 For Y schal not hope in my bouwe; and my swerd schal not saue me.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 For thou hast saued vs fro men turmentinge vs; and thou hast schent men hatinge vs.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 We schulen be preisid in God al dai; and in thi name we schulen knouleche to thee in to the world.
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 But now thou hast put vs abac, and hast schent vs; and thou, God, schalt not go out in oure vertues.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Thou hast turned vs awei bihynde aftir oure enemyes; and thei, that hatiden vs, rauyschiden dyuerseli to hem silf.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Thou hast youe vs as scheep of meetis; and among hethene men thou hast scaterid vs.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Thou hast seeld thi puple with out prijs; and multitude was not in the chaungyngis of hem.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Thou hast set vs schenschip to oure neiyboris; mouwyng and scorn to hem that ben in oure cumpas.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Thou hast set vs into licnesse to hethene me; stiryng of heed among puplis.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Al dai my schame is ayens me; and the schenschipe of my face hilide me.
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 Fro the vois of dispisere, and yuele spekere; fro the face of enemy, and pursuere.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Alle these thingis camen on vs, and we han not foryete thee; and we diden not wickidli in thi testament.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 And oure herte yede not awei bihynde; and thou hast bowid awei oure pathis fro thi weie.
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 For thou hast maad vs lowe in the place of turment; and the schadewe of deth hilide vs.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 If we foryaten the name of oure God; and if we helden forth oure hondis to an alien God.
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 Whether God schal not seke these thingis? for he knowith the hid thingis of herte.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 For whi we ben slayn al dai for thee; we ben demed as scheep of sleyng.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Lord, rise vp, whi slepist thou? rise vp, and putte not awei in to the ende.
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Whi turnest thou awei thi face? thou foryetist oure pouert, and oure tribulacioun.
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 For oure lijf is maad low in dust; oure wombe is glued togidere in the erthe.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Lord, rise vp thou, and helpe vs; and ayenbie vs for thi name.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< Psalms 44 >