< Psalms 42 >
1 To victorie, to the sones of Chore. As an hert desirith to the wellis of watris; so thou, God, my soule desirith to thee.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi, kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
2 Mi soule thirstide to God, `that is a `quik welle; whanne schal Y come, and appere bifor the face of God?
Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo. Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
3 Mi teeris weren looues to me bi dai and nyyt; while it is seid to me ech dai, Where is thi God?
Misozi yanga yakhala chakudya changa usana ndi usiku, pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
4 I bithouyte of these thingis, and Y schedde out in me my soule; for Y schal passe in to the place of the wondurful tabernacle, til to the hows of God. In the vois of ful out ioiyng and knoulechyng; is the sown of the etere.
Zinthu izi ndimazikumbukira pamene ndikukhuthula moyo wanga: momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu, kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko pakati pa anthu a pa chikondwerero.
5 Mi soule, whi art thou sory; and whi disturblist thou me? Hope thou in God, for yit Y schal knouleche to hym; he is the helthe of my cheer,
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Yembekezera Mulungu, pakuti ndidzamulambirabe, Mpulumutsi wanga ndi
6 and my God. My soule is disturblid at my silf; therfor, God, Y schal be myndeful of thee fro the lond of Jordan, and fro the litil hil Hermonyim.
Mulungu wanga. Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga kotero ndidzakumbukira Inu kuchokera ku dziko la Yorodani, ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
7 Depthe clepith depthe; in the vois of thi wyndows. Alle thin hiye thingis and thi wawis; passiden ouer me.
Madzi akuya akuyitana madzi akuya mu mkokomo wa mathithi anu; mafunde anu onse obwera mwamphamvu andimiza.
8 The Lord sente his merci in the dai; and his song in the nyyt.
Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake, nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane; pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
9 At me is a preier to the God of my lijf; Y schal seie to God, Thou art my `takere vp. Whi foryetist thou me; and whi go Y sorewful, while the enemy turmentith me?
Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa, “Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?”
10 While my boonys ben brokun togidere; myn enemyes, that troblen me, dispiseden me. While thei seien to me, bi alle daies; Where is thi God?
Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo pamene adani anga akundinyoza, tsiku lonse akunena kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
11 Mi soule, whi art thou sori; and whi disturblist thou me? Hope thou in God, for yit Y schal knouleche to hym; `he is the helthe of my cheer, and my God.
Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.