< Psalms 31 >

1 To victorie, the salm of Dauid. Lord, Y hopide in thee, be Y not schent with outen ende; delyuere thou me in thi riytfulnesse.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Bouwe doun thin eere to me; haaste thou to delyuere me. Be thou to me in to God defendere, and in to an hows of refuyt; that thou make me saaf.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 For thou art my strengthe and my refuyt; and for thi name thou schalt lede me forth, and schalt nurische me.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Thou schalt lede me out of the snare, which thei hidden to me; for thou art my defendere.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 I bitake my spirit in to thin hondis; Lord God of treuthe, thou hast ayen bouyt me.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 Thou hatist hem that kepen vanytees superfluli.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 Forsothe Y hopide in the Lord; Y schal haue fulli ioie, and schal be glad in thi merci. For thou byheldist my mekenesse; thou sauedist my lijf fro nedis.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 And thou closidist not me togidere withynne the hondis of the enemy; thou hast sett my feet in a large place.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 Lord, haue thou merci on me, for Y am troblid; myn iye is troblid in ire, my soule and my wombe `ben troblid.
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 For whi my lijf failide in sorewe; and my yeeris in weilynges. Mi vertu is maad feble in pouert; and my boonys ben disturblid.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 Ouer alle myn enemyes Y am maad schenship greetli to my neiyboris; and drede to my knowun. Thei that sien me with outforth, fledden fro me; Y am youun to foryetyng,
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 as a deed man fro herte. I am maad as a lorun vessel;
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 for Y herde dispisyng of many men dwellynge in cumpas. In that thing the while thei camen togidere ayens me; thei counceliden to take my lijf.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 But, Lord, Y hopide in thee; Y seide, Thou art my God; my tymes ben in thin hondis.
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 Delyuer thou me fro the hondis of mynen enemyes; and fro hem that pursuen me.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Make thou cleer thi face on thi seruaunt; Lord, make thou me saaf in thi merci;
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 be Y not schent, for Y inwardli clepide thee. Unpitouse men be aschamed, and be led forth in to helle; (Sheol h7585)
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
18 gileful lippys be maad doumbe. That speken wickidnesse ayens a iust man; in pride, and in mysusyng.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Lord, the multitude of thi swetnesse is ful greet; which thou hast hid to men dredynge thee. Thou hast maad a perfit thing to hem, that hopen in thee; in the siyt of the sones of men.
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Thou schalt hide hem in the priuyte of thi face; fro disturblyng of men. Thou schalt defende hem in thi tabernacle; fro ayenseiyng of tungis.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Blessid be the Lord; for he hath maad wondurful his merci to me in a strengthid citee.
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Forsothe Y seide in the passyng of my soule; Y am cast out fro the face of thin iyen. Therfor thou herdist the vois of my preier; while Y criede to thee.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 Alle ye hooli men of the Lord, loue hym; for the Lord schal seke treuthe, and he schal yelde plenteuousli to hem that doen pride.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Alle ye that hopen in the Lord, do manli; and youre herte be coumfortid.
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

< Psalms 31 >