< Psalms 28 >

1 To Dauid. Lord, Y schal crye to thee; my God, be thou not stille fro me, be thou not stille `ony tyme fro me; and Y schal be maad lijk to hem, that goen doun in to the lake.
Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2 Lord, here thou the vois of my bisechyng, while Y preie to thee; whyle Y reise myn hondis to thin hooli temple.
Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3 Bitake thou not me togidere with synneris; and leese thou not me with hem that worchen wickidnesse. Whyche speken pees with her neiybore; but yuels ben in her hertis.
Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4 Yyue thou to hem vpe the werkis of hem; and vpe the wickidnesse of her fyndyngis. Yyue thou to hem vpe the werkis of her hondis; yelde thou her yeldyng to hem.
Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5 For thei vndurstoden not the werkis of the Lord, and bi the werkis of hise hondis thou schalt destrie hem; and thou schalt not bilde hem.
Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
6 Blissid be the Lord; for he herde the vois of my bisechyng.
Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7 The Lord is myn helpere and my defendere; and myn herte hopide in hym, and Y am helpid. And my fleisch flouride ayen; and of my wille Y schal knowleche to hym.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8 The Lord is the strengthe of his puple; and he is defendere of the sauyngis of his crist.
Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9 Lord, make thou saaf thi puple, and blesse thou thin eritage; and reule thou hem, and enhaunse thou hem til in to with outen ende.
Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

< Psalms 28 >