< Psalms 25 >

1 To Dauid.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Lord, to thee Y haue reisid my soule; my God, Y truste in thee, be Y not aschamed.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Nethir myn enemyes scorne me; for alle men that suffren thee schulen not be schent.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Alle men doynge wickyd thingis superfluli; be schent. Lord, schewe thou thi weies to me; and teche thou me thi pathis.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Dresse thou me in thi treuthe, and teche thou me, for thou art God my sauyour; and Y suffride thee al dai.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Lord, haue thou mynde of thi merciful doyngis; and of thi mercies that ben fro the world.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Haue thou not mynde on the trespassis of my yongthe; and on myn vnkunnyngis. Thou, Lord, haue mynde on me bi thi merci; for thi goodnesse.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 The Lord is swete and riytful; for this he schal yyue a lawe to men trespassynge in the weie.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 He schal dresse deboner men in doom; he schal teche mylde men hise weies.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Alle the weies of the Lord ben mercy and treuthe; to men sekynge his testament, and hise witnessyngis.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Lord, for thi name thou schalt do merci to my synne; for it is myche.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Who is a man, that dredith the Lord? he ordeyneth to hym a lawe in the weie which he chees.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 His soule schal dwelle in goodis; and his seed schal enerite the lond.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 The Lord is a sadnesse to men dredynge hym; and his testament is, that it be schewid to hem.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Myn iyen ben euere to the Lord; for he schal breide awey my feet fro the snare.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Biholde thou on me, and haue thou mercy on me; for Y am
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 oon aloone and pore The tribulaciouns of myn herte ben multiplied; delyuere thou me of my nedis.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Se thou my mekenesse and my trauel; and foryyue thou alle my trespassis.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Bihold thou myn enemyes, for thei ben multiplied; and thei haten me bi wickid hatrede.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Kepe thou my soule, and delyuere thou me; be Y not aschamed, for Y hopide in thee.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Innocent men and riytful cleuyden to me; for Y suffride thee.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 God, delyuere thou Israel; fro alle hise tribulaciouns.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Psalms 25 >