< Psalms 20 >

1 To victorie, the salm of Dauid. The Lord here thee in the dai of tribulacioun; the name of God of Jacob defende thee.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Sende he helpe to thee fro the hooli place; and fro Syon defende he thee.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Be he myndeful of al thi sacrifice; and thi brent sacrifice be maad fat.
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Yyue he to thee aftir thin herte; and conferme he al thi counsel.
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 We schulen be glad in thin helthe; and we schulen be magnyfied in the name of oure God.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 The Lord fille alle thin axyngis; nowe Y haue knowe, that the Lord hath maad saaf his crist. He schal here hym fro his hooly heuene; the helthe of his riyt hond is in poweris.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Thes in charis, and these in horsis; but we schulen inwardli clepe in the name of oure Lord God.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Thei ben boundun, and felden doun; but we han rise, and ben reisid.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Lord, make thou saaf the kyng; and here thou vs in the dai in which we inwardli clepen thee.
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!

< Psalms 20 >