< Psalms 2 >

1 Whi gnastiden with teeth hethene men; and puplis thouyten veyn thingis?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 The kyngis of erthe stoden togidere; and princes camen togidere ayens the Lord, and ayens his Crist?
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Breke we the bondis of hem; and cast we awei the yok of hem fro vs.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 He that dwellith in heuenes schal scorne hem; and the Lord schal bimowe hem.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Thanne he schal speke to hem in his ire; and he schal disturble hem in his stronge veniaunce.
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 Forsothe Y am maad of hym a kyng on Syon, his hooli hil; prechynge his comaundement.
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 The Lord seide to me, Thou art my sone; Y haue gendrid thee to dai.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Axe thou of me, and Y schal yyue to thee hethene men thin eritage; and thi possessioun the termes of erthe.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Thou schalt gouerne hem in an yrun yerde; and thou schalt breke hem as the vessel of a pottere.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 And now, ye kyngis, vndurstonde; ye that demen the erthe, be lerud.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Serue ye the Lord with drede; and make ye ful ioye to hym with tremblyng.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Take ye lore; lest the Lord be wrooth sumtyme, and lest ye perischen fro iust waie. Whanne his `ire brenneth out in schort tyme; blessed ben alle thei, that tristen in hym.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Psalms 2 >