< Psalms 147 >

1 Alleluya. Herie ye the Lord, for the salm is good; heriyng be myrie, and fair to oure God.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 The Lord schal bilde Jerusalem; and schal gadere togidere the scateryngis of Israel.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 Which Lord makith hool men contrit in herte; and byndith togidere the sorewes of hem.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 Which noumbrith the multitude of sterris; and clepith names to alle tho.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Oure Lord is greet, and his vertu is greet; and of his wisdom is no noumbre.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 The Lord takith vp mylde men; forsothe he makith low synneris `til to the erthe.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Bifore synge ye to the Lord in knoulechyng; seye ye salm to oure God in an harpe.
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Which hilith heuene with cloudis; and makith redi reyn to the erthe. Which bryngith forth hei in hillis; and eerbe to the seruice of men.
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Which yyueth mete to her werk beestis; and to the briddys of crowis clepinge hym.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 He schal not haue wille in the strengthe of an hors; nether it schal be wel plesaunt to hym in the leggis of a man.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 It is wel plesaunt to the Lord on men that dreden hym; and in hem that hopen on his mercy.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Jerusalem, herie thou the Lord; Syon, herie thou thi God.
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 For he hath coumfortid the lockis of thi yatis; he hath blessid thi sones in thee.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 Which hath set thi coostis pees; and fillith thee with the fatnesse of wheete.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 Which sendith out his speche to the erthe; his word renneth swiftli.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 Which yyueth snow as wolle; spredith abrood a cloude as aische.
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 He sendith his cristal as mussels; who schal suffre bifore the face of his cooldnesse?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 He schal sende out his word, and schal melte tho; his spirit schal blowe, and watris schulen flowe.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 Which tellith his word to Jacob; and hise riytfulnessis and domes to Israel.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 He dide not so to ech nacioun; and he schewide not hise domes to hem.
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 147 >