< Psalms 141 >
1 `The salm `of Dauith. Lord, Y criede to thee, here thou me; yyue thou tent to my vois, whanne Y schal crye to thee.
Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
2 Mi preier be dressid as encense in thi siyt; the reisyng of myn hondis be as the euentid sacrifice.
Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
3 Lord, sette thou a keping to my mouth; and a dore of stonding aboute to my lippis.
Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
4 Bowe thou not myn herte in to wordis of malice; to excuse excusingis in synne. With men worchinge wickidnesse; and Y schal not comyne with the chosun men of hem.
Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
5 A iust man schal repreue me in mersi, and schal blame me; but the oile of a synner make not fat myn heed. For whi and yit my preier is in the wel plesaunt thingis of hem;
Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
6 for the domesmen of hem ioyned to the stoon weren sopun vp. Here thei my wordis,
Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
7 for tho weren myyti. As fatnesse is brokun out on the erthe; oure bonys ben scatered niy helle. Lord, Lord, (Sheol )
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol )
8 for myn iyen ben to thee, Y hopide in thee; take thou not awei my soule.
Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
9 Kepe thou me fro the snare which thei ordeyneden to me; and fro the sclaundris of hem that worchen wickidnesse. Synneris schulen falle in the nett therof;
Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 Y am aloone til Y passe.
Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.