< Psalms 14 >

1 To the victorie of Dauid. The vnwise man seide in his herte, God is not. Thei ben corrupt, and ben maad abhomynable in her studies; noon is that doith good, noon is til to oon.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
2 The Lord bihelde fro heuene on the sones of men; that he se, if ony is vndurstondynge, ethir sekynge God.
Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
3 Alle bowiden awei, togidere thei ben maad vnprofitable; noon is that doth good, noon is `til to oon. The throte of hem is an open sepulcre, thei diden gilefuli with her tungis; the venym of snakis is vndur her lippis. Whos mouth is ful of cursyng and bittirnesse; her feet ben swift to schede out blood. Sorewe and cursidnesse is in the weies of hem, and thei knewen not the weie of pees; the drede of God is not bifor her iyen.
Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
4 Whether alle men that worchen wickidnesse schulen not knowe; that deuowren my puple, as mete of breed?
Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
5 Thei clepeden not the Lord; thei trembliden there for dreed, where was no drede;
Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
6 for the Lord is in a riytful generacioun. Thou hast schent the counsel of a pore man; for the Lord is his hope.
Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
7 Who schal yyue fro Syon helthe to Israel? Whanne the Lord hath turned awei the caitifte of his puple; Jacob schal `fulli be ioiful, and Israel schal be glad.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!

< Psalms 14 >