< Psalms 129 >

1 The song of greces. Israel seie now; Ofte thei fouyten ayens me fro my yongth.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 Ofte thei fouyten ayens me fro my yongthe; and sotheli thei miyten not to me.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 Synneris forgeden on my bak; thei maden long her wickidnesse.
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 The `iust Lord schal beete the nollis of synneris;
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 alle that haten Sion be schent, and turned abak.
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 Be thei maad as the hey of hous coppis; that driede vp, bifore that it be drawun vp.
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 Of which hei he that schal repe, schal not fille his hond; and he that schal gadere hondfullis, schal not fille his bosum.
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 And thei that passiden forth seiden not, The blessing of the Lord be on you; we blessiden you in the name of the Lord.
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

< Psalms 129 >