< Psalms 127 >
1 The song of greces of Salomon. `No but the Lord bilde the hous; thei that bilden it han trauelid in veyn. No but the Lord kepith the citee; he wakith in veyn that kepith it.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
2 It is veyn to you to rise bifore the liyt; rise ye after that ye han sete, that eten the breed of sorewe. Whanne he schal yyue sleep to his loued; lo!
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
3 the eritage of the Lord `is sones, the mede is the fruyt of wombe.
Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
4 As arowis ben in the hond of the miyti; so the sones of hem that ben schakun out.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
5 Blessid is the man, that hath fillid his desier of tho; he schal not be schent, whanne he schal speke to hise enemyes in the yate.
Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.