< Psalms 119 >

1 Alleluia. Blessid ben men with out wem in the weie; that gon in the lawe of the Lord.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Blessid ben thei, that seken hise witnessingis; seken him in al the herte.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 For thei that worchen wickidnesse; yeden not in hise weies.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Thou hast comaundid; that thin heestis be kept greetly.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 I wolde that my weies be dressid; to kepe thi iustifiyngis.
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Thanne Y schal not be schent; whanne Y schal biholde perfitli in alle thin heestis.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 I schal knouleche to thee in the dressing of herte; in that that Y lernyde the domes of thi riytfulnesse.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 I schal kepe thi iustifiyngis; forsake thou not me on ech side.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 In what thing amendith a yong waxinge man his weie? in keping thi wordis.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 In al myn herte Y souyte thee; putte thou me not awei fro thin heestis.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 In myn herte Y hidde thi spechis; that Y do not synne ayens thee.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Lord, thou art blessid; teche thou me thi iustifiyngis.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 In my lippis Y haue pronounsid; alle the domes of thi mouth.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 I delitide in the weie of thi witnessingis; as in alle richessis.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 I schal be ocupied in thin heestis; and Y schal biholde thi weies.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 I schal bithenke in thi iustifiyngis; Y schal not foryete thi wordis.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Yelde to thi seruaunt; quiken thou me, and Y schal kepe thi wordis.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Liytne thou myn iyen; and Y schal biholde the merueils of thi lawe.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 I am a comeling in erthe; hide thou not thin heestis fro me.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Mi soule coueitide to desire thi iustifiyngis; in al tyme.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Thou blamedist the proude; thei ben cursid, that bowen awei fro thin heestis.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Do thou awei `fro me schenschipe and dispising; for Y souyte thi witnessingis.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 For whi princis saten, and spaken ayens me; but thi seruaunt was exercisid in thi iustifiyngis.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 For whi and thi witnessyngis is my thenkyng; and my counsel is thi iustifiyngis.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Mi soule cleuede to the pawment; quykine thou me bi thi word.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 I telde out my weies, and thou herdist me; teche thou me thi iustifiyngis.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Lerne thou me the weie of thi iustifiyngis; and Y schal be exercisid in thi merueils.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Mi soule nappide for anoye; conferme thou me in thi wordis.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Remoue thou fro me the weie of wickidnesse; and in thi lawe haue thou merci on me.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 I chees the weie of treuthe; Y foryat not thi domes.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Lord, Y cleuede to thi witnessyngis; nyle thou schende me.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 I ran the weie of thi comaundementis; whanne thou alargidist myn herte.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Lord, sette thou to me a lawe, the weie of thi iustifiyngis; and Y schal seke it euere.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Yyue thou vndurstonding to me, and Y schal seke thi lawe; and Y schal kepe it in al myn herte.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Lede me forth in the path of thin heestis; for Y wolde it.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 `Bowe thou myn herte in to thi witnessingus; and not in to aueryce.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Turne thou awei myn iyen, that `tho seen not vanyte; quykene thou me in thi weie.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Ordeyne thi speche to thi seruaunt; in thi drede.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Kitte awey my schenschip, which Y supposide; for thi domes ben myrie.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Lo! Y coueitide thi comaundementis; quikene thou me in thin equite.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 And, Lord, thi merci come on me; thin heelthe come bi thi speche.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 And Y schal answere a word to men seiynge schenschipe to me; for Y hopide in thi wordis.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 And take thou not awei fro my mouth the word of treuthe outerli; for Y hopide aboue in thi domes.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 And Y schal kepe thi lawe euere; in to the world, and in to the world of world.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 And Y yede in largenesse; for Y souyte thi comaundementis.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 And Y spak of thi witnessyngis in the siyt of kingis; and Y was not schent.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 And Y bithouyte in thin heestis; whiche Y louede.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 And Y reiside myn hondis to thi comaundementis, whiche Y louede; and Y schal be excercisid in thi iustifiyngis.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Lord, haue thou mynde on thi word to thi seruaunt; in which word thou hast youe hope to me.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 This coumfortide me in my lownesse; for thi word quikenede me.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Proude men diden wickidli bi alle thingis; but Y bowide not awei fro thi lawe.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Lord, Y was myndeful on thi domes fro the world; and Y was coumfortid.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Failing helde me; for synneris forsakinge thi lawe.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Thi iustifiyngis weren delitable to me to be sungun; in the place of my pilgrimage.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Lord, Y hadde mynde of thi name bi niyt; and Y kepte thi lawe.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 This thing was maad to me; for Y souyte thi iustifiyngis.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Lord, my part; Y seide to kepe thi lawe.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 I bisouyte thi face in al myn herte; haue thou merci on me bi thi speche.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 I bithouyte my weies; and Y turnede my feet in to thi witnessyngis.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 I am redi, and Y am not disturblid; to kepe thi comaundementis.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 The coordis of synneris han biclippid me; and Y haue not foryete thi lawe.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 At mydnyyt Y roos to knouleche to thee; on the domes of thi iustifiyngis.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 I am parcener of alle that dreden thee; and kepen thin heestis.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Lord, the erthe is ful of thi merci; teche thou me thi iustifiyngis.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Lord, thou hast do goodnesse with thi seruaunt; bi thi word.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Teche thou me goodnesse, and loore, and kunnyng; for Y bileuede to thin heestis.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Bifor that Y was maad meke, Y trespasside; therfor Y kepte thi speche.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Thou art good; and in thi goodnesse teche thou me thi iustifiyngis.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 The wickidnesse of hem that ben proude, is multiplied on me; but in al myn herte Y schal seke thin heestis.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 The herte of hem is cruddid as mylk; but Y bithouyte thi lawe.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 It is good to me, that thou hast maad me meke; that Y lerne thi iustifiyngis.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 The lawe of thi mouth is betere to me; than thousyndis of gold and of siluer.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Thin hondis maden me, and fourmeden me; yyue thou vndurstondyng to me, that Y lerne thin heestis.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Thei that dreden thee schulen se me, and schulen be glad; for Y hopide more on thi wordis.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Lord, Y knewe, that thi domes ben equite; and in thi treuth thou hast maad me meke.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Thi merci be maad, that it coumforte me; bi thi speche to thi seruaunt.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Thi merciful doyngis come to me, and Y schal lyue; for thi lawe is my thenkyng.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Thei that ben proude be schent, for vniustli thei diden wickidnesse ayens me; but Y schal be exercisid in thin heestis.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Thei that dreden thee be turned to me; and thei that knowen thi witnessyngis.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Myn herte be maad vnwemmed in thi iustifiyngis; that Y be not schent.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Mi soule failide in to thin helthe; and Y hopide more on thi word.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Myn iyen failiden in to thi speche; seiynge, Whanne schalt thou coumforte me?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 For Y am maad as a bowge in frost; Y haue not foryete thi iustifiyngis.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Hou many ben the daies of thi seruaunt; whanne thou schalt make doom of hem that pursuen me?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Wickid men telden to me ianglyngis; but not as thi lawe.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Alle thi comaundementis ben treuthe; wickid men han pursued me, helpe thou me.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Almeest thei endiden me in erthe; but I forsook not thi comaundementis.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Bi thi mersi quikene thou me; and Y schal kepe the witnessingis of thi mouth.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Lord, thi word dwellith in heuene; with outen ende.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Thi treuthe dwellith in generacioun, and in to generacioun; thou hast foundid the erthe, and it dwellith.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 The dai lastith contynueli bi thi ordynaunce; for alle thingis seruen to thee.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 No but that thi lawe was my thenking; thanne perauenture Y hadde perischid in my lownesse.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 With outen ende Y schal not foryete thi iustifiyngis; for in tho thou hast quikened me.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 I am thin, make thou me saaf; for Y haue souyt thi iustifiyngis.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Synneris aboden me, for to leese me; Y vndurstood thi witnessingis.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 I siy the ende of al ende; thi comaundement is ful large.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Lord, hou louede Y thi lawe; al dai it is my thenking.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Aboue myn enemyes thou madist me prudent bi thi comaundement; for it is to me with outen ende.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 I vndurstood aboue alle men techinge me; for thi witnessingis is my thenking.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 I vndirstood aboue eelde men; for Y souyte thi comaundementis.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 I forbeed my feet fro al euel weie; that Y kepe thi wordis.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 I bowide not fro thi domes; for thou hast set lawe to me.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Thi spechis ben ful swete to my cheekis; aboue hony to my mouth.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 I vnderstood of thin heestis; therfor Y hatide al the weie of wickidnesse.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Thi word is a lanterne to my feet; and liyt to my pathis.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 I swoor, and purposide stidefastli; to kepe the domes of thi riytfulnesse.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 I am maad low bi alle thingis; Lord, quykene thou me bi thi word.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Lord, make thou wel plesinge the wilful thingis of my mouth; and teche thou me thi domes.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Mi soule is euere in myn hondis; and Y foryat not thi lawe.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Synneris settiden a snare to me; and Y erride not fro thi comaundementis.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 I purchasside thi witnessyngis bi eritage with outen ende; for tho ben the ful ioiyng of myn herte.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 I bowide myn herte to do thi iustifiyngis with outen ende; for reward.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 I hatide wickid men; and Y louede thi lawe.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Thou art myn helpere, and my `taker vp; and Y hopide more on thi word.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Ye wickide men, bowe awei fro me; and Y schal seke the comaundementis of my God.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Vp take thou me bi thi word, and Y schal lyue; and schende thou not me fro myn abydyng.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Helpe thou me, and Y schal be saaf; and Y schal bithenke euere in thi iustifiyngis.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Thou hast forsake alle men goynge awey fro thi domes; for the thouyt of hem is vniust.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 I arettide alle the synneris of erthe brekeris of the lawe; therfor Y louede thi witnessyngis.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Naile thou my fleischis with thi drede; for Y dredde of thi domes.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 I dide doom and riytwisnesse; bitake thou not me to hem that falsli chalengen me.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Take vp thi seruaunt in to goodnesse; thei that ben proude chalenge not me.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Myn iyen failiden in to thin helthe; and in to the speche of thi riytfulnesse.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Do thou with thi seruaunt bi thi merci; and teche thou me thi iustifiyngis.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 I am thi seruaunt, yyue thou vndurstondyng to me; that Y kunne thi witnessingis.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Lord, it is tyme to do; thei han distried thi lawe.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Therfor Y louede thi comaundementis; more than gold and topazion.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Therfor Y was dressid to alle thin heestis; Y hatide al wickid weie.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Lord, thi witnessingis ben wondirful; therfor my soule souyte tho.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Declaring of thi wordis liytneth; and yyueth vnderstonding to meke men.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 I openede my mouth, and drouy the spirit; for Y desiride thi comaundementis.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Biholde thou on me, and haue merci on me; bi the dom of hem that louen thi name.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Dresse thou my goyingis bi thi speche; that al vnriytfulnesse haue not lordschip on me.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Ayeyn bie thou me fro the false chalengis of men; that Y kepe thin heestis.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Liytne thi face on thi seruaunt; and teche thou me thi iustifiyngis.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Myn iyen ledden forth the outgoynges of watris; for thei kepten not thi lawe.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Lord, thou art iust; and thi dom is riytful.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Thou hast comaundid riytfulnesse, thi witnessingis; and thi treuthe greetli to be kept.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Mi feruent loue made me to be meltid; for myn enemys foryaten thi wordis.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Thi speche is greetli enflawmed; and thi seruaunt louede it.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 I am yong, and dispisid; Y foryat not thi iustifiyngis.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Lord, thi riytfulnesse is riytfulnesse with outen ende; and thi lawe is treuthe.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Tribulacioun and angwische founden me; thin heestis is my thenking.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Thi witnessyngis is equite with outen ende; yyue thou vndirstondyng to me, and Y schal lyue.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 I criede in al myn herte, Lord, here thou me; and Y schal seke thi iustifiyngis.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 I criede to thee, make thou me saaf; that Y kepe thi comaundementis.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 I bifor cam in ripenesse, and Y criede; Y hopide aboue on thi wordis.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Myn iyen bifor camen to thee ful eerli; that Y schulde bithenke thi speches.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Lord, here thou my vois bi thi merci; and quykene thou me bi thi doom.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Thei that pursuen me neiyden to wickidnesse; forsothe thei ben maad fer fro thi lawe.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Lord, thou art nyy; and alle thi weies ben treuthe.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 In the bigynnyng Y knewe of thi witnessingis; for thou hast foundid tho with outen ende.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Se thou my mekenesse, and delyuere thou me; for Y foryat not thi lawe.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Deme thou my dom, and ayenbie thou me; quikene thou me for thi speche.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Heelthe is fer fro synners; for thei souyten not thi iustifiyngis.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Lord, thi mercies ben manye; quykene thou me bi thi dom.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Thei ben manye that pursuen me, and doen tribulacioun to me; Y bowide not awei fro thi witnessingis.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 I siy brekers of the lawe, and Y was meltid; for thei kepten not thi spechis.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Lord, se thou, for Y louede thi comaundementis; quikene thou me in thi merci.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 The bigynnyng of thi wordis is treuthe; alle the domes of thi riytwisnesse ben withouten ende.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Princes pursueden me with outen cause; and my herte dredde of thi wordis.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 I schal be glad on thi spechis; as he that fyndith many spuylis.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 I hatide and wlatide wickidnesse; forsothe Y louede thi lawe.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 I seide heriyngis to thee seuene sithis in the dai; on the domes of thi riytfulnesse.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Miche pees is to hem that louen thi lawe; and no sclaundir is to hem.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Lord, Y abood thin heelthe; and Y louede thin heestis.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Mi soule kepte thi witnessyngis; and louede tho greetli.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 I kepte thi `comaundementis, and thi witnessingis; for alle my weies ben in thi siyt.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Lord, my biseching come niy in thi siyt; bi thi speche yyue thou vndurstonding to me.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Myn axing entre in thi siyt; bi thi speche delyuere thou me.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Mi lippis schulen telle out an ympne; whanne thou hast tauyte me thi iustifiyngis.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Mi tunge schal pronounce thi speche; for whi alle thi comaundementis ben equite.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Thin hond be maad, that it saue me; for Y haue chose thin heestis.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Lord, Y coueitide thin heelthe; and thi lawe is my thenking.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Mi soule schal lyue, and schal herie thee; and thi domes schulen helpe me.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 I erride as a scheep that perischide; Lord, seke thi seruaunt, for Y foryat not thi comaundementis.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalms 119 >