< Psalms 118 >

1 Alleluia. Knouleche ye to the Lord, for he is good; for his merci is with outen ende.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Israel seie now, for he is good; for his merci is with outen ende.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 The hous of Aaron seie now; for his merci is with outen ende.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Thei that dreden the Lord, seie now; for his merci is withouten ende.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 Of tribulacioun Y inwardli clepide the Lord; and the Lord herde me in largenesse.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 The Lord is an helpere to me; Y schal not drede what a man schal do to me.
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 The Lord is an helpere to me; and Y schal dispise myn enemyes.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 It is betere for to trist in the Lord; than for to triste in man.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 It is betere for to hope in the Lord; than for to hope in princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 Alle folkis cumpassiden me; and in the name of the Lord it bifelde, for Y am auengide on hem.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Thei cumpassinge cumpassiden me; and in the name of the Lord, for Y am auengid on hem.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Thei cumpassiden me as been, and thei brenten out as fier doith among thornes; and in the name of the Lord, for Y am avengid on hem.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 I was hurlid, and turnede vpsedoun, that Y schulde falle doun; and the Lord took me vp.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 The Lord is my strengthe, and my heryyng; and he is maad to me in to heelthe.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 The vois of ful out ioiyng and of heelthe; be in the tabernaclis of iust men.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 The riyt hond of the Lord hath do vertu, the riyt hond of the Lord enhaunside me; the riyt hond of the Lord hath do vertu.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 I schal not die, but Y schal lyue; and Y schal telle the werkis of the Lord.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 The Lord chastisinge hath chastisid me; and he yaf not me to deth.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Opene ye to me the yatis of riytfulnesse, and Y schal entre bi tho, and Y schal knouleche to the Lord;
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 this yate is of the Lord, and iust men schulen entre bi it.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 I schal knouleche to thee, for thou herdist me; and art maad to me in to heelthe.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 The stoon which the bilderis repreueden; this is maad in to the heed of the corner.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 This thing is maad of the Lord; and it is wonderful bifore oure iyen.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 This is the dai which the Lord made; make we ful out ioye, and be we glad ther ynne.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 O! Lord, make thou me saaf, O! Lord, make thou wel prosperite;
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 blessid is he that cometh in the name of the Lord. We blesseden you of the hous of the Lord;
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 God is Lord, and hath youe liyt to vs. Ordeyne ye a solempne dai in thicke puplis; til to the horn of the auter.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Thou art my God, and Y schal knouleche to thee; thou art my God, and Y schal enhaunse thee. I schal knouleche to thee, for thou herdist me; and thou art maad to me in to heelthe.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Knouleche ye to the Lord, for he is good; for his merci is with outen ende.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psalms 118 >