< Psalms 113 >

1 Alleluya. Children, preise ye the Lord; preise ye the name of the Lord.
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 The name of the Lord be blessid; fro this tyme now and til in to the world.
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Fro the risyng of the sunne til to the goyng doun; the name of the Lord is worthi to be preisid.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 The Lord is hiy aboue alle folkis; and his glorie is aboue heuenes.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Who is as oure Lord God, that dwellith in hiye thingis;
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 and biholdith meke thingis in heuene and in erthe?
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 Reisynge a nedi man fro the erthe; and enhaunsinge a pore man fro drit.
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 That he sette hym with princes; with the princes of his puple.
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 Which makith a bareyn womman dwelle in the hous; a glad modir of sones.
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Psalms 113 >