< Psalms 104 >
1 Mi soule, blesse thou the Lord; my Lord God, thou art magnyfied greetli. Thou hast clothid knouleching and fairnesse; and thou art clothid with liyt,
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 as with a cloth. And thou stretchist forth heuene as a skyn;
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 and thou hilist with watris the hiyer partis therof. Which settist a cloude thi stiyng; which goest on the fetheris of wyndis.
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 Which makist spiritis thin aungels; and thi mynystris brennynge fier.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 Which hast foundid the erthe on his stablenesse; it schal not be bowid in to the world of world.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 The depthe of watris as a cloth is the clothing therof; watris schulen stonde on hillis.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 Tho schulen fle fro thi blamyng; men schulen be aferd of the vois of thi thundur.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 Hillis stien vp, and feeldis goen doun; in to the place which thou hast foundid to tho.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Thou hast set a terme, which tho schulen not passe; nether tho schulen be turned, for to hile the erthe.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 And thou sendist out wellis in grete valeis; watris schulen passe bitwix the myddil of hillis.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 Alle the beestis of the feeld schulen drynke; wielde assis schulen abide in her thirst.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 Briddis of the eir schulen dwelle on tho; fro the myddis of stoonys thei schulen yyue voices.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 And thou moistist hillis of her hiyer thingis; the erthe schal be fillid of the fruyt of thi werkis.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 And thou bringist forth hei to beestis; and eerbe to the seruyce of men. That thou bringe forth breed of the erthe;
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 and that wiyn make glad the herte of men. That he make glad the face with oile; and that breed make stidefast the herte of man.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 The trees of the feeld schulen be fillid, and the cedris of the Liban, whiche he plauntide;
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 sparewis schulen make nest there. The hous of the gerfaukun is the leeder of tho;
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 hiye hillis ben refute to hertis; a stoon is refutt to irchouns.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 He made the moone in to tymes; the sunne knewe his goyng doun.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Thou hast set derknessis, and nyyt is maad; alle beestis of the wode schulen go ther ynne.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 Liouns whelpis rorynge for to rauysche; and to seke of God meete to hem silf.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 The sunne is risun, and tho ben gaderid togidere; and tho schulen be set in her couchis.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 A man schal go out to his werk; and to his worching, til to the euentid.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 Lord, thi werkis ben magnefiede ful myche, thou hast maad alle thingis in wisdom; the erthe is fillid with thi possessioun.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 This see is greet and large to hondis; there ben crepinge beestis, of which is noon noumbre. Litil beestis with grete;
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 schippis schulen passe there. This dragoun which thou hast formyd; for to scorne hym.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 Alle thingis abiden of thee; that thou yyue to hem meete in tyme.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 Whanne thou schalt yyue to hem, thei schulen gadere; whanne thou schalt opene thin hond, alle thingis schulen be fillid with goodnesse.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 But whanne thou schalt turne awey the face, thei schulen be disturblid; thou schalt take awei the spirit of them, and thei schulen faile; and thei schulen turne ayen in to her dust.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Sende out thi spirit, and thei schulen be formed of the newe; and thou schalt renule the face of the erthe.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 The glorie of the Lord be in to the world; the Lord schal be glad in hise werkis.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 Which biholdith the erthe, and makith it to tremble; which touchith hillis, and tho smoken.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 I schal singe to the Lord in my lijf; Y schal seie salm to my God, as longe as Y am.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Mi speche be myrie to him; forsothe Y schal delite in the Lord.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Synneris faile fro the erthe, and wickid men faile, so that thei be not; my soule, blesse thou the Lord.
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.