< Proverbs 9 >
1 Wisdom bildide an hous to him silf; he hewide out seuene pileris,
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 he offride his slayn sacrifices, he medlide wijn, and settide forth his table.
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 He sente hise handmaides, that thei schulden clepe to the tour; and to the wallis of the citee.
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 If ony man is litil; come he to me. And wisdom spak to vnwise men,
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 Come ye, ete ye my breed; and drynke ye the wiyn, which Y haue medlid to you.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Forsake ye yong childhed, and lyue ye; and go ye bi the weyes of prudence.
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 He that techith a scornere, doith wrong to him silf; and he that vndirnymmeth a wickid man, gendrith a wem to him silf.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 Nile thou vndirnyme a scornere; lest he hate thee. Vndirnyme thou a wise man; and he schal loue thee.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Yyue thou occasioun to a wise man; and wisdom schal be encreessid to hym. Teche thou a iust man; and he schal haste to take.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 The bigynnyng of wisdom is the dreed of the Lord; and prudence is the kunnyng of seyntis.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 For thi daies schulen be multiplied bi me; and yeeris of lijf schulen be encreessid to thee.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 If thou art wijs; thou schalt be to thi silf, and to thi neiyboris. Forsothe if thou art a scornere; thou aloone schalt bere yuel.
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 A fonned womman, and ful of cry, and ful of vnleueful lustis, and that kan no thing outirli,
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 sittith in the doris of hir hous, on a seete, in an hiy place of the cite;
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 to clepe men passinge bi the weie, and men goynge in her iournei.
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 Who is a litil man `of wit; bowe he to me. And sche spak to a coward,
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 Watris of thefte ben swettere, and breed hid is swettere.
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 And wiste not that giauntis ben there; and the gestis `of hir ben in the depthis of helle. Sotheli he that schal be applied, ether fastned, to hir; schal go doun to hellis. For whi he that goith awei fro hir; schal be saued. (Sheol )
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )