< Proverbs 31 >
1 The wordis of Lamuel, the king; the visioun bi which his modir tauyte hym.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 What my derlyng? what the derlyng of my wombe? what the derlyng of my desiris?
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Yyue thou not thi catel to wymmen, and thi richessis to do awei kyngis.
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 A! Lamuel, nyle thou yiue wyn to kingis; for no pryuete is, where drunkenesse regneth.
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 Lest perauenture thei drynke, and foryete domes, and chaunge the cause of the sones of a pore man.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Yyue ye sidur to hem that morenen, and wyn to hem that ben of bitter soule.
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 Drinke thei, and foryete thei her nedinesse; and thenke thei no more on her sorewe.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Opene thi mouth for a doumb man,
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 and opene thi mouth for the causes of alle sones that passen forth. Deme thou that that is iust, and deme thou a nedi man and a pore man.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Who schal fynde a stronge womman? the prijs of her is fer, and fro the laste endis.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 The herte of hir hosebond tristith in hir; and sche schal not haue nede to spuylis.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Sche schal yelde to hym good, and not yuel, in alle the daies of hir lijf.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Sche souyte wolle and flex; and wrouyte bi the counsel of hir hondis.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Sche is maad as the schip of a marchaunt, that berith his breed fro fer.
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 And sche roos bi nyyt, and yaf prey to hir meyneals, and metis to hir handmaidis.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Sche bihelde a feeld, and bouyte it; of the fruyt of hir hondis sche plauntide a vyner.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Sche girde hir leendis with strengthe, and made strong hir arm.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Sche taastide, and siy, that hir marchaundie was good; hir lanterne schal not be quenchid in the niyt.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Sche putte hir hondis to stronge thingis, and hir fyngris token the spyndil.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Sche openyde hir hond to a nedi man, and stretchide forth hir hondis to a pore man.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Sche schal not drede for hir hous of the cooldis of snow; for alle hir meyneals ben clothid with double clothis.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Sche made to hir a ray cloth; bijs and purpur is the cloth of hir.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Hir hosebonde is noble in the yatis, whanne he sittith with the senatours of erthe.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Sche made lynnun cloth, and selde; and yaf a girdil to a Chananei.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Strengthe and fairnesse is the clothing of hir; and sche schal leiye in the laste dai.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Sche openyde hir mouth to wisdom; and the lawe of merci is in hir tunge.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Sche bihelde the pathis of hir hous; and sche eet not breed idili.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Hir sones risiden, and prechiden hir moost blessid; hir hosebonde roos, and preiside hir.
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 Many douytris gaderiden richessis; thou passidist alle.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Fairnesse is disseiuable grace, and veyn; thilke womman, that dredith the Lord, schal be preisid.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Yyue ye to hir of the fruyt of hir hondis; and hir werkis preise hir in the yatis.
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.