< Proverbs 3 >

1 Mi sone, foryete thou not my lawe; and thyn herte kepe my comaundementis.
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 For tho schulen sette to thee the lengthe of daies, and the yeeris of lijf, and pees.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Merci and treuthe forsake thee not; bynde thou tho to thi throte, and write in the tablis of thin herte.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 And thou schalt fynde grace, and good teching bifore God and men.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Haue thou trist in the Lord, of al thin herte; and triste thou not to thi prudence.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 In alle thi weies thenke thou on hym, and he schal dresse thi goyngis.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Be thou not wijs anentis thi silf; drede thou God, and go awei fro yuel.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 For whi helthe schal be in thi nawle, and moisting of thi boonys.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Onoure thou the Lord of thi catel, and of the beste of alle thi fruytis yyue thou to pore men;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 and thi bernes schulen be fillid with abundaunce, and pressours schulen flowe with wiyn.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 My sone, caste thou not awei the teching of the Lord; and faile thou not, whanne thou art chastisid of him.
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 For the Lord chastisith hym, whom he loueth; and as a fadir in the sone he plesith hym.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Blessid is the man that fyndith wisdom, and which flowith with prudence.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 The geting therof is betere than the marchaundie of gold and of siluer; the fruytis therof ben the firste and clenneste.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 It is preciousere than alle richessis; and alle thingis that ben desirid, moun not be comparisound to this.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Lengthe of daies is in the riythalf therof, and richessis and glorie ben in the lifthalf therof.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 The weies therof ben feire weies, and alle the pathis therof ben pesible.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 It is a tre of lijf to hem that taken it; and he that holdith it, is blessid.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 The Lord foundide the erthe bi wisdom; he stablischide heuenes bi prudence.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 The depthis of watris braken out bi his wisdom; and cloudis wexen togidere bi dewe.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 My sone, these thingis flete not awey fro thin iyen; kepe thou my lawe, and my counsel;
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 and lijf schal be to thi soule, and grace `schal be to thi chekis.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Thanne thou schalt go tristili in thi weie; and thi foot schal not snapere.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 If thou schalt slepe, thou schalt not drede; thou schalt reste, and thi sleep schal be soft.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Drede thou not bi sudeyne feer, and the powers of wickid men fallynge in on thee.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 For the Lord schal be at thi side; and he schal kepe thi foot, that thou be not takun.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Nil thou forbede to do wel him that mai; if thou maist, and do thou wel.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Seie thou not to thi frend, Go, and turne thou ayen, and to morewe Y schal yyue to thee; whanne thou maist yyue anoon.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Ymagyne thou not yuel to thi freend, whanne he hath trist in thee.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Stryue thou not ayens a man with out cause, whanne he doith noon yuel to thee.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Sue thou not an vniust man, sue thou not hise weies.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 For ech disseyuer is abhomynacioun of the Lord; and his speking is with simple men.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Nedinesse is sent of the Lord in the hous of a wickid man; but the dwelling places of iust men schulen be blessid.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 He schal scorne scorneris; and he schal yyue grace to mylde men.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Wise men schulen haue glorie; enhaunsing of foolis is schenschipe.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Proverbs 3 >