< Proverbs 20 >
1 Wiyn is a letcherouse thing and drunkenesse is ful of noise; who euere delitith in these, schal not be wijs.
Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
2 As the roryng of a lioun, so and the drede of the kyng; he that territh hym to ire, synneth ayens his owne lijf.
Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
3 It is onour to a man that departith hym silf fro stryuyngis; but fonned men ben medlid with dispisyngis.
Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
4 A slow man nolde ere for coold; therfor he schal begge in somer, and me schal not yyue to hym.
Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
5 As deep watir, so counsel is in the herte of a man; but a wijs man schal drawe it out.
Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
6 Many men ben clepid merciful; but who schal fynde a feithful man?
Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
7 Forsothe a iust man that goith in his simplenesse, schal leeue blessid sones aftir hym.
Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
8 A king that sittith in the seete of doom, distrieth al yuel bi his lokyng.
Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
9 Who may seie, Myn herte is clene; Y am clene of synne?
Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
10 A weiyte and a weiyte, a mesure and a mesure, euer eithir is abhomynable at God.
Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
11 A child is vndurstondun bi hise studies, yf his werkis ben riytful and cleene.
Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
12 An eere heringe, and an iye seynge, God made euere eithir.
Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
13 Nyle thou loue sleep, lest nedynesse oppresse thee; opene thin iyen, and be thou fillid with looues.
Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
14 Ech biere seith, It is yuel, it is yuel; and whanne he hath go awey, thanne he schal haue glorie.
Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
15 Gold, and the multitude of iemmes, and a preciouse vessel, ben the lippis of kunnyng.
Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
16 Take thou awei the cloth of hym, that was borewe of an othere man; and for straungeris take thou awei a wed fro hym.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
17 The breed of a leesing is sweet to a man; and aftirward his mouth schal be fillid with rikenyng.
Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
18 Thouytis ben maad strong bi counselis; and bateils schulen be tretid bi gouernals.
Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
19 Be thou not medlid with him that schewith pryuetees, and goith gylefulli, and alargith hise lippis.
Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
20 The liyt of hym that cursith his fadir and modir, schal be quenchid in the myddis of derknessis.
Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
21 Eritage to which me haastith in the bigynnyng, schal wante blessing in the laste tyme.
Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
22 Seie thou not, Y schal yelde yuel for yuel; abide thou the Lord, and he schal delyuere thee.
Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
23 Abhomynacioun at God is weiyte and weiyte; a gileful balaunce is not good.
Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
24 The steppis of man ben dressid of the Lord; who forsothe of men mai vndurstonde his weie?
Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
25 Falling of man is to make auow to seyntis, and aftirward to withdrawe the vowis.
Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
26 A wijs kyng scaterith wickid men; and bowith a bouwe of victorie ouer hem.
Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
27 The lanterne of the Lord is the spirit of man, that sekith out alle the priuetees of the wombe.
Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
28 Merci and treuthe kepen a kyng; and his trone is maad strong bi mekenesse.
Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
29 The ful out ioiyng of yonge men is the strengthe of hem; and the dignyte of elde men is hoornesse.
Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
30 The wannesse of wounde schal wipe aweie yuels, and woundis in the priuyere thingis of the wombe.
Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.