< Numbers 34 >

1 And the Lord spak to Moises,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 and seide, Comaunde thou to the sones of Israel, and thou schalt seie to hem, Whanne ye han entrid in to the lond of Canaan, and it bifelde in to possessioun `to you bi lot, it schal be endid bi these endis.
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 The south part schal bigynne at the wildirnesse of Syn, which is bisidis Edom, and it schal haue termes ayens the eest,
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 the saltiste see, whiche termes schulen cumpasse the south coost bi the `stiynge of Scorpioun, `that is, of an hil clepid Scorpioun, so that tho passe in to Senna, and come to the south, `til to Cades Barne; fro whennus the coostis schulen go out to the town, Abdar bi name, and schulen strecche forth `til to Asemona;
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 and the terme schal go bi cumpas fro Assemona `til to the stronde of Egipt, and it schal be endid bi the brynke of the grete see.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 Forsothe the west coost schal bigynne at the greet see, and schal be closid bi that ende.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 Sotheli at the north coost, the termes schulen bigynne at the greet see, and schulen come `til to the hiyeste hil,
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 fro which tho schulen come in to Emath, `til to the termes of Sedada;
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 and the coostis schulen go `til to Ephrona, and the town of Enan. These schulen be the termes in the north part.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 Fro thennus thei schulen mete coostis ayens the eest coost, fro the town Henan `til to Sephama;
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 and fro Sephama termes schulen go doun in to Reblatha, ayens the welle `of Daphnyn; fro thennus tho schulen come ayens the eest to the se of Cenereth;
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 and tho schulen strecche forth `til to Jordan, and at the laste tho schulen be closid with the salteste see. Ye schulen haue this lond bi hise coostis `in cumpas.
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 And Moises comaundide to the sones of Israel, and seide, This schal be the lond which ye schulen welde bi lot, and which the Lord comaundide to be youun to nyne lynagis and to the half lynage;
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 for the lynage of the sones of Ruben, bi her meynees, and the lynage of the sones of Gad, bi kynrede and noumbre, and half the lynage of Manasses,
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 that is, twey lynagis and an half, han take her part ouer Jordan, ayens Jerico, at the eest coost.
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
16 And the Lord seide to Moises,
Yehova anawuza Mose kuti,
17 These ben the `names of men that schulen departe the lond to you, Eleazar, preest, and Josue, the sone of Nun, and of each lynage, o prynce;
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 of whiche these ben the names, of the lynage of Juda,
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 Caleph, the sone of Jephone;
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 of the lynage of Symeon, Samuhel, the sone of Amyud;
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 of the lynage of Beniamyn, Heliad, sone of Casselon;
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 of the lynage of the sones of Dan, Bochi, sone of Jogli; of the sones of Joseph,
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 of the lynage of Manasses, Hamyel, sone of Ephoth;
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 of the lynage of Effraym, Camuhel, sone of Septhan;
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 of the lynage of Zabulon, Elisaphan, sone of Pharnat;
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 of the lynage of Isacar, duyk Phaltiel, the sone of Ozan; of the lynage of Azer,
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 Abyud, the sone of Salomy;
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 of the lynage of Neptalym, Fedahel, the sone of Amyud.
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 These men it ben, to whiche the Lord comaundide, that thei schulden departe to the sones of Israel the lond of Chanaan.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

< Numbers 34 >