< Numbers 24 >

1 And whanne Balaam siy that it pleside the Lord that he schulde blesse Israel, he yede not as he `hadde go bifore, `that he schulde seke fals dyuynyng `bi chiteryng of briddis, but he dresside his face ayens the desert,
Tsopano Balaamu ataona kuti kunakomera Yehova kudalitsa Israeli, sanapitenso ku mawula monga ankachitira kale, koma kuyangʼana ku chipululu.
2 and reiside iyen, and siy Israel dwellynge in tentis bi hise lynagis. And whanne the Spirit of God felde on hym, and whanne a parable was takun,
Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye
3 he seide, Balaam, the sone of Beor, seide, a man whois iye is stoppid seide,
ndipo ananena uthenga wake: “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka,
4 the herere of Goddis wordis seide, which bihelde the reuelacioun of almyyti God, which fallith doun, and hise iyen ben openyd so, Hou faire ben thi tabernaclis,
uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, yemwe amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, yemwe amagwa chafufumimba, koma maso ake ali chipenyere:
5 Jacob, and thi tentis, Israel!
“Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo, misasa yako, iwe Israeli!
6 as valeys ful of woodis, and moiste gardyns bisidis floodis, as tabernaclis whiche the Lord hath set, as cedris bisidis watris;
“Monga zigwa zotambalala, monga minda mʼmbali mwa mtsinje, monga aloe wodzalidwa ndi Yehova, monga mikungudza mʼmbali mwa madzi.
7 watir schal flowe of his bokat, and his seed schal be in to many watris, `that is, puplis. The kyng of hym schal be takun a wei for Agag, and the rewme of hym schal be doon awai.
Madzi adzayenderera mʼmitsuko yake; mbewu zake zidzakhala ndi madzi ambiri. “Mfumu yake idzakhala yamphamvu kuposa Agagi; ufumu wake udzakwezedwa.
8 God ledde hym out of Egipt, whos strengthe is lijk an vnicorn; thei schulen deuoure hethene men, enemyes `of hym, that is, of Israel; and thei schulen breke the boonus of hem, and schulen perse with arowis.
“Mulungu womutulutsa mʼdziko la Igupto ali ndi mphamvu ngati za njati. Amawononga mitundu yomuwukira ndi kuphwanya mafupa awo, amalasa ndi mivi yake.
9 He restide and slepte as a lyoun, and as a lionesse, whom no man schal dore reise. He that blessith thee, schal be blessid; he that cursith, schal
Monga mkango waumuna, amabisala nagona pansi, monga mkango waukazi, adzamuputa ndani? “Amene adalitsa iwe, adalitsike ndipo amene atemberera iwe, atembereredwe!”
10 be arettid in to cursyng And Balaach was wrooth ayens Balaam, and seide, whanne the hondis weren wrungun to gidere, I clepide thee to curse myn enemyes, whiche ayenward thou hast blessid thries.
Kenaka Balaki anakwiyira Balaamu. Anawomba mʼmanja ndi kunena naye kuti, “Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, koma taona, wawadalitsa katatu konseka.
11 Turne ayen to thi place; forsothe Y demede to onoure thee greetli, but the Lord priuyde thee fro onour disposid.
Tsopano choka msanga uzipita kwanu! Ndinanena kuti ndidzakulipira bwino kwambiri, koma Yehova sanafune kuti ulandire malipirowo.”
12 Balaam answeride to Balaach, Whethir Y seide not to thi messangeris, whiche thou sentist to me,
Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine,
13 Thouy Balaach schal yyue to me his hows ful of siluer and of gold, Y schal not mow passe the word of my Lord God, that Y brynge forth of myn herte ony thing, ethir of good ethir of yuel, but what euer thing the Lord schal seie, Y schal speke this?
kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena?
14 Netheles Y schal go to my puple, and Y schal yyue counsel to thee, what thi puple schal do in the laste tyme to this puple.
Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”
15 Therfor whanne a parable was takun, he seide eft, Balaam, the sone of Beor seide, a man whos iye is stoppid,
Ndipo iye ananena uthenga wake nati, “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka.
16 seide, the herere of Goddis wordis seide, which knowith the doctrine of the hiyeste, and seeth the reuelacioun of almiyti God, which fallith doun and hath opyn iyen,
Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, amene ali ndi nzeru zochokera kwa Wammwambamwamba, amene amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, amene amagwa chafufumimba koma diso lake lili lotsekuka:
17 Y schal se hym, but not now; Y schal biholde hym, but not nyy; a sterre schal be borun of Jacob, and a yerde schal rise of Israel; and he schal smyte the duykis of Moab, and he schal waste alle the sones of Seth; and Ydumye schal be hys possessioun,
“Ndikumuona iye koma osati tsopano; ndikumupenya iye koma osati pafupi. Nyenyezi idzatuluka mwa Yakobo; ndodo yaufumu idzatuluka mwa Israeli. Iye adzagonjetsa Mowabu ndi kugonjetsa ana onse a Seti.
18 the eritage of Seir schal bifalle to his enemyes; forsothe Israel schal do strongli, of Jacob schal be he that schal be lord,
Edomu adzagonjetsedwa; Seiri, mdani wake, adzawonongedwa koma mphamvu za Israeli zidzachuluka.
19 and schal leese the relikis of the citee.
Wolamulira adzachokera mwa Yakobo ndipo adzawononga otsala a mu mzindamo.”
20 And whanne he hadde seyn Amalech, he took a parable, and seide, Amalech is the bigynning of hethene men, whos laste thingis schulen be lost.
Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu: “Aamaleki anali oyamba mwa mitundu ya anthu koma potsiriza pake adzawonongeka.”
21 Also `he siy Cyney, and whanne a parable was takun, he seide, Forsothe thi dwellyng place is strong, but if thou schalt sette thi nest in a stoon,
Kenaka anaonanso Akeni ndipo ananena uthenga wake, “Malo amene mukukhalamo ndi otetezedwa, chisa chanu chinayikidwa pa thanthwe;
22 and schalt be chosun of the generacioun of Cyn, hou longe schalt thou mow dwelle? forsothe Assur schal take thee.
komabe inu Akeni mudzawonongedwa, pamene Asuri adzakutengeni ukapolo.”
23 And whanne a parable was takun, he spak eft, Alas! who schal lyue, whanne the Lord schal make thes thingis?
Ndipo ananenanso uthenga wina kuti, “Aa, ndani adzakhala ndi moyo Mulungu akachita zimenezi?
24 Thei schulen come in grete schippis fro Ytalie, thei schulen ouercome Assiries, and thei schulen distrie Ebrews, and at the last also thei hem silf schulen perische.
Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu; kupondereza Asuri ndi Eberi, koma iwonso adzawonongeka.”
25 And Balaam roos, and turnide ayen in to his place; and Balaach yede ayen bi the weye in which he cam.
Pamenepo Balaamu ananyamuka ndi kubwerera kwawo ndipo Balaki anapitanso njira yake.

< Numbers 24 >