< Numbers 17 >

1 And the Lord spak to Moises, `and seide, Speke thou to the sones of Israel,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 and take thou yerdis, bi her kynredis, bi ech kynrede o yeerde, take thou of alle the princes of the lynagis twelue yerdis; and thou schalt write the name of each lynage aboue his yerde;
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
3 forsothe the name of Aaron schal be in the lynage of Leuy, and o yerde schal conteyne alle the meynees of hem.
Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
4 And thou schalt putte tho yerdis in the tabernacle of boond of pees, bifor the witnessyng, where Y schal speke to thee; the yerde of hym schal buriowne, whom Y schal chese of hem;
Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
5 and Y schal refreyne fro me the playnyngis of the sones of Israel, bi whiche thei grutchen ayens you.
Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
6 And Moyses spak to the sones of Israel; and alle princes yauen to hym yerdis, bi alle lynagis; and the yerdis weren twelue, without the yerde of Aaron.
Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
7 And whanne Moises hadde put tho yerdis bifor the Lord, in the tabernacle of witnessyng, he yede ayen in the day suynge,
Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
8 and founde that the yerde of Aaron, `in the hows of Leuy, buriounnede; and whanne knoppis weren greet, the blossoms `hadden broke out, whiche weren alargid in leeuys, and weren fourmed in to alemaundis.
Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
9 Therfor Moyses brouyte forth alle the yerdis fro the siyt of the Lord to al the sones of Israel; and thei sien, and resseyueden ech his yerde.
Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
10 And the Lord seide to Moises, Bere ayen the yerde of Aaron in to the tabernacle of witnessyng, that it be kept there in to `the signe of the rebel sones of Israel, and that her `playntis reste fro me, lest thei dien.
Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
11 And Moises dide, as the Lord comaundide.
Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
12 Forsothe the sones of Israel seiden to Moises, Lo! we ben wastid, alle we perischiden;
Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
13 who euer neiyeth to the tabernacle of the Lord, he dieth; whethir we schulen be doon awei alle `til to deeth?
Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”

< Numbers 17 >