< Numbers 13 >

1 And there the Lord spak to Moises,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 and seide, Sende thou men that schulen biholde the lond of Canaan, which Y schal yyue to the sones of Israel, of ech lynage o man of the princes.
“Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
3 Moises dide that that the Lord comaundide, and sente fro the deseert of Pharan princes, men of whiche these ben the names.
Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
4 Of the lynage of Ruben, Semmya, the sone of Zectur.
Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
5 Of the lynage of Symeon, Saphat, the sone of Hury.
kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
6 Of the lynage of Juda, Caleph, the sone of Jephone.
kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
7 Of the lynage of Isachar, Igal, the sone of Joseph.
kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
8 Of the lynage of Effraym, Osee, the sone of Nun.
kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
9 Of the lynage of Beniamyn, Phalti, the sone of Raphu.
kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
10 Of the lynage of Zabulon, Gediel, the sone of Sodi.
kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
11 Of the lynage of Joseph, of the gouernaunce of Manasses, Gaddi, the sone of Susy.
kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
12 Of the lynage of Dan, Amyel, the sone of Gemalli.
kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
13 Of the lynage of Aser, Sur, the sone of Mychael.
kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
14 Of the lynage of Neptalym, Nabdi, the sone of Napsi.
kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
15 Of the lynage of Gad, Guel, the sone of Machi.
kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
16 These ben the names of men, which Moises sente to biholde the lond of Canaan; and he clepide Osee, the sone of Nun, Josue.
Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
17 Therfor Moises sente hem to biholde the lond of Canaan, and seide to hem, `Stie ye bi the south coost; and whanne ye comen to the hillis,
Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
18 biholde ye the lond, what maner lond it is; and biholde ye the puple which is the dwellere therof, whether it is strong, ethir feble, `whether thei ben fewe in noumbre, ether manye;
Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
19 whether that lond is good, ethir yuel; what maner citees ben, wallid, ether without wallis;
Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
20 whether the lond is fat, ether bareyn, `whether it is ful of woodis, ethir without trees. Be ye coumfortid, and `brynge ye to vs of the fruytis of that lond. Sotheli the tyme was, whanne grapis first ripe myyten be etun thanne.
Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
21 And whanne thei hadden stied, thei aspieden the lond, fro the deseert of Syn `til to Rohob, as men entryth to Emath.
Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
22 And thei stieden to the south, and camen in to Ebron, where Achyman, and Sisai, and Tholmai, the sones of Enach, weren; for Hebron was maad bi seuen yeer bifor Thamnys, the citee of Egipt.
Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
23 And thei yeden til to the stronde of clustre, and kittiden doun a sioun with his grape, which twei men baren in a barre; also thei token of pumgarnadis, and of the figis of that place which is clepid Nehelescol,
Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
24 that is, the stronde of grape, for the sones of Israel baren a clustre fro thennus.
Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
25 And the aspieris of the lond, whanne thei hadden cumpassid al the cuntrey, after fourti daies camen to Moises and Aaron,
Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
26 and to al the cumpany of the sones of Israel, in to the deseert of Pharan which is in Cades. And `the aspieris spaken to hem, and schewiden the fruytis of the lond to al the multitude, and telden,
Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
27 and seiden, We camen to the lond, to which thou sentest vs, which lond treuli flowith with mylk and hony, as it may be knowun bi these fruytis;
Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
28 but it hath strongeste inhabiteris, and grete cytees, and wallid; we sien there the kynrede of Anachym; Amalech dwellith in the south;
Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
29 Ethei, and Jebusei, and Amorey dwellen in the hilli placis; forsothe Cananey dwellith bisidis the see, and bisidis the floodis of Jordan.
Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
30 Among thes thingis Caleph peeside the grutchyng of the puple, that was maad ayens Moises, and seide, `Stie we, and welde we the lond, for we moun gete it.
Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
31 Forsothe other aspieris, that weren with hym, seiden, We moun not stie to this puple, for it is strongere than we.
Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
32 And thei deprauyden the lond which thei hadden biholde, anentis the sones of Israel, and seiden, The lond which we cumpassiden deuourith hise dwelleris; the puple which we bihelden is of large stature; there we syen summe wondris ayens kynde,
Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
33 of the sones of Enach, of the kynde of geauntis, to whiche we weren comparisound, and weren seien as locustis.
Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”

< Numbers 13 >