< Nehemiah 8 >

1 And the seuenthe monethe `was comun vndur Esdras and Neemye; sotheli the sones of Israel weren in her cytees. And al the puple was gaderid togydere as o man, to the street which is bifor the yate of watris. And thei seiden to Esdras, the scribe, that he schulde brynge the book of the lawe of Moises, which the Lord hadde comaundid to Israel.
Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
2 Therfor Esdras, the preest, brouyte the lawe bifor the multitude of men and of wymmen, and bifor alle that myyten vndurstonde, `in the firste day of the seuenth monethe.
Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
3 And he redde in it opynli in the street that was bifor the yate of watris, fro the morewtid `til to myddai, in the siyt of men and of wymmen and of wise men; and the eeris of al the puple weren reisid to the book.
Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
4 Forsothe Esdras the writere stood on the grees of tree, which he hadde maad to speke theron; and Mathatie, and Semma, and Ananye, and Vrie, and Elchie, and Maasie stoden bisidis hym at his riyt half; and Phadaie, Mysael, and Melchie, Assum, and Aseph, Dana, and Zacharie, and Mosollam stoden at the left half.
Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
5 And Esdras openyde the book bifor al the puple; for he apperide ouer al the puple; and whanne he hadde openyd the book, al the puple stood.
Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
6 And Esdras blesside the Lord God with greet vois; and al the puple answeride, Amen, Amen, reisynge her hondis. And thei weren bowid, and thei worschipiden God, lowli on the erthe.
Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
7 Forsothe Josue, and Baany, and Serebie, Jamyn, Acub, Septhai, Odia, Maasie, Celitha, Ayarie, Jozabeth, Anan, Phallaie, dekenes, maden silence in the puple for to here the lawe. Sotheli the puple stood in her degree.
Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
8 And thei redden in the book of Goddis lawe distinctli, `ether atreet, and opynli to vndurstonde; `and thei vndurstoden, whanne it was red.
Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
9 Forsothe Neemye seide, he is Athersata, and Esdras, the preest and writere, and the dekenes, expownynge to al the puple, It is a dai halewid to `oure Lord God; nyle ye morne, and nyle ye wepe. For al the puple wepte, whanne it herde the wordis of the lawe.
Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
10 And he seide to hem, Go ye, and `ete ye fatte thingis, and drynke ye wiyn `maad swete with hony, and sende ye partis to hem, that maden not redi to hem silf, for it is an hooli dai of the Lord; `nyle ye be sory, for the ioye of the Lord is youre strengthe.
Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
11 Sotheli the dekenes maden silence in al the puple, and seiden, Be ye stille, for it is an hooli dai, and `nyle ye make sorewe.
Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
12 Therfor al the puple yede for to ete, and drynke, and to sende partis, and `to make greet gladnesse; for thei vndurstoden the wordis, whiche he hadde tauyt hem.
Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
13 And in the secound dai the princes of meynees, alle the puplis, prestis, and dekenes, weren gaderid togidere to Esdras, the writere, that he schulde expowne to hem the wordis of the lawe.
Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
14 And thei foundun writun in the lawe, that the Lord comaundide `in the hond of Moyses, that the sones of Israel dwelle in tabernaclis in the solempne dai, in the seuenthe moneth;
Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
15 and that thei preche, and pupplische a vois in alle her citees, and in Jerusalem; and seie, Go ye out in to the hil, and brynge ye bowis of olyue, and bowis of the faireste tree, the bowis of a myrte tree, and the braunchis of a palm tree, and the bowis of a `tree ful of wode, that tabernaclis be maad, as it is writun.
Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
16 And al the puple yede out, and thei brouyten, and maden to hem silf tabernaclis, `ech man in `his hows roof, and in her stretis, `ether foryerdis, and in the large placis of Goddis hows, and in the street of the yate of watris, and in the street of the yate of Effraym.
Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
17 Therfor al the chirche of hem, that camen ayen fro caytifte, made tabernaclis, and thei dwelliden in tabernaclis. For the sones of Israel hadden not do siche thingis fro the daies of Josue, sone of Nun, `til to that dai; and ful greet gladnesse was.
Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
18 Forsothe Esdras radde in the book of Goddis lawe bi alle daies, fro the firste dai `til to the laste dai; and thei maden solempnytee bi seuene daies, and in the eiyte day thei maden a gaderyng of siluer, `bi the custom.
Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.

< Nehemiah 8 >