< Micah 6 >

1 Here ye whiche thingis the Lord spekith. Rise thou, stryue thou bi doom ayens mounteyns, and litle hillis here thi vois.
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 Mounteyns, and the stronge foundementis of erthe, here the doom of the Lord; for the doom of the Lord with his puple, and he schal be demyd with Israel.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 Mi puple, what haue Y don to thee, ether what was Y greuouse to thee? Answere thou to me.
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 For Y ledde thee out of the lond of Egipt, and of the hous of seruage Y delyuerede thee; and Y sente bifore thi face Moises, and Aaron, and Marye.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 My puple, bithenke, Y preie, what Balaac, kyng of Moab, thouyte, and what Balaam, sone of Beor, of Sethym, answeride to hym til to Galgala, that thou schuldist knowe the riytwisnesse of the Lord.
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 What worthi thing schal Y offre to the Lord? schal Y bowe the knee to the hiye God? Whether Y schal offre to hym brent sacrifices, and calues of o yeer?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 Whether God mai be paid in thousyndis of wetheris, ether in many thousyndis of fatte geet buckis? Whether Y schal yyue my firste bigetun for my greet trespas, the fruyt of my wombe for synne of my soule?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 Y schal schewe to thee, thou man, what is good, and what the Lord axith of thee; forsothe for to do doom, and for to loue merci, and be bisi for to walke with thi God.
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 The vois of the Lord crieth to the citee, and heelthe schal be to alle men dredynge thi name. Ye lynagis, here; and who schal approue it?
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Yit fier is in the hous of the vnpitouse man, the tresouris of wickidnesse, and a lesse mesure ful of wraththe.
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Whether Y schal iustifie the wickid balaunce, and the gileful weiytis of litil sak,
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 in whiche riche men therof ben fillid with wickidnesse? And men dwellynge ther ynne spaken leesyng, and the tunge of hem was gileful in the mouth of hem.
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 And Y therfor bigan for to smyte thee, in perdicioun on thi synnes.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Thou schalt ete, and schalt not be fillid, and thi mekyng is in the middil of thee; and thou schalt take, and schalt not saue; and which thou schalt saue, Y schal yyue in to swerd.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Thou schalt sowe, and schal not repe; thou schalt trede the `frut of oliue, and schalt not be anoyntid with oile; and must, and schalt not drynke wyn.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 And thou keptist the heestis of Amry, and al the werk of the hous of Acab, and hast walkid in the lustis of hem, that Y schulde yyue thee in to perdicioun, and men dwellynge in it in to scornyng, and ye schulen bere the schenschipe of my puple.
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

< Micah 6 >