< Leviticus 19 >

1 The Lord spak to Moises, and seide,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speke thou to al the cumpenye of the sones of Israel, and thou schalt seie to hem, Be ye hooli, for Y am hooli, youre Lord God.
“Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Khalani oyera mtima chifukwa Ine, Yehova Mulungu wanu, ndine Woyera.
3 Ech man drede his fadir and his modir. Kepe ye my sabatis; Y am youre Lord God.
“‘Aliyense mwa inu azilemekeza abambo ake ndi amayi ake. Ndipo muzisunga masabata anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
4 Nyle ye be turned to ydols, nether ye schulen make to you yotun goddis; Y am youre Lord God.
“‘Musatembenukire ku mafano kapena kudzipangira nokha milungu ya zitsulo zosungunula. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 If ye offren a sacrifice of pesible thingis to the Lord, that it be quemeful,
“‘Pamene mukupereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, muyipereke mwanjira yoti ilandiridwe.
6 ye schulen ete it in that day, in which it is offrid, and in the tother dai; sotheli what euer thing is residue in to the thridde dai, ye schulen brenne in fier.
Nsembe izidyedwa tsiku lomwe mwayiperekalo kapena mmawa mwake. Chilichonse chotsala mpaka tsiku lachitatu chiyenera kutenthedwa.
7 If ony man etith therof aftir twei daes, he schal be vnhooli, and gilti of vnfeithfulnes `ether wickidnesse; and he schal bere his wickidnesse,
Ngati mudya choperekacho tsiku lachitatu, ndiye kuti mwachita chonyansa ndipo chakudyacho sichidzalandiridwa.
8 for he defoulide the hooli thing of the Lord, and his soule schal perische fro his puple.
Munthu aliyense amene adya chakudyacho adzasenza machimo ake chifukwa wayipitsa chinthu chimene ndi choyera kwa Yehova. Munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.
9 Whanne thou schalt repe the fruytis of thi lond, thou schalt not kitte `til to the ground the corn of the lond, nether thou schalt gadere the eeris of corn that ben left;
“‘Pamene mukolola zinthu mʼmunda mwanu musakolole mpaka mʼmphepete mwa munda, ndipo musatole khunkha lake.
10 nethir in thi vyner thou schalt gadere reysyns and greynes fallynge doun, but thou schalt leeue to be gaderid of pore men and pilgryms; Y am youre Lord God.
Musakolole mphesa zonse mʼmunda wanu wa mpesa kapena kutola mphesa zakugwa mʼmundamo. Zimenezi muzisiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wako.
11 Ye schulen not do thefte. Ye schulen not lye, and no man disseyue his neiybour.
“‘Musabe. “‘Musamanamizane. “‘Musachitirane zinthu mwachinyengo.
12 Thou schalt not forswere in my name, nethir thou schalt defoule the name of thi God; Y am the Lord.
“‘Musalumbire mʼdzina langa monyenga popeza kutero ndi kuyipitsa dzina la Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
13 Thou schalt not make fals chalenge to thi neiybore, nethir thou schalt oppresse hym bi violence. The werk of thin hirid man schal not dwelle at thee til the morewtid.
“‘Musapsinje mnzanu kapena kumulanda zinthu zake. “‘Musasunge malipiro a munthu wantchito usiku wonse mpaka mmawa.
14 Thou schalt not curse a deef man, nether thou schalt sette an hurtyng bifor a blynd man; but thou schalt drede thi Lord God, for Y am the Lord.
“‘Musatemberere wosamva kapena kuyikira munthu wosaona chinthu choti apunthwe nacho patsogolo pake, koma muziopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
15 Thou schalt not do that, that is wickid, nether thou schalt deme vniustli; biholde thou not the persoone of a pore man, nethir onoure thou the face of a myyti man; deme thou iustli to thi neiybore.
“‘Musamaweruze mopanda chilungamo. Musachite tsankho pakati pa osauka ndi olemera, koma muweruze mlandu wa mnzanu mwachilungamo.
16 Thou schalt not be a sclaunderere, nether a priuey bacbitere in the puplis; thou schalt not stonde ayens the blood of thi neiybore; Y am the Lord.
“‘Musamapite uku ndi uku kunena bodza pakati pa anthu anu. “‘Musachite kanthu kalikonse kamene kangadzetse imfa kwa mnzanu. Ine ndine Yehova.
17 Thou schalt not hate thi brothir in thin herte, but repreue hym opynly, lest thou haue synne on hym.
“‘Musamude mʼbale wanu mu mtima mwanu. Koma mudzudzuleni mnzanu moona mtima kuti musakhale wolakwa.
18 Thou schalt not seke veniaunce, nether thou schalt be myndeful of the wrong of thi cyteseyns; thou schalt loue thi freend as thi silf; Y am the Lord.
“‘Musamubwezere mnzanu choyipa kapena kumusungira kanthu kunkhosi, koma konda mnansi wako monga iwe mwini. Ine ndine Yehova.
19 Kepe ye my lawis. Thou schalt not make thi beestis to gendre with the lyuynge beestis of another kynde. Thou schalt not sowe the feeld with dyuerse sede. Thou schalt not be clothid in a cloth, which is wouun of twei thingis.
“‘Muzisunga malangizo anga. “‘Tsono musamalole kuti ngʼombe zanu zikwerane ndi chiweto cha mtundu wina. “‘Ndiponso musamadzale mbewu za mitundu iwiri mʼmunda umodzi. “‘Musavale chovala chopangidwa ndi nsalu za mitundu iwiri.
20 If a man slepith with a womman by fleischly knowyng of seed, which womman is an `hand maide, ye, a noble womman of kyn, and netheles is not ayenbouyt bi prijs, nethir rewardid with fredom, bothe schulen be betun, and thei schulen not die, for sche was not fre.
“‘Ngati munthu agonana ndi kapolo wamkazi amene wafunsidwa mbeta ndi munthu wina, koma sanawomboledwe kapenanso kulandira ufulu wake, alangidwe. Koma onsewa asaphedwe, chifukwa mkaziyo anali asanalandire ufulu wake.
21 Sotheli the man for his trespas schal offre a ram to the Lord, at the dore of the tabernacle of witnessyng;
Koma mwamunayo abwere ndi nsembe yopepesera kupalamula kwa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna
22 and the preest schal preye for hym, and for his trespas, bifor the Lord; and the Lord schal be merciful to hym, and the synne schal be foryouun.
ndipo wansembe achite nayo mwambo wopepesera chifukwa cha kupalamula kumene anachita pamaso pa Yehova. Akatero tchimo lake lidzakhululukidwa.
23 Whanne ye han entrid in to the lond of biheest, and han plauntid therynne appil trees, ye schulen do awei the firste flouris; the applis whiche tho trees bryngen forth, schulen be vncleene to you, nethir ye schulen ete of tho.
“‘Mukadzalowa mʼdzikomo ndi kudzala mtengo wa mtundu uliwonse wa zipatso, zipatso zakezo mudzaziyese ngati zodetsedwa. Ndiye kuti kwa zaka zitatu zidzakhale zoletsedwa kwa inu. Musadzazidye nthawi imeneyi.
24 Forsothe in the fourthe yeer al the fruyt of tho trees schal be `halewid preiseful to the Lord;
Chaka chachinayi, zipatso zake zonse zidzakhala zopatulika, ndipo zidzakhala chopereka cha matamando kwa Yehova.
25 forsothe in the fifthe yeer ye schulen ete fruytis, and schulen gadere applis, whiche tho trees bryngen forth; Y am youre Lord God.
Koma chaka chachisanu, mudzatha kudya zipatso zake kuti mitengoyo idzakubalireni zochuluka. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26 Ye schulen not ete fleisch with blood. Ye schulen not make veyn diuynyng, nether ye schulen kepe dremes;
“‘Musadye nyama ya magazi. “‘Musamawombeze kapena kuchita zamatsenga.
27 nether ye schulen clippe the heer in round, nether ye schulen schaue the beerd;
“‘Musamamete mduliro kapena kumeta mʼmphepete mwa ndevu zanu.
28 and on deed men ye schulen not kitte youre fleischis, nether ye schulen make to you ony fyguris, ether markis in youre fleisch; Y am the Lord.
“‘Musadzichekecheke pathupi panu chifukwa cha munthu wakufa kapena kudzitema mphini pa thupi lanu. Ine ndine Yehova.
29 Sette thou not thi douytir to do leccherie for hire, and the lond be defoulid, and be fillid with synne.
“‘Musamuyipitse mwana wanu wamkazi pomusandutsa mkazi wachiwerewere. Mukatero dziko lidzasanduka la anthu achiwerewere ndi lodzaza ndi zoyipa.
30 Kepe ye my sabatis, and drede ye my seyntuarie; Y `am the Lord.
“‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga opatulika. Ine ndine Yehova.
31 Bowe ye not to astronomyers, nether axe ye ony thing of fals dyuynours, that ye be defoulid bi hem; Y am youre Lord God.
“‘Musamapite kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kapena kwa owombeza. Musamawafunefune kuti angakuyipitseni. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
32 Rise thou bifor an hoor heed, and onoure thou the persoone of an eld man, and drede thou thi Lord God; Y am the Lord.
“‘Muzikhala mwa ulemu pamaso pa munthu wachikulire, ndipo muzichitira ulemu munthu wokalamba. Kumeneko ndiye kuopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
33 If a comelyng enhabitith in youre lond, and dwellith among you, dispise ye not hym,
“‘Pamene mlendo akhala nanu mʼdziko mwanu, musamuzunze.
34 but be he among you as a man borun in the lond; and ye schulen loue hym as you silf, for also ye weren comelyngis in the lond of Egipt; Y am youre Lord God.
Mlendo amene akhala nanu akhale ngati mmodzi mwa mbadwa zanu. Mumukonde monga momwe mumadzikondera inu nomwe. Paja inu munali alendo mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
35 Nyle ye do ony wickid thing in doom, in reule, in weiyte, and in mesure; the balance be iust,
“‘Musamachite za chinyengo poweruza mlandu, kapena poyeza utali, kulemera ngakhalenso kuchuluka kwa zinthu.
36 and the weiytis be euene, the buschel be iust, and the sextarie be euene; Y am youre Lord God, that ladde you out of the lond of Egipt.
Miyeso ya sikelo, miyeso yoyezera kulemera kwa zinthu, miyeso yotchedwa efa ndi miyeso yotchedwa hini zikhale zolungama. Ine ndine Yehova, Mulungu wanu amene ndinakutulutsani ku dziko la Igupto.
37 Kepe ye alle myn heestis, and alle domes, and do ye tho; Y am the Lord.
“‘Choncho muzisunga malangizo ndi malamulo angawa ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.’”

< Leviticus 19 >