< Leviticus 10 >

1 And whanne Nadab and Abyu, the sones of Aaron, hadden take censeris, thei puttiden fier and encense aboue, and offriden bifor the Lord alien fier, which thing was not comaundid to hem.
Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
2 And fier yede out fro the Lord, and deuouride hem, and thei weren deed bifor the Lord.
Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
3 And Moises seide to Aaron, This thing it is which the Lord spak, Y schal be halewid in hem that neiyen to me, and Y schal be glorified in the siyt of al the puple; which thing Aaron herde, and was stille.
Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
4 Sotheli whanne Moises hadde clepid Mysael and Elisaphan, the sones of Oziel, brother of Aaron's fadir, he seide to hem, Go ye, and take awey youre britheren fro the siyt of seyntuarie, and bere ye out of the castels.
Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
5 And anoon thei yeden, and token hem, as thei laien clothid with lynnun cootis, and castiden out, as it was comaundid to hem.
Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
6 And Moises spak to Aaron, and to Eliasar and Ithamar, the sones of Aaron, Nyle ye make nakid youre heedis, and nyle ye reende clothis, lest perauenture ye dien, and indignacioun rise on al the cumpany; youre britheren and all the hows of Israel byweile the brennyng which the Lord reiside.
Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
7 But ye schulen not go out of the yatis of the tabernacle, ellis ye schulen perische; for the oile of hooli anoyntyng is on you. Whiche diden alle thingis bi the comaundement of Moises.
Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
8 Also the Lord seide to Aaron,
Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
9 Thou and thi sones schulen not drynke wyn, and al thing that may make drunkun, whanne ye schulen entre in to the tabernacle of witnessing, lest ye dien; for it is euerlastynge comaundement in to youre generaciouns,
“Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
10 that ye haue kunnyng to make doom bytwixe hooli thing and vnhooli, bitwixe pollutid thing and cleene;
Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
11 and that ye teche the sones of Israel alle my lawful thingis, whiche the Lord spak to hem bi the hond of Moyses.
ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
12 And Moises spak to Aaron, and to Eliazar and Ythamar, hise sones, that weren residue, Take ye the sacrifice that lefte of the offryng of the Lord, and ete ye it with out sour dow, bisidis the auter, for it is hooli `of the noumbre of hooli thingis.
Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
13 Sotheli ye schulen ete in the hooli place that that is youun to thee and to thi sones, of the offryngis of the Lord, as it is comaundid to me Also thou,
Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
14 and thi sones, and thi douytris with thee, schulen ete in the clenneste place the brest which is offrid, and the schuldur which is departid; for tho ben kept to thee and to thi fre sones, of the heelful sacrifices of the sones of Israel;
Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
15 for thei reiseden bifor the Lord the schuldur and brest, and the ynnere fatnessis that ben brent in the auter; and perteynen tho to thee, and to thi sones, bi euerlastynge lawe, as the Lord comaundide.
Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
16 Among these thingis whanne Moises souyte the `buk of geet that was offrid for synne, he foond it brent, and he was wrooth ayens Eliazar and Ythamar, `the sones of Aaron that weren left.
Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
17 And he seide, Whi eten not ye the sacrifice for synne in the hooli place, which sacrifice is hooli `of the noumbre of hooli thingis, and is youun to you, that ye bere the wickydnesse of the multitude, and preye for it in the siyt of the Lord;
“Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
18 moost sithen of the blood therof is not borun yn with ynne hooli thingis, and ye ouyten ete it in the seyntuarie, as it is comaundid to me?
Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
19 And Aaron answeride, Sacrifice for synne, and brent sacrifice is offrid to dai bifor the Lord; sotheli this that thou seest, bifelde to me; how myyte Y ete it, ether plese God in cerymonyes with soreuful soule?
Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
20 And whanne Moises hadde herd this, he resseyuede satisfaccioun.
Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.

< Leviticus 10 >