< Lamentations 3 >

1 Aleph. I am a man seynge my pouert in the yerde of his indignacioun.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 Aleph. He droof me, and brouyte in to derknessis, and not in to liyt.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 Aleph. Oneli he turnede in to me, and turnede togidere his hond al dai.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 Beth. He made eld my skyn, and my fleisch; he al to-brak my boonys.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 Beth. He bildid in my cumpas, and he cumpasside me with galle and trauel.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 Beth. He settide me in derk places, as euerlastynge deed men.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 Gymel. He bildide aboute ayens me, that Y go not out; he aggregide my gyues.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Gymel. But and whanne Y crie and preye, he hath excludid my preier.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 Gymel. He closide togidere my weies with square stoonus; he distriede my pathis.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 Deleth. He is maad a bere settinge aspies to me, a lioun in hid places.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 Deleth. He distriede my pathis, and brak me; he settide me desolat.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Deleth. He bente his bowe, and settide me as a signe to an arowe.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 He. He sente in my reynes the douytris of his arowe caas.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 He. Y am maad in to scorn to al the puple, the song of hem al dai.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 He. He fillide me with bitternesses; he gretli fillide me with wermod.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 Vau. He brak at noumbre my teeth; he fedde me with aische.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 Vau. And my soule is putte awei; Y haue foryete goodis.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Vau. And Y seide, Myn ende perischide, and myn hope fro the Lord.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Zai. Haue thou mynde on my pouert and goyng ouer, and on wermod and galle.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Zai. Bi mynde Y schal be myndeful; and my soule schal faile in me.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Zai. Y bithenkynge these thingis in myn herte, schal hope in God.
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 Heth. The mercies of the Lord ben manye, for we ben not wastid; for whi hise merciful doyngis failiden not.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Heth. Y knew in the morewtid; thi feith is miche.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Heth. My soule seide, The Lord is my part; therfor Y schal abide hym.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 Teth. The Lord is good to hem that hopen in to hym, to a soule sekynge hym.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 Teth. It is good to abide with stilnesse the helthe of God.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 Teth. It is good to a man, whanne he hath bore the yok fro his yongthe.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 Joth. He schal sitte aloone, and he schal be stille; for he reiside hym silf aboue hym silf.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Joth. He schal sette his mouth in dust, if perauenture hope is.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Joth. He schal yyue the cheke to a man that smytith hym; he schal be fillid with schenschipis.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 Caph. For the Lord schal not putte awei with outen ende.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 Caph. For if he castide awei, and he schal do merci bi the multitude of hise mercies.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Caph. For he makide not low of his herte; and castide not awei the sones of men. Lameth.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 That he schulde al to-foule vndur hise feet alle the boundun men of erthe. Lameth.
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 That he schulde bowe doun the dom of man, in the siyt of the cheer of the hiyeste.
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 Lameth. That he schulde peruerte a man in his dom, the Lord knew not.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 Men. Who is this that seide, that a thing schulde be don, whanne the Lord comaundide not?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Men. Nether goodis nether yuels schulen go out of the mouth of the hiyeste.
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Men. What grutchide a man lyuynge, a man for hise synnes?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Nun. Serche we oure weies, and seke we, and turne we ayen to the Lord.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Nun. Reise we oure hertis with hondis, to the Lord in to heuenes.
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 Nun. We han do wickidli, and han terrid thee to wraththe; therfor thou art not able to be preied.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 Sameth. Thou hilidist in stronge veniaunce, and smitidist vs; thou killidist, and sparidist not.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 Sameth. Thou settidist a clowde to thee, that preier passe not.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Sameth. Thou settidist me, drawing vp bi the roote, and castynge out, in the myddis of puplis.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 Ayn. Alle enemyes openyden her mouth on vs.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Ayn. Inward drede and snare is maad to vs, profesie and defoulyng.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Ayn. Myn iyen ledden doun departyngis of watris, for the defoulyng of the douyter of my puple.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 Phe. Myn iye was turmentid, and was not stille; for no reste was.
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 Phe. Vntil the Lord bihelde, and siy fro heuenes.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Phe. Myn iye robbide my soule in alle the douytris of my citee.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 Sade. Myn enemyes token me with out cause, bi huntyng as a brid.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Sade. My lijf slood in to a lake; and thei puttiden a stoon on me.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Sade. Watris flowiden ouer myn heed; Y seide, Y perischide.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 Coph. Lord, Y clepide to help thi name, fro the laste lake.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Coph. Thou herdist my vois; turne thou not awei thin eere fro my sobbyng and cries.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Coph. Thou neiyidist to me in the dai, wherynne Y clepide thee to help; thou seidist, Drede thou not.
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 Res. Lord, ayenbiere of my lijf, thou demydist the cause of my soule.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Res. Lord, thou siest the wickidnesse of hem ayens me; deme thou my doom.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Res. Thou siest al the woodnesse, alle the thouytis of hem ayenus me.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 Syn. Lord, thou herdist the schenshipis of hem; alle the thouytis of hem ayens me.
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 Syn. The lippis of men risynge ayens me, and the thouytis of hem ayens me al dai.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Syn. Se thou the sittynge and risyng ayen of hem; Y am the salm of hem.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 Thau. Lord, thou schalt yelde while to hem, bi the werkis of her hondis.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Tau. Thou schalt yyue to hem the scheeld of herte, thi trauel.
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Tau. Lord, thou schalt pursue hem in thi strong veniaunce, and thou schalt defoule hem vndur heuenes.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Lamentations 3 >