< Judges 8 >

1 And the men of Effraym seiden to hym, What is this thing, which thou woldist do, that thou clepidist not vs, whanne thou yedist to batel ayens Madian? And thei chidden strongli, and almest diden violence.
Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.
2 To whiche he answeride, `What sotheli siche thing myyte Y do, what maner thing ye diden? Whethir a reisyn of Effraym is not betere than the vindagis of Abiezer?
Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita?
3 And the Lord bitook in to youre hondis the princes of Madian, Oreb and Zeb. What sich thing myyte Y do, what maner thing ye diden? And whanne he hadde spoke this thing, the spirit of hem restide, bi which thei bolneden ayens hym.
Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.
4 And whanne Gedeon hadde come to Jordan, he passide it with thre hundrid men, that weren with hym; and for weerynesse thei myyten not pursue hem that fledden.
Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo.
5 And he seide to the men of Socoth, Y biseche, yyue ye looues to the puple, which is with me; for thei failiden greetli, that we moun pursue Zebee and Salmana, kyngis of Madian.
Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”
6 The princes of Socoth answeriden in scorne, In hap the pawmes of the hondis of Zebee and of Salmana ben in thin hond, and therfor thou axist, that we yyue looues to thin oost.
Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”
7 To whiche he seide, Therfor, whanne the Lord schal bitake Zebee and Salmana in to myn hondis, and whanne Y schal turne ayen ouercomere in pees, Y schal to-reende youre fleischis with the thornes and breris of deseert.
Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”
8 And he stiede fro thennus, and cam in to Phanuel; and he spak lijk thingis to men of that place, to whom also thei answeriden, as the men of Socoth hadden answerid.
Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja.
9 And so he seide to hem, Whanne Y schal turne ayen ouercomere in pees, Y schal distrie this tour.
Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”
10 Forsothe Zebee and Salmana restiden with al her oost; for fiftene thousynde men leften of alle the cumpenyes of the `puplis of the eest, whanne an hundrid and twenti thousynde of `fiyteris and of men drawynge out swerd weren slayn.
Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000.
11 And Gedeon stiede bi the weye of hem that dwelliden in tabernaclis at the eest coost of Nobe and of Lethoa, and smoot the `tentis of enemyes, that weren sikur, and supposiden not ony thing of aduersite.
Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera.
12 And Zebee and Salmana fledden, whiche Gedeon pursuede and took, whanne al `the oost of hem was disturblid.
Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.
13 And he turnede ayen fro batel bifor the `risyng of the sunne,
Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi.
14 and took a child of the men of Socoth; and he axide hym the names of the princes and eldere men of Socoth; and he descryuede seuene and seuenti men in noumbre.
Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti.
15 And he cam to Socoth, and seide to hem, Lo Zebee and Salmana! of whiche ye vpbreideden me, and seiden, In hap the hondis of Zebee and of Salmana ben in thin hondis, and therfor thou axist, that we yyue looues to men, that ben weeri and failiden.
Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’”
16 Therfor Gedeon took the eldere men of the citee, and thornes and breris of deseert, and he to-rente with tho, and al to-brak the men of Socoth; also he destriede the tour of Phanuel,
Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo.
17 whanne the dwelleris of the citee weren slayn.
Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.
18 And he seide to Zebee and Salmana, What maner men weren thei, whiche ye killiden in Thabor? Whiche answeriden, Thei weren lijk thee, and oon of hem was as the sone of a kyng.
Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?” Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”
19 To whiche he seide, Thei weren my britheren, the sones of my modir; the Lord lyueth, if ye hadden saued hem, Y `nolde sle you.
Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.”
20 And he seide to Jepther, his firste gendrid sone, Rise thou, and sle hem. Which drow not swerd; for he dredde, for he was yit a child.
Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.
21 And Zebee and Salmana seiden, Ryse thou, and falle on vs; for thou art bi the age and strengthe of man. Gedeon roos, and killide Zebee and Salmana, and took the ournementis, and bellis, with whiche the neckis of kyngis camels ben wont to be maad fair.
Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.
22 And alle the men of Israel seiden to Gedeon, Be thou lord of vs, thou, and thi sone, and the sone of thi sone; for thou deliueridist vs fro the hond of Madian.
Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”
23 To whiche he seide, Y schal not be lord of you, nethir my sone schal be lord on you, but the Lord schal be lord.
Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.”
24 And he seide to hem, Y axe oon axyng of you, yyue ye to me the eere ryngis of youre prey; for Ismaelitis weren wont to haue goldun eere ryngis.
Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).
25 Whiche answeriden, We schulen yyue moost gladli. And thei spredden forth a mentil on the erthe, and castiden forth therynne `eere ryngis of the prey;
Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha.
26 and the weiyte of `eere ryngis axid was a thousynde and seuene hundrid siclis of gold, with out ournementis and brochis and cloth of purpur, whiche the kyngis of Madian weren wont to vse, and outakun goldun bies of camels.
Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo.
27 And Gedeon made therof ephot, that is, a preestis cloth, `and propir cloth of the hiyeste preest, and he puttide it in his citee Ephra; and al Israel diden fornycacioun, `that is ydolatrye, ther ynne; and it was maad to Gedeon and to al his hows in to fallyng.
Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.
28 Forsothe Madian was maad low bifor the sones of Israel, and thei myyten no more reise nollis; but the lond restide fourti yeer, in whiche Gedeon was souereyn.
Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.
29 And so Jerobaal, sone of Joas, yede, and dwellide in his hows;
Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo.
30 and he hadde seuenti sones, that yeden out of his thiy, for he hadde many wyues.
Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri.
31 Forsothe a concubyn, `that is, secoundarie wijf, of hym, whom he hadde in Sichem, gendride to hym a sone, Abymelech bi name.
Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki.
32 And Gedeon, sone of Joas, diede in good elde, and was biried in the sepulcre of Joas, his fadir, in Ephra, of the meynee of Ezri.
Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.
33 Forsothe aftir that Gedeon was deed, the sones of Israel turneden awey `fro Goddis religioun, and diden fornycacioun, `that is, idolatrie, with Baalym; and thei smytiden boond of pees with Baal, that he schulde be to hem in to God,
Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo.
34 nether thei hadden mynde of her Lord God, that delyuerede hem fro the hond of alle her enemyes `bi cumpas;
Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse.
35 nether thei diden merci with the hous of Gerobaal Gedeon, bi alle the goodis whiche he `hadde do to Israel.
Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.

< Judges 8 >