< Judges 17 >

1 In that tyme was a man, `Mycas bi name, of the hil of Effraym.
Munthu wina dzina lake Mika wochokera ku dziko la mapiri la Efereimu anawuza amayi ake kuti
2 And he seide to his modir, Lo! Y haue a thousynde `and an hundrid platis of siluer, whiche thou departidist to thee, and on whiche thou sworist, while Y herde, and tho ben at me. To whom sche answeride, Blessid be my sone of the Lord.
“Ndinamva inu mukutemberera munthu amene anaba ndalama zanu zasiliva 1,100. Ndalamazo zili ndi ine, ndinatenga ndine.” Pamenepo amayi akewo anati, “Yehova akudalitse mwana wanga!”
3 Therefor he yeldide tho to his modir; and sche seide to hym, Y halewide and avowide this siluer to the Lord, that my sone resseyue of myn hond, and make a grauun ymage and a yotun ymage; and now I `yyue it to thee.
Choncho Mika anabweza ndalama 1,100 za siliva kwa amayi ake, ndipo amayi akewo anati, “Ine ndapatulira Yehova ndalama za silivazi kuti mwana wanga aseme fano ndi kulikuta ndi siliva. Ndiye tsopano ndikubwezera ndalamazo.”
4 Therfor he yeldide to his modir; and sche took twei hundryd platis of siluer, and yaf tho to a werk man of siluer, that he schulde make of tho a grauun `ymage and yotun, that was in `the hows of Mycas.
Tsono Mika atabweza ndalama zija kwa amayi ake, iwo anatengapo ndalama za siliva 200 namupatsa mmisiri wosula siliva. Iye anakonza fano, nasungunula siliva uja ndi kulikutira fano lija. Ndipo Mika anayika fanolo mʼnyumba mwake.
5 Which departide also a litil hous ther ynne to God; and made ephod, and theraphym, that is, a preestis cloth, and ydols; and he fillide the hond of oon of his sones, and he was maad a preest to hym.
Mikayu anali ndi kachisi, ndipo anapanga efodi ndi mafano otchedwa terafimu. Anapatula mwana wake mmodzi kuti akhale wansembe.
6 In tho daies was no kyng in Israel, but ech man dide this, that semyde riytful to hym silf.
Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense amachita zomwe zinamukomera.
7 Also another yonge wexynge man was of Bethleem of Juda, of the kynrede therof, `that is, of Juda, and he was a dekene, and dwellide there.
Ku Betelehemu mʼdziko la Yuda kunali mnyamata wina amene anali wa fuko la Levi.
8 And he yede out of the citee of Bethleem, and wolde be a pilgrim, where euere he foond profitable to hym silf. And whanne he made iourney, and `hadde come in to the hil of Effraym, and hadde bowid a litil in to `the hows of Mycha,
Iyeyu anachoka mu mzinda wa Betelehemu uja ku Yuda kukafuna malo ena okhala. Akuyenda, anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ku nyumba ya Mika.
9 `he was axid of hym, Fro whennus comest thou? Which answeride, Y am a dekene of Bethleem of Juda, and Y go, that Y dwelle where Y may, and se that it is profitable to me.
Tsono Mika anamufunsa kuti, “Mukuchokera kuti?” Ndipo iye anayakha kuti, “Ndine Mlevi wochokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Ndikufunafuna malo okhala.”
10 Micha seide, Dwelle thou at me, and be thou fadir and preest `to me; and Y schal yyue to thee bi ech yeer ten platis of siluer, and double cloth, and tho thingis that ben nedeful to lijflode.
Tsono Mika anati kwa iye, “Khalani ndi ine. Mukhale ngati mlangizi wanga ndi wansembe, ndipo ine ndizikupatsani ndalama za siliva khumi pa chaka komanso zovala ndi zakudya.”
11 He assentide, and dwellide `at the man; and he was to the man as oon of sones.
Choncho Mleviyo anavomera kuti azikhala naye, ndipo mnyamatayo anakhala ngati mmodzi mwa ana ake aamuna.
12 And Mycha fillide his hond, and hadde the child preest at hym,
Pambuyo pake Mika anapatula Mleviyo ndipo mnyamatayu anakhala wansembe. Tsono ankakhala mʼnyumba ya Mika.
13 and seide, Now Y woot, that God schal do wel to me, hauynge a preest of the kyn of Leuy.
Ndipo Mika anati, “Tsopano ndadziwa kuti Yehova adzandikomera mtima chifukwa Mleviyu ndiye wakhala wansembe wanga.”

< Judges 17 >