< Judges 14 >

1 Therfor Sampson yede doun in to Thannatha, and he siy there a womman of `the douytris of Filisteis;
Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
2 and he stiede, and telde to his fadir and `to his modir, and seide, Y siy a womman in Thannatha of the `douytris of Filistees, and Y biseche, that ye take hir a wijf to me.
Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
3 To whom his fadir and modir seiden, Whether no womman is among the douytris of thi britheren and in al my puple, for thou wolt take a wijf of Filisteis, that ben vncircumcidid? And Sampson seide to his fadir, Take thou this wijf to me, for sche pleside myn iyen.
Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
4 Forsothe his fadir and modir wisten not, that the thing was don of the Lord; and that he souyte occasiouns ayens Filisteis; for in that tyme Filisteis weren lordis of Israel.
(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
5 Therfor Sampson yede doun with his fadir and modir in to Thannatha; and whanne thei hadden come to the vyneris of the citee, a fers and rorynge `whelp of a lioun apperide, and ran to Sampson.
Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
6 Forsothe the spirit of the Lord felde in to Sampson, and he to-rente the lioun, as if he `to-rendide a kide `in to gobetis, and outerli he hadde no thing in the hond; and he nolde schewe this to the fadir and modir.
Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
7 And he yede doun, and spak to the womman, that pleside hise iyen.
Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
8 And aftir summe daies he turnede ayen to take hir `in to matrimonye; and he `bowide awey to se the `careyn of the lioun; and lo! a gaderyng of bees was in the `mouth of the lioun, and `a coomb of hony.
Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
9 And whanne he hadde take it in hondis, he eet in the weie; and he cam to his fadir and modir, and yaf part `to hem, and thei eeten; netheles he nolde schewe to hem, that he hadde take hony of the `mouth of the lioun.
Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
10 And so his fadir yede doun to the womman, and made a feeste to his sone Sampson; for yonge men weren wont to do so.
Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
11 Therfor whanne the citeseyns of that place hadden seyn hym, thei yauen to hym thretti felowis, whiche schulen be with hym.
Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
12 To whiche Sampson spak, Y schal putte forth to you a probleme, `that is, a douyteful word and priuy, and if ye `asoilen it to me with ynne seuen daies of the feeste, Y schal yyue to you thretti lynnun clothis, and cootis `of the same noumbre; sotheli if ye moun not soyle,
Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
13 ye schulen yyue to me thretti lynnun clothis, and cootis `of the same noumbre. Whiche answeriden to hym, Sette forth the probleme, that we here it.
Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
14 And he seide to hem, Mete yede out of the etere, and swetnesse yede out of the stronge. And bi thre daies thei myyten not assoile the `proposicioun, that is, the resoun set forth.
Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
15 And whanne the seuenthe dai cam, thei seiden to `the wijf of Sampson, Glose thin hosebonde, and counseile hym, that he schewe to thee what the probleme signyfieth. That if thou nylt do, we schulen brenne thee and `the hous of thi fadir. Whether herfor ye clepiden vs to weddyngis, that ye schulden robbe vs?
Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
16 And sche schedde teerys at Sampson, and pleynede, and seide, Thou hatist me, and louest not, therfor thou nylt expowne to me the probleme, which thou settidist forth to the sones of my puple. And he answeride, Y nolde seie to my fadir and modir, and schal Y mow schewe to thee?
Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
17 Therfor bi seuene dayes of the feest sche wepte at hym; at the laste `he expownede in the seuenthe dai, whanne sche was diseseful to hym. And anoon sche telde to hir citeseyns.
Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
18 And thei seiden to hym in the seuenthe dai bifor the goyng doun of the sunne, What is swettere than hony, and what is strengere than a lioun? And he seide to hem, If ye hadden not erid in my cow calf, `that is, my wijf, ye hadden not founde my proposicioun.
Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
19 Therfor the spirit of the Lord felde in to hym; and he yede doun to Ascalon, and killyde there thretti men, whose clothis he took awey, and he yaf to hem that soiliden the probleme; and he was ful wrooth, and stiede in to `the hows of his fadir.
Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
20 Forsothe his wijf took an hosebonde, oon of the frendis and keperis `of hir.
Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

< Judges 14 >