< Joshua 19 >

1 And the secounde lot of the sones of Symeon yede out, bi her meynees; and the eritage of hem,
Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
2 in the myddis of possessioun of the sones of Juda, was Bersabee, and Sabee,
Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
3 and Melada, and Asersua, Bala,
Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
4 and Asem, and Betholaad, Bethularma, and Siceleth,
Elitoladi, Betuli, Horima,
5 and Bethmarchaboth, and Asersua,
Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
6 and Bethelebaoth, and Saroem, threttene citees, and `the townes of tho;
Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
7 Aym, and Remmon, and Athar, and Asam, foure citees, and `the townes of tho; alle the townes bi cumpas of these citees,
Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
8 `til to Balath Brameth, ayens the south coost, weren seuentene citees. This is the eritage of the sones of Symeon, bi her meynees,
Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
9 in the possessioun and part of the sones of Juda, for it was more; and therfor the sones of Symeon hadden possessioun in the myddis of the eritage therof.
Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
10 And the thridde lot of the sones of Zabulon felde, bi her meynees; and the terme of possessioun of the sones of Zabulon was maad `til to Sarith;
Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
11 and it stieth fro the see, and Medala; and it cometh in to Debbaseth, `til to the stronde which is ayens Jecenam;
Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
12 and it turneth ayen fro Sarith, ayens the eest, in to the coostis of Sechelech Tabor; and goith out to Daberth; and it stieth ayens Jasie;
Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
13 and fro thennus it passith to the eest coost to Gethefer, and Thacasym; and it goith out in to Remmon, Amphar, and Noa; and cumpassith to the north, and Nachon;
Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
14 and the goyngis out therof ben the valei of Jeptael,
Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
15 and Cathel, and Neamai, and Semrom, and Jedaba, and Bethleem, twelue citees, and `the townes of tho.
Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
16 This is the eritage of the lynage of the sones of Zabulon, bi her meynees, and the citees and `townes of tho.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
17 The fourthe lot yede out to Isacar, bi hise meynees; and the eritage therof was Jezrael,
Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
18 and Casseloth,
Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
19 and Symen, and Affraym, and Seon,
Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
20 and Anaarath, and Cabith, and Cesion, Hames,
Rabiti, Kisoni, Ebezi,
21 and Ramech, and Enganym, and Enadda, and Bethfeses.
Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
22 And the terme therof cometh `til to Tabor, and Seesyma, and Hethsemes; and the outgoyngis therof weren Jordan, sixtene citees, and `the townes of tho.
Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
23 This is the possessioun of the sones of Ysachar, bi her meynees, the citees and the townes of tho.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
24 And the fiuethe lot felde to the lynage of the sones of Aser, by her meynees;
Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
25 and the terme of hem was Alchat, and Adi, and Bethen,
Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
26 and Mesaph, and Elmelech, and Amaad, and Messal; and it cometh `til to Carmel of the see, and Sior, and Labanath; and it turneth ayen,
Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
27 ayens the eest, to Bethdagan; and passith `til to Zabulon, and to the valei of Jeptael, ayens the north, in Bethemeth, and Neyel; and it goith out to the left side to Gabul,
Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
28 and Acran, and Roob, and Omynon, and Chane, `til to grete Sidon;
Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
29 and it turneth ayen in to Horma, `til to the strongeste citee Tire, and `til to Ossam; and the outgoyngis therof schulen be in to the see, fro the part of Aczyma,
Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
30 and Affeth, and Roob; two and twenti citees, and `the townes of tho.
Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
31 This is the possessioun of the sones of Aser, bi her meynees, `the citees, and `townes of tho.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
32 The sixte lot of the sones of Neptalym felde, bi her meynees;
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
33 and the terme bigan of Heleth, and Helon, and Sannaira, and Adarny, `which is Neceb, and Jebnael, `til to Letum; and the outgoyng of hem til to Jordan;
Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
34 and the terme turneth ayen, ayens the west, in to Arnoth of Thabor; and fro thennus it goith out in to Hucota, and passith in to Zabulon, ayens the south, and in to Asor, ayens the west, and in to Juda, at Jordan, ayens the risyng of the sunne;
Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
35 of the strongeste citee Assydym, Ser, and Amraath,
Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
36 and Rechath, Cenereth, and Edema,
Adama, Rama, Hazori,
37 and Arama, Asor, and Cedes, and Edrai,
Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
38 Nason, and Jeron, and Magdael, Horem, and Bethanath, and Bethsemes; nyntene citees, and `the townes of tho.
Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
39 This is the possessioun of the lynage of the sones of Neptalym, bi her meynees, the citees, and the townes of tho.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
40 The seuenthe lot yede out to the lynage of the sones of Dan, bi her meynees;
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
41 and the terme of the possessioun therof was Saraa, and Ascahol, and Darsemes, that is, the citee of the sunne,
Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
42 Selenym, and Hailon, and Jethala,
Saalabini, Ayaloni, Itira,
43 Helom, and Thenna, and Acrom,
Eloni, Timna, Ekroni,
44 Helthecem, Jebtom, and Baalath, Lud,
Eliteke, Gibetoni, Baalati,
45 and Benebarach, and `Jethremmon, and Ihercon,
Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
46 and Arecon, with the terme that biholdith Joppen,
Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
47 and is closid with that ende. And the sones of Dan stieden, and fouyten ayens Lesem; and thei token it, and smytiden it bi the scharpnes of swerd, and hadden in possessioun, and dwelliden therynne; and thei clepiden the name therof Lesan Dan, by the name of Dan, her fadir.
Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
48 This is the possessioun of the lynage of Dan, bi her meynees, the citees, and townes of tho.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
49 And whanne thei hadden fillid to departe the lond bi lot to alle men bi her lynagis, the sones of Israel yauen possessioun to Josue, sone of Nun,
Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
50 in the myddis of hem, bi the comaundement of the Lord, the citee which he axide, Thannath Sara, in the hil of Effraym; and he bildide the citee, and dwellide therynne.
Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
51 These ben the possessiouns whiche Eleazar, preest, and Josue, sone of Nun, and the princis of meynees, and of the lynagis of the sones of Israel, departiden bi lot in Silo, bifor the Lord, at the dore of tabernacle of witnessing, and departiden the lond.
Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.

< Joshua 19 >