< John 17 >

1 These thingis Jhesus spak, and whanne he hadde cast vp hise iyen in to heuene, he seide, Fadir, the our cometh, clarifie thi sone, that thi sone clarifie thee.
Yesu atatha kunena izi, anayangʼana kumwamba ndipo anapemphera: “Atate, nthawi yafika. Lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanuyo akulemekezeni Inu.
2 As thou hast youun to hym power on ech fleisch, that al thing that thou hast youun to hym, he yyue to hem euerlastynge lijf. (aiōnios g166)
Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. (aiōnios g166)
3 And this is euerlastynge lijf, that thei knowe thee very God aloone, and whom thou hast sent, Jhesu Crist. (aiōnios g166)
Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. (aiōnios g166)
4 Y haue clarified thee on the erthe, Y haue endid the werk, that thou hast youun to me to do.
Ine ndabweretsa ulemerero wanu pa dziko pamene ndamaliza ntchito imene munandipatsa kuti ndi igwire.
5 And now, fadir, clarifie thou me at thi silf, with the clerenesse that Y hadde at thee, bifor the world was maad.
Ndipo tsopano, Atate, ndilemekezeni Ine pamaso panu ndi ulemerero uja umene ndinali nawo kwa Inu dziko lapansi lisanayambe.
6 Y haue schewid thi name to tho men, whiche thou hast youun to me of the world; thei weren thine, and thou hast youun hem to me, and thei han kept thi word.
“Ine ndawadziwitsa za Inu anthu amene munandipatsa mʼdziko lapansi. Iwo anali anu. Inu munawapereka kwa Ine ndipo amvera mawu anu.
7 And now thei han knowun, that alle thingis that thou hast youun to me, ben of thee.
Tsopano akudziwa kuti zonse zimene munandipatsa nʼzochokera kwa Inu.
8 For the wordis that thou hast youun to me, Y yaf to hem; and thei han takun, and han knowun verili, that Y wente out fro thee; and thei bileueden, that thou sentist me.
Pakuti Ine ndiwapatsa mawu amene Inu munandipatsa ndipo awalandira. Iwo akudziwa ndithu kuti Ine ndinachokera kwa Inu, ndipo akukhulupirira kuti Inu ndiye amene munandituma Ine.
9 Y preie for hem, Y preye not for the world, but for hem that thou hast youun to me, for thei ben thine.
Ine ndikuwapempherera. Ine sindikupempherera dziko lapansi, koma anthu amene Inu mwandipatsa, pakuti ndi anu.
10 And alle my thingis ben thine, and thi thingis ben myne; and Y am clarified in hem.
Zonse zimene Ine ndili nazo ndi zanu, ndipo zonse zimene Inu muli nazo ndi zanga. Choncho Ine ndalemekezedwa mwa iwowo.
11 And now Y am not in the world, and these ben in the world, and Y come to thee. Hooli fadir, kepe hem in thi name, whiche thou yauest to me, that thei ben oon, as we ben.
Ine sindikukhalanso mʼdziko lapansi nthawi yayitali, koma iwo akanali mʼdziko lapansi. Ine ndikubwera kwa Inu. Atate Woyera, atetezeni ndi mphamvu za dzina lanu. Dzina limene munandipatsa Ine, kuti iwo akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
12 While Y was with hem, Y kepte hem in thi name; thilke that thou yauest to me, Y kepte, and noon of hem perischide, but the sone of perdicioun, that the scripture be fulfillid.
Pamene ndinali nawo, ndinawateteza ndi kuwasunga mosamala mʼdzina limene munandipatsa. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatayika kupatula yekhayo amene anayenera kuwonongeka kuti malemba akwaniritsidwe.
13 But now Y come to thee, and Y speke these thingis in the world, that thei haue my ioie fulfillid in hem silf.
“Tsopano ndikubwera kwa Inu. Ndikunena izi ndikanali mʼdziko lapansi, kuti iwo akhale ndi muyeso wodzaza wachimwemwe changa mʼkati mwawo.
14 Y yaf to hem thi word, and the world hadde hem in hate; for thei ben not of the world, as Y am not of the world.
Ine ndawapatsa mawu anu ndipo dziko lapansi likudana nawo, pakuti sali a dziko lapansi monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
15 Y preye not, that thou take hem awei fro the world, but that thou kepe hem fro yuel.
Sindikupempha kuti muwachotse mʼdziko lapansi koma kuti muwateteze kwa woyipayo.
16 They ben not of the world, as Y am not of the world.
Iwo si a dziko lapansi, monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
17 Halewe thou hem in treuth; thi word is treuthe.
Ayeretseni ndi choonadi chanu. Mawu anu ndiye choonadi.
18 As thou sentist me in to the world, also Y sente hem `in to the world.
Monga Inu munandituma Ine mʼdziko lapansi, Inenso ndikuwatuma mʼdziko lapansi.
19 And Y halewe my silf for hem, that also thei ben halewid in treuthe.
Chifukwa cha iwowa Ine ndikudziyeretsa, kuti iwo ayeretsedwenso kwenikweni.
20 And Y preye not oneli for hem, but also for hem that schulden bileue in to me bi the word of hem;
“Ine sindikupempherera iwo okhawa, komanso amene adzandikhulupirira chifukwa cha uthenga wawo.
21 that all ben oon, as thou, fadir, in me, and Y in thee, that also thei in vs be oon; that the world bileue, that thou hast sent me.
Ndikuwapempherera kuti onsewa akhale amodzi. Monga Inu Atate muli mwa Ine ndi Ine mwa Inu, iwonso akhale mwa Ife kuti dziko lapansi likhulupirire kuti Inu munandituma Ine.
22 And Y haue youun to hem the clerenesse, that thou hast youun to me, that thei ben oon,
Ine ndawapatsa ulemerero umene munandipatsa Ine, kuti akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
23 as we ben oon; Y in hem, and thou in me, that thei be endid in to oon; and that the world knowe, that thou sentist me, and hast loued hem, as thou hast loued also me.
Ine ndikhale mwa iwo ndipo Inu mwa Ine kuti umodzi wawo ukhale wangwiro. Choncho dziko lapansi lidzadziwa kuti Inu munandituma Ine ndipo Inu mwawakonda iwowa monga momwe Inu munandikondera Ine.
24 Fadir, thei whiche thou yauest to me, Y wole that where Y am, that thei be with me, that thei see my clerenesse, that thou hast youun to me; for thou louedist me bifor the makyng of the world.
“Atate, Ine ndikufuna kuti anthu amene mwandipatsa Ine adzakhale ndi Ine kumene kuli Ine, ndi kuona ulemerero wanga, ulemerero umene munandipatsa chifukwa Inu munandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.
25 Fadir, riytfuli the world knew thee not, but Y knew thee, and these knewen, that thou sentist me.
“Atate wolungama, ngakhale kuti dziko lapansi silikudziwani Inu, Ine ndimakudziwani, ndipo iwo amadziwa kuti Inu munandituma Ine.
26 And Y haue maad thi name knowun to hem, and schal make knowun; that the loue bi which thou `hast loued me, be in hem, and Y in hem.
Ine ndawadziwitsa dzina lanu, ndipo ndidzapitiriza kuwadziwitsa dzina lanulo, kuti chikondi chomwe munandikonda nacho chikhale mwa iwo, ndipo Ine mwa iwo.”

< John 17 >