< John 14 >
1 Be not youre herte afraied, ne drede it; ye bileuen in God, and bileue ye in me.
“Mtima wanu usavutike. Khulupirirani Mulungu; khulupirirani Inenso.
2 In the hous of my fadir ben many dwellyngis; if ony thing lesse, Y hadde seid to you, for Y go to make redi to you a place.
Mʼnyumba mwa Atate anga muli zipinda zambiri. Kukanakhala kuti mulibemo ndikanakuwuzani. Ine ndikupita kumeneko kukakukonzerani malo.
3 And if Y go, and make redi to you a place, eftsoones Y come, and Y schal take you to my silf, that where Y am, ye be.
Ndipo ndikapita kukakukonzerani malo, ndidzabweranso kudzakutengani, kuti kumene kuli Ineko, inunso mukakhale komweko.
4 And whidur Y go, ye witen, and ye witen the weie.
Inu mukudziwa njira ya kumene Ine ndikupita.”
5 Thomas seith to hym, Lord, we witen not whidur thou goist, and hou moun we wite the weie?
Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye ife sitikudziwa kumene Inu mukupita, nanga tingadziwe bwanji njirayo?”
6 Jhesus seith to hym, Y am weie, treuthe, and lijf; no man cometh to the fadir, but bi me.
Yesu anayankha kuti, “Ine ndine njira, choonadi ndi moyo. Palibe munthu angafike kwa Atate popanda kudzera mwa Ine.
7 If ye hadden knowe me, sotheli ye hadden knowe also my fadir; and aftirward ye schulen knowe hym, and ye han seyn hym.
Mukanandidziwadi Ine, mukanadziwanso Atate anga. Kuyambira tsopano, mukuwadziwa ndipo mwawaona.”
8 Filip seith to hym, Lord, schewe to vs the fadir, and it suffisith to vs.
Filipo anati, “Ambuye, tionetseni Atatewo ndipo ife tikhutitsidwa.”
9 Jhesus seith to hym, So long tyme Y am with you, and `han ye not knowun me? Filip, he that seeth me, seeth also the fadir. Hou seist thou, schewe to vs the fadir?
Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe Filipo, ndakhala pakati panu nthawi yonseyi ndipo iwe sukundidziwabe? Aliyense amene waona Ine, waonanso Atate. Tsono ukunena bwanji kuti, ‘Tionetseni Atate?’
10 Bileuest thou not, that Y am in the fadir, and the fadir is in me? The wordis that Y speke to you, Y speke not of my silf; but the fadir hym silf dwellynge in me, doith the werkis.
Kodi sukukhulupirira kuti Ine ndili mwa Atate, ndipo Atate ali mwa Ine? Mawu amene Ine ndiyankhula kwa inu si mawu anga okha koma ndi mawu Atate wokhala mwa Ine, amene akugwira ntchito yake.
11 Bileue ye not, that Y am in the fadir, and the fadir is in me?
Khulupirirani Ine pamene ndi kuti Ine ndili mwa Atate ndipo Atate ali mwa Ine. Koma ngati si chomwecho, khulupiriranitu Ine chifukwa cha ntchito zanga zodabwitsa.
12 Ellis bileue ye for thilke werkis. Treuli, treuli, Y seie to you, if a man bileueth in me, also he schal do the werkis that Y do; and he schal do grettere werkis than these, for Y go to the fadir.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene akhulupirira Ine adzachita zimene Ine ndakhala ndikuchita. Iye adzachita ngakhale zinthu zazikulu kuposa zimenezi, chifukwa ndikupita kwa Atate.
13 And what euere thing ye axen the fadir in my name, Y schal do this thing, that the fadir be glorified in the sone.
Ndipo Ine ndidzachita chilichonse chimene inu mudzapempha mʼdzina langa kuti Atate alemekezedwe mwa Mwana.
14 If ye axen ony thing in my name, Y schal do it.
Ngati mudzapempha kanthu kalikonse mʼdzina langa, Ine ndidzachita.
15 If ye louen me, kepe ye my comaundementis.
“Ngati mundikonda Ine, sungani malamulo anga.
16 And Y schal preye the fadir, and he schal yyue to you another coumfortour, to dwelle with you with outen ende, (aiōn )
Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthawi zonse. (aiōn )
17 the spirit of treuthe; which spirit the world may not take, for it seeth hym not, nether knowith hym. But ye schulen knowe hym, for he schal dwelle with you, and he schal be in you.
Nkhosweyo ndiye Mzimu wachoonadi. Dziko lapansi silingalandire Nkhosweyi chifukwa samuona kapena kumudziwa. Koma inu mumamudziwa pakuti amakhala nanu ndipo adzakhala mwa inu.
18 Y schal not leeue you fadirles, Y schal come to you.
Ine sindikusiyani nokha kuti mukhale ana amasiye. Ine ndidzabweranso kwa inu.
19 Yit a litil, and the world seeth not now me; but ye schulen se me, for Y lyue, and ye schulen lyue.
Patsala nthawi yochepa dziko lapansi silidzandionanso koma inu mudzandiona. Popeza kuti Ine ndili ndi moyo, inunso mudzakhala ndi moyo.
20 In that dai ye schulen knowe, that Y am in my fadir, and ye in me, and Y in you.
Tsiku limenelo inu mudzazindikira kuti Ine ndili mwa Atate, ndipo inu muli mwa Ine, ndipo Ine ndili mwa inu.
21 He that hath my comaundementis, and kepith hem, he it is that loueth me; and he that loueth me, schal be loued of my fadir, and Y schal loue hym, and Y schal schewe to hym my silf.
Iye amene amadziwa malamulo anga ndi kuwasunga ndiye amene amandikonda. Wokonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga ndipo Inenso ndidzamukonda ndikudzionetsa ndekha kwa iye.”
22 Judas seith to hym, not he of Scarioth, Lord, what is don, that thou schalt schewe thi silf to vs, and not to the world?
Kenaka Yudasi (osati Yudasi Isikarioti) anati, “Koma Ambuye, nʼchifukwa chiyani mukufuna kudzionetsa nokha kwa ife, osati ku dziko lapansi?”
23 Jhesus answerde, and seide `to hym, If ony man loueth me, he schal kepe my word; and my fadir schal loue hym, and we schulen come to hym, and we schulen dwelle with hym.
Yesu anamuyankha kuti, “Ngati wina aliyense andikonda Ine, adzasunga mawu anga. Atate wanga adzamukonda, ndipo Ife tidzabwera ndi kukhala naye.
24 He that loueth me not, kepith not my wordis; and the word which ye han herd, is not myn, but the fadris, that sente me.
Iye amene sandikonda Ine sasunga mawu anga. Mawu awa amene mukumva si anga ndi a Atate amene anandituma Ine.
25 These thingis Y haue spokun to you, dwellynge among you; but thilke Hooli Goost,
“Ndayankhula zonsezi ndikanali nanu.
26 the coumfortour, whom the fadir schal sende in my name, he schal teche you alle thingis, `and schal schewe to you alle thingis, what euere thingis Y schal seie to you.
Koma Nkhosweyo, Mzimu Woyera, amene Atate adzamutumiza mʼdzina langa adzakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo adzakukumbutsani zonse zimene ndinakuwuzani.
27 Pees Y leeue to you, my pees Y yyue to you; not as the world yyueth, Y yiue to you; be not youre herte affrayed, ne drede it.
Ine ndikukusiyirani mtendere. Ndikukupatsani mtendere wanga. Ine sindikukupatsani monga dziko lapansi limaperekera. Mtima wanu usavutike ndipo musachite mantha.
28 Ye han herd, that Y seide to you, Y go, and come to you. If ye loueden me, forsothe ye schulden haue ioye, for Y go to the fadir, for the fadir is grettere than Y.
“Inu munamva Ine ndikunena kuti, ‘Ine ndikupita ndipo ndidzabweranso kwa inu.’ Mukanandikonda, mukanasangalala kuti Ine ndikupita kwa Atate, pakuti Atate ndi wamkulu kuposa Ine.
29 And now Y haue seid to you, bifor that it be don, that whanne it is don, ye bileuen.
Ine ndakuwuzani tsopano zisanachitike, kuti zikadzachitika mudzakhulupirire.
30 Now Y schal not speke many thingis with you; for the prince of this world cometh, and hath not in me ony thing.
Ine sindiyankhulanso nanu zambiri nthawi yayitali popeza wolamulira dziko lapansi akubwera. Iye alibe mphamvu pa Ine,
31 But that the world knowe, that Y loue the fadir; and as the fadir yaf a comaundement to me, so Y do. `Rise ye, go we hennus.
koma kuti dziko lapansi lizindikire kuti Ine ndimakonda Atate ndi kuti ndimachita zokhazokha zimene Atate wandilamulira Ine. “Nyamukani; tizipita.”