< John 12 >
1 Therfor Jhesus bifor sixe daies of pask cam to Bethanye, where Lazarus hadde be deed, whom Jhesus reiside.
Masiku asanu ndi limodzi Paska asanafike, Yesu anafika ku Betaniya, kumene kumakhala Lazaro, amene Yesu anamuukitsa kwa akufa.
2 And thei maden to hym a soopere there, and Martha mynystride to hym; and Lazarus was oon of men that saten at the mete with hym.
Kumeneko anamukonzera Yesu chakudya cha madzulo. Marita anatumikira pamene Lazaro anali mmodzi wa iwo amene anakhala nawo pa chakudyacho.
3 Therfor Marie took a pound of oynement of trewe narde precious, and anoyntide the feet of Jhesu, and wipte hise feet with hir heeris; and the hous was fulfillid of the sauour of the oynement.
Kenaka Mariya anatenga botolo la mafuta a nadi, onunkhira bwino kwambiri, amtengowapatali; Iye anadzoza mapazi a Yesu napukuta ndi tsitsi lake. Ndipo nyumba yonse inadzaza ndi fungo lonunkhira bwino la mafutawo.
4 Therfor Judas Scarioth, oon of hise disciplis, that was to bitraye hym,
Koma mmodzi wa ophunzira ake, Yudasi Isikarioti, amene pambuyo pake adzamupereka anati,
5 seide, Whi is not this oynement seeld for thre hundrid pens, and is youun to nedi men?
“Nʼchifukwa chiyani mafuta awa sanagulitsidwe ndipo ndalama zake nʼkuzipereka kwa osauka?” Mafutawo anali a mtengo wa malipiro a chaka chimodzi.
6 But he seide this thing, not for it perteynede to hym of nedi men, but for he was a theef, and he hadde the pursis, and bar tho thingis that weren sent.
Iye sananene izi chifukwa cha kuganizira osauka koma chifukwa anali mbava; ngati wosunga thumba la ndalama, amabamo zomwe ankayikamo.
7 Therfor Jhesus seide, Suffre ye hir, that in to the day of my biriyng sche kepe that;
Yesu anayankha kuti, “Mulekeni. Mafutawa anayenera kusungidwa mpaka tsiku loyika maliro anga.
8 for ye schulen euermore haue pore men with you, but ye schulen not euermore haue me.
Inu mudzakhala ndi osauka nthawi zonse, koma simudzakhala nane nthawi zonse.”
9 Therfore myche puple of Jewis knew, that Jhesus was there; and thei camen, not oonli for Jhesu, but to se Lazarus, whom he hadde reisid fro deth.
Pa nthawi imeneyi gulu lalikulu la Ayuda linadziwa kuti Yesu anali kumeneko, ndipo linabwera, sichifukwa cha Iye yekha koma kudzaonanso Lazaro, amene anamuukitsa kwa akufa.
10 But the princis of prestis thouyten to sle Lazarus,
Choncho akulu a ansembe anakonza njira yoti aphenso Lazaro,
11 for manye of the Jewis wenten awei for him, and bileueden in Jhesu.
pakuti chifukwa cha iye Ayuda ambiri amapita kwa Yesu ndi kumukhulupirira.
12 But on the morew a myche puple, that cam togidere to the feeste dai, whanne thei hadden herd, that Jhesus cam to Jerusalem,
Tsiku lotsatira, gulu lalikulu la anthu lomwe linabwera kuphwando linamva kuti Yesu anali mʼnjira kupita ku Yerusalemu.
13 token braunchis of palmes, and camen forth ayens hym, and crieden, Osanna, blessid is the kyng of Israel, that cometh in the name of the Lord.
Iwo anatenga nthambi za kanjedza ndi kupita kukakumana naye, akufuwula kuti, “Hosana! “Wodala Iye amene akubwera mʼdzina la Ambuye! “Yodala Mfumu ya Israeli!”
14 And Jhesus foond a yonge asse, and sat on hym,
Yesu anapeza bulu wamngʼono ndi kukwerapo, monga kunalembedwa kuti:
15 as it is writun, The douytir of Syon, nyle thou drede; lo! thi kyng cometh, sittynge on `an asse fole.
“Usachite mantha mwana wamkazi wa Ziyoni; taona mfumu yako ikubwera, itakhala pa mwana wabulu.”
16 Hise disciplis knewen not first these thingis, but whanne Jhesus was glorified, thanne thei hadden mynde, for these thingis weren writun of hym, and these thingis thei diden to hym.
Poyamba ophunzira ake sanamvetsetse zonsezi. Koma pomwe Yesu analemekezedwa ndi pamene anazindikira kuti zinthu izi zinalembedwa ndipo kuti anamuchitira Iye.
17 Therfor the puple bar witnessyng, that was with hym, whanne he clepide Lazarus fro the graue, and reiside hym fro deth.
Tsopano gulu la anthu lomwe linali naye pa nthawi imene amaukitsidwa Lazaro ku manda linapitiriza kuchitira umboni.
18 And therfor the puple cam, and mette with hym, for thei herden that he hadde don this signe.
Anthu ambiri, anapita kukakumana naye, chifukwa iwo anamva kuti Iye anachita chizindikiro chodabwitsachi.
19 Therfor the Farisees seiden to hem silf, Ye seen, that we profiten no thing; lo! al the world wente aftir hym.
Choncho Afarisi anati kwa wina ndi mnzake, “Taonani, palibe chimene mwachitapo. Anthu onse akumutsatira Iye!”
20 And there weren summe hethene men, of hem that hadden come vp to worschipe in the feeste dai.
Tsopano panali Agriki ena pakati pa amene anapita kukapembedza ku phwando.
21 And these camen to Filip, that was of Bethsaida of Galilee, and preieden hym, and seiden, Sire, we wolen se Jhesu.
Iwo anabwera kwa Filipo, wochokera ku Betisaida wa ku Galileya, ndi pempho, nati, “Akulu, ife tikufuna kuona Yesu.”
22 Filip cometh, and seith to Andrew; eft Andrew and Filip seiden to Jhesu.
Filipo anapita kukawuza Andreya; Andreya ndi Filipo pamodzi anakawuza Yesu.
23 And Jhesus answerde `to hem, and seide, The our cometh, that mannus sone be clarified.
Yesu anayankha kuti, “Nthawi yafika yakuti Mwana wa Munthu alemekezedwe.
24 Treuli, treuli, Y seie to you, but a corn of whete falle in to the erthe, and be deed, it dwellith aloone; but if it be deed, it bryngith myche fruyt.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti, ‘Mbewu ya tirigu imakhala imodzi yokha ngati sikugwa mʼnthaka ndi kufa. Koma ngati imfa, imabereka mbewu zambiri.’
25 He that loueth his lijf, schal leese it; and he that hatith his lijf in this world, kepith it in to euerlastynge lijf. (aiōnios )
Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. (aiōnios )
26 If ony man serue me, sue he me; and where Y am, there my mynystre schal be. If ony man serue me, my fadir schal worschipe hym.
Aliyense amene atumikira Ine ayenera kunditsata; ndipo kumene Ine ndili, wotumikira wanga adzakhalanso komweko. Atate anga adzalemekeza amene atumikira Ine.
27 Now my soule is troublid, and what schal Y seie? Fadir, saue me fro this our; but therfor Y cam in to this our;
“Moyo wanga ukuvutika tsopano, kodi ndidzanena chiyani? Ndinene kuti Atate pulumutseni ku nthawi ino? Ayi. Chifukwa chimene Ine ndinabwera pa nthawi iyi ndi chimenechi.
28 fadir, clarifie thi name. And a vois cam fro heuene, and seide, And Y haue clarified, and eft Y schal clarifie.
Atate, lemekezani dzina lanu!” Kenaka mawu anabwera kuchokera kumwamba, “Ine ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.”
29 Therfor the puple that stood, and herde, seide, that `thundur was maad; othere men seide, an aungel spak to hym.
Gulu la anthu lomwe linali pamenepo litamva linati, “Kwagunda bingu,” ena anati, “Mngelo wayankhula kwa Iye.”
30 Jhesus answerde, and seide, This vois cam not for me, but for you.
Yesu anati, “Mawu awa abwera chifukwa cha inu osati chifukwa cha Ine.
31 Now is the doom of the world, now the prince of this world schal be cast out.
Ino tsopano ndi nthawi yachiweruzo pa dziko lapansi; tsopano olamulira wa dziko lapansi adzathamangitsidwa.
32 And if Y schal be enhaunsid fro the erthe, Y schal drawe alle thingis to my silf.
Koma Ine, akadzandipachika pa dziko lapansi, ndidzakokera anthu onse kwa Ine.”
33 And he seide this thing, signifiynge bi what deth he `was to die.
Iye ananena izi kuti aonetse mmene adzafere.
34 And the puple answeride to hym, We han herd of the lawe, that Crist dwellith with outen ende; and hou seist thou, It bihoueth mannys sone to be arerid? Who is this mannus sone? (aiōn )
Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?” (aiōn )
35 And thanne Jhesus seith to hem, Yit a litil liyt is in you; walke ye, the while ye han liyt, that derknessis catche you not; he that wandrith in derknessis, woot nere whidur he goith.
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Inu mukhala ndi kuwunika kwa nthawi pangʼono. Yendani pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mdima usakupitirireni. Munthu amene amayenda mu mdima sadziwa kumene akupita.
36 While ye han liyt, bileue ye in liyt, that ye be the children of liyt. Jhesus spak these thingis, and wente, and hidde hym fro hem.
Khulupirirani kuwunika, pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mukhale ana a kuwunika.” Yesu atamaliza kuyankhula izi, Iye anachoka nabisala kuti asamuone.
37 And whanne he hadde don so many myraclis bifor hem, thei bileueden not `in to hym;
Ngakhale Yesu anachita zizindikiro zodabwitsa zonsezi pamaso pawo, sanamukhulupirirebe.
38 that the word of Ysaie, the prophete, schulde be fulfillid, which he seide, Lord, who bileuede to oure heryng, and to whom is the arm of the Lord schewid?
Izi zinakwaniritsa mawu a mneneri Yesaya kuti: “Ambuye, wakhulupirira uthenga wathu ndani, ndipo ndi kwa yani komwe mkono wa Ambuye wavumbulutsidwa?”
39 Therfor thei myyten not bileue, for eft Ysaye seide,
Pa chifukwa cha ichi iwo sanakhulupirire, chifukwa Yesaya ananenanso kuti:
40 He hath blyndid her iyen, and he hath maad hard the herte of hem, that thei se not with iyen, and vndurstonde with herte; and that thei be conuertid, and Y heele hem.
“Iye wachititsa khungu maso awo ndi kuwumitsa mitima yawo, kotero kuti iwo sangathe kuona ndi maso awo, kapena kuzindikira ndi mitima yawo, kapena kutembenuka kuti Ine ndikanawachiza.”
41 Ysaye seide these thingis, whanne he say the glorie of hym, and spak of hym.
Yesaya ananena izi chifukwa anaona ulemerero wa Yesu ndi kuyankhula za Iye.
42 Netheles `of the pryncis manye bileueden in hym, but for the Farisees thei knowlechiden not, that thei schulden not be put out of the synagoge;
Komabe pa nthawi yomweyi ambiri ngakhale atsogoleri anakhulupirira Iye. Koma chifukwa cha Afarisi iwo sanavomereze chikhulupiriro chawo chifukwa amaopa kuti angawatulutse mʼsunagoge;
43 for thei loueden the glorie of men, more than the glorie of God.
pakuti iwo amakonda kuyamikiridwa ndi anthu kuposa kuyamikiridwa ndi Mulungu.
44 And Jhesus criede, and seide, He that bileueth in me, bileueth not in me, but in hym that sente me.
Kenaka Yesu anafuwula nati, “Munthu aliyense amene akhulupirira Ine, sakhulupirira Ine ndekha, komanso Iye amene anandituma Ine.
45 He that seeth me, seeth hym that sente me.
Iye amene waona Ine, waonanso Iye amene anandituma Ine.
46 Y liyt cam in to the world, that ech that bileueth in me, dwelle not in derknessis.
Ine ndabwera mʼdziko lapansi monga kuwunika, kotero palibe amene amakhulupirira Ine nʼkumakhalabe mu mdima.
47 And if ony man herith my words, and kepith hem, Y deme hym not; for Y cam not, that Y deme the world, but that Y make the world saaf.
“Ndipo munthu amene amva mawu anga koma osawasunga, Ine sindimuweruza. Pakuti Ine sindinabwere kudzaweruza dziko lapansi, koma kudzapulumutsa.
48 He that dispisith me, and takith not my wordis, hath hym that schal iuge hym; thilke word that Y haue spokun, schal deme hym in the last dai.
Iye amene akana Ine ndipo salandira mawu anga ali ndi womuweruza. Tsiku lomaliza mawu amene ndiyankhulawa adzamutsutsa.
49 For Y haue not spokun of my silf, but thilke fadir that sente me, yaf to me a maundement, what Y schal seie, and what Y schal speke.
Pakuti Ine sindiyankhula mwa Ine ndekha, koma Atate amene anandituma amandilamulira choti ndinene ndi momwe ndinenere.
50 And Y woot, that his maundement is euerlastynge lijf; therfor tho thingis that Y speke, as the fadir seide to me, so Y speke. (aiōnios )
Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.” (aiōnios )