< John 11 >
1 And ther was a sijk man, Lazarus of Bethanye, of the castel of Marie and Martha, hise sistris.
Tsopano munthu wina dzina lake Lazaro anadwala. Iye anali wa ku Betaniya, mudzi wa Mariya ndi mchemwali wake Marita.
2 And it was Marye, which anoyntide the Lord with oynement, and wipte hise feet with hir heeris, whos brother Lazarus was sijk.
Mariyayo ndi yemwe uja amene anadzoza Ambuye ndi mafuta onunkhira napukuta mapazi ake ndi tsitsi lake. Lazaro wodwalayo anali mlongo wake.
3 Therfor hise sistris senten to hym, and seide, Lord, lo! he whom thou louest, is sijk.
Choncho alongo ake anatumiza mawu kwa Yesu kuti, “Ambuye, uja amene Inu mumamukonda akudwala.”
4 And Jhesus herde, and seide to hem, This syknesse is not to the deth, but for the glorie of God, that mannus sone be glorified bi hym.
Atamva izi, Yesu anati, “Kudwalako safa nako. Koma akudwala kuti Mulungu alemekezedwe; ndi kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe chifukwa cha matendawo.”
5 And Jhesus louyde Martha, and hir sistir Marie, and Lazarus.
Yesu anakonda Marita, mchemwali wake ndi Lazaro.
6 Therfor whanne Jhesus herde, that he was sijk, thanne he dwellide in the same place twei daies.
Koma atamva kuti Lazaro akudwala, Iye anakhalabe kumene anali masiku ena awiri.
7 And after these thingis he seide to hise disciplis, Go we eft in to Judee.
Kenaka anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tibwerere ku Yudeya.”
8 The disciplis seien to hym, Maister, now the Jewis souyten for to stoone thee, and eft goist thou thidir?
Ophunzira akewo anati, “Rabi, posachedwa pomwepa Ayuda anafuna kukugendani ndi miyala, koma Inu mukupitanso komweko?”
9 Jhesus answerde, Whether ther ben not twelue ouris of the dai? If ony man wandre in the dai, he hirtith not, for he seeth the liyt of this world.
Yesu anayankha kuti, “Kodi sipali maora khumi ndi awiri pa tsiku? Munthu amene amayenda masana sapunthwa, popeza akuona chifukwa cha kuwala kwa dziko lapansi.
10 But if he wandre in the niyt, he stomblith, for liyt is not in him.
Koma amene akuyenda usiku amapunthwa, chifukwa kuwalako alibe.”
11 He seith these thingis, and aftir these thingis he seith to hem, Lazarus, oure freend, slepith, but Y go to reise hym fro sleep.
Iye atatha kunena izi, anapitirira kuwawuza iwo kuti, “Bwenzi lathu Lazaro wagona tulo; koma Ine ndikupita kumeneko kukamudzutsa.”
12 Therfor hise disciplis seiden, Lord, if he slepith, he schal be saaf.
Ophunzira ake anayankha kuti, “Ambuye, ngati wagona adzapeza bwino.”
13 But Jhesus hadde seid of his deth; but thei gessiden, that he seide of slepyng of sleep.
Yesu ankayankhula za imfa yake koma ophunzira ake ankaganiza kuti amanena za tulo chabe.
14 Thanne therfor Jhesus seide to hem opynli, Lazarus is deed;
Ndipo kenaka anawawuza momveka kuti, “Lazaro wamwalira.
15 and Y haue ioye for you, that ye bileue, for Y was not there; but go we to hym.
Ine ndikukondwera chifukwa cha inu kuti kunalibe kumeneko; koma kuti mukakhulupirire tiyeni tipiteko.”
16 Therfor Thomas, that is seid Didymus, seide to euen disciplis, Go we also, that we dien with hym.
Pamenepo Tomasi, wotchedwa Didimo, anati kwa ophunzira anzake, “Tiyeni nafenso tipite, kuti tikafere naye pamodzi.”
17 And so Jhesus cam, and foond hym hauynge thanne foure daies in the graue.
Yesu atafika, anapeza kuti Lazaro anali atagona mʼmanda masiku anayi.
18 And Bethany was bisidis Jerusalem, as it were fiftene furlongis.
Mudzi wa Betaniya unali pafupi ndi Yerusalemu pa mtunda wosachepera makilomita atatu,
19 And many of the Jewis camen to Mary and Martha, to coumforte hem of her brothir.
ndipo Ayuda ambiri anabwera kwa Marita ndi Mariya kudzawatonthoza pa imfa ya mʼbale wawo.
20 Therfor as Martha herde, that Jhesu cam, sche ran to hym; but Mary sat at home.
Pamene Marita anamva kuti Yesu akubwera, anapita kukakumana naye. Koma Mariya anatsala ku nyumba.
21 Therfor Martha seide to Jhesu, Lord, if thou haddist be here, my brother hadde not be deed.
Marita anati kwa Yesu, “Ambuye, mukanakhala muli kuno, mlongo wanga sakanamwalira.
22 But now Y woot, that what euere thingis thou schalt axe of God, God schal yyue to thee.
Koma ine ndikudziwa kuti ngakhale tsopano Mulungu adzakupatsani chilichonse chimene mudzamupempha.”
23 Jhesus seith to hir, Thi brother schal rise ayen.
Yesu anati kwa iye, “Mlongo wako adzauka.”
24 Martha seith to hym, Y woot, that he schal rise ayen in the ayen risyng in the laste dai.
Marita anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti adzauka pa kuukanso pa tsiku lomaliza.”
25 Jhesus seith to hir, Y am ayen risyng and lijf; he that bileueth in me, yhe, thouy he be deed, he schal lyue;
Yesu anati kwa iye, “Ine ndine kuuka ndi moyo. Wokhulupirira Ine, angakhale amwalira adzakhala ndi moyo.
26 and ech that lyueth, and bileueth in me, schal not die with outen ende. Bileuest thou this thing? (aiōn )
Aliyense amene ali ndi moyo ndi kukhulupirira Ine sadzamwalira. Kodi iwe ukukhulupirira izi?” (aiōn )
27 Sche seith to hym, Yhe, Lord, Y haue bileued, that thou art Crist, the sone of the lyuynge God, that hast come in to this world.
Marita anamuwuza Iye kuti, “Inde Ambuye, ine ndikukhulupirira kuti ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu, amene abwera mʼdziko lapansi.”
28 And whanne sche hadde seid this thing, sche wente, and clepide Marie, hir sistir, in silence, and seide, The maister cometh, and clepith thee.
Ndipo iye atanena izi anabwerera ndi kukayitana mchemwali wake Mariya namuyankhula monongʼona pambali, nati, “Aphunzitsi abwera ndipo akukuyitana.”
29 Sche, as sche herd, aroos anoon, and cam to hym.
Mariya atamva izi, anayimirira mofulumira napita kwa Iye.
30 And Jhesus cam not yit `in to the castel, but he was yit in that place, where Martha hadde comun ayens hym.
Tsopano nʼkuti Yesu asanalowe mʼmudzi, koma anali akanali pa malo pamene Marita anakumana naye.
31 Therfor the Jewis that weren with hir in the hous, and coumfortiden hir, whanne thei sayn Marie, that sche roos swithe, and wente out, thei sueden hir, and seiden, For sche goith to the graue, to wepe there.
Ayuda amene ankamutonthoza Mariya mʼnyumba, anaona mmene iye anayimira mofulumira ndi kutuluka kunja, iwo anamutsata akuganizira kuti ankapita ku manda kukalirira kumeneko.
32 But whanne Marie was comun where Jhesus was, sche seynge hym felde doun to his feet, and seide to hym, Lord, if thou haddist be here, my brother hadde not be deed.
Mariya anafika pamalo pamene panali Yesu ndipo atamuona, anagwa pa mapazi ake ndipo anati, “Ambuye mukanakhala muli kuno mlongo wanga sakanamwalira.”
33 And therfor whanne Jhesu saiy hir wepyng, and the Jewis wepynge that weren with hir, he `made noise in spirit, and troblide hym silf,
Yesu ataona iye akulira, ndi Ayuda amene anabwera naye akuliranso, anakhudzidwa kwambiri ndi kuvutika mu mzimu.
34 and seide, Where han ye leid hym? Thei seien to hym, Lord, come, and se.
Iye anafunsa kuti, “Kodi mwamuyika kuti?” Iwo anayankha kuti, “Ambuye tiyeni mukaone.”
35 And Jhesus wepte. Therfor the Jewis seiden,
Yesu analira.
36 Lo! hou he louede hym.
Pamenepo Ayuda anati, “Taonani mmene Iye anamukondera Lazaro!”
37 And summe of hem seiden, Whethir this man that openyde the iyen of the borun blynde man, myyte not make that this schulde not die?
Koma ena a iwo anati, “Iye amatsekula maso a munthu wosaona, kodi sakanakhoza kuletsa kuti munthu uyu asamwalire?”
38 Therfor Jhesus eft makynge noise in hym silf, cam to the graue. And there was a denne, and a stoon was leid theronne.
Yesu atakhudzidwanso kwambiri anafika ku manda. Manda akewo anali phanga ndipo anatsekapo ndi mwala.
39 And Jhesus seith, Take ye awey the stoon. Martha, the sistir of hym that was deed, seith to hym, Lord, he stynkith now, for he hath leye foure daies.
Yesu anati, “Chotsani mwala.” Marita mlongo wa womwalirayo anati, “Koma Ambuye, nthawi ino wayamba kununkha, pakuti wakhala mʼmenemu masiku anayi.”
40 Jhesus seith to hir, Haue Y not seid to thee, that if thou bileuest, thou schalt se the glorie of God?
Kenaka Yesu anati, “Kodi Ine sindinakuwuze kuti ngati iwe ukhulupirira, udzaona ulemerero wa Mulungu?”
41 Therfor thei token awei the stoon. And Jhesus lifte vp hise iyen, and seide, Fadir, Y do thankyngis to thee, for thou hast herd me; and Y wiste,
Choncho iwo anachotsa mwalawo. Kenaka Yesu anayangʼana kumwamba ndikuti, “Atate, Ine ndikukuthokozani chifukwa mumandimvera.
42 that thou euermore herist me, but for the puple that stondith aboute, Y seide, that thei bileue, that thou hast sent me.
Ine ndimadziwa kuti Inu mumandimvera nthawi zonse, koma Ine ndanena izi chifukwa cha anthu amene ayima pano, kuti iwo akhulupirire kuti Inu munandituma Ine.”
43 Whanne he hadde seid these thingis, he criede with a greet vois, Lazarus, come thou forth.
Yesu atanena izi, Iye anayitana ndi mawu ofuwula kuti, “Lazaro, tuluka!”
44 And anoon he that was deed, cam out, boundun the hondis and feet with boondis, and his face boundun with a sudarie. And Jhesus seith to hem, Vnbynde ye hym, and suffre ye hym to go forth.
Munthu womwalirayo anatuluka, womangidwa miyendo ndi manja ndi nsalu za ku manda, ndi nkhope yake yokulungidwa nsalu. Yesu anawawuza kuti, “Mʼmasuleni, ndipo muloleni apite.”
45 Therfor many of the Jewis that camen to Marie and Martha, and seyn what thingis Jhesus dide, bileueden in hym.
Choncho Ayuda ambiri amene anabwera kudzamuchereza Mariya ndi kuona zimene Yesu anachita anamukhulupirira Iye.
46 But summe of hem wente to the Farisees, and seiden to hem, what thingis Jhesus `hadde don.
Koma ena a iwo anapita kwa Afarisi ndi kukawawuza zimene Yesu anachita.
47 Therfor the bischopis and the Farisees gadriden a counsel ayens Jhesu, and seiden, What do we? for this man doith many myraclis.
Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anayitanitsa msonkhano wa akulu olamulira. Iwo anafunsa kuti, “Kodi ife tikuchita chiyani? Pano pali munthu uyu akuchita zizindikiro zodabwitsa zambiri.
48 If we leeue hym thus, alle men schulen bileue in hym; and Romayns schulen come, and schulen take our place and oure folk.
Ngati ife timuleka kuti apitirize chotere, aliyense adzamukhulupirira Iye, ndipo kenaka Aroma adzabwera ndi kudzatenga malo athu pamodzi ndi dziko lathu.”
49 But oon of hem, Cayfas bi name, whanne he was bischop of that yeer, seide to hem,
Kenaka mmodzi wa iwo, dzina lake Kayafa, amene anali mkulu wa ansembe chaka chimenecho, anayankhula kuti, “Inu simukudziwa kanthu kalikonse!
50 Ye witen nothing, ne thenken, that it spedith to you, that o man die for the puple, and that al the folc perische not.
Inu simukuzindikira kuti kuli bwino kwa inu kuti munthu mmodzi afe mʼmalo mwa anthu kusiyana ndi kuti mtundu wonse uwonongeke.”
51 But he seide not this thing of hym silf, but whanne he was bischop of that yeer, he prophesiede, that Jhesu was to die for the folc,
Iye sananene izi mwa iye yekha, koma monga mkulu wa ansembe chaka chimenecho ananenera kuti Yesu anayanera kufera mtundu wa Ayuda,
52 and not oneli for the folc, but that he schulde gadere in to oon the sones of God that weren scaterid.
ndipo osati mtundu okhawo komanso kwa ana ena a Mulungu onse obalalikana, kuti awabweretse pamodzi ndi kuwapanga kukhala amodzi.
53 Therfor fro that day thei souyten for to sle hym.
Choncho kuyambira tsiku limeneli iwo anakonzekera za kuti amuphe.
54 Therfor Jhesus walkide not thanne opynli among the Jewis; but he wente in to a cuntre bisidis desert, in to a citee, that is seid Effren, and there he dwellide with hise disciplis.
Chifukwa cha ichi Yesu sanayendenso moonekera pakati pa Ayuda. Mʼmalo mwake Iye anapita ku chigawo cha kufupi ndi chipululu, ku mudzi wa Efereimu, kumene Iye anakhalako ndi ophunzira ake.
55 And the pask of the Jewis was niy, and many of the cuntrey wenten vp to Jerusalem bifor the pask, to halewe hem silf.
Nthawi ya Paska wa Ayuda itayandikira, ambiri anakwera kupita ku Yerusalemu kuchokera ku madera a ku midzi chifukwa cha mwambo wa kuyeretsedwa Paska asanafike.
56 Therfor thei souyten Jhesu, and spaken togidere, stondynge in the temple, What gessen ye, for he cometh not to the feeste day?
Iwo anapitiriza kumufunafuna Yesu, ndipo pamene ankayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi ukuganiza chiyani? Kodi Iye sabwera konse kuphwando?”
57 For the bischopis and Farisees hadden youun a maundement, that if ony man knowe where he is, that he schewe, that thei take hym.
Koma akulu a ansembe ndi Afarisi anapereka lamulo kuti ngati wina aliyense adziwe kumene kunali Yesu, iye akawawuze kuti akamugwire.