< Job 8 >

1 Sotheli Baldath Suytes answeride, and seide,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Hou longe schalt thou speke siche thingis? The spirit of the word of thi mouth is manyfold.
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Whether God supplauntith, `ethir disseyueth, doom, and whether Almyyti God distrieth that, that is iust?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Yhe, thouy thi sones synneden ayens hym, and he lefte hem in the hond of her wickidnesse;
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 netheles, if thou risist eerli to God, and bisechist `Almyyti God, if thou goist clene and riytful,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 anoon he schal wake fulli to thee, and schal make pesible the dwellyng place of thi ryytfulnesse;
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 in so miche that thi formere thingis weren litil, and that thi laste thingis be multiplied greetli.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 For whi, axe thou the formere generacioun, and seke thou diligentli the mynde of fadris.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 For we ben men of yistirdai, and `kunnen not; for oure daies ben as schadewe on the erthe.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 And thei schulen teche thee, thei schulen speke to thee, and of her herte thei schulen bring forth spechis.
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Whether a rusche may lyue with out moysture? ethir a spier `may wexe with out watir?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Whanne it is yit in the flour, nethir is takun with hond, it wexeth drie bifor alle erbis.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 So the weies of alle men, that foryeten God; and the hope of an ypocrite schal perische.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 His cowardise schal not plese hym, and his trist schal be as a web of yreyns.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 He schal leene, `ether reste, on his hows, and it schal not stonde; he schal vndursette it, and it schal not rise togidere.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 The rusche semeth moist, bifor that the sunne come; and in the risyng of the sunne the seed therof schal go out.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Rootis therof schulen be maad thicke on an heep of stoonys, and it schal dwelle among stoonys.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 If a man drawith it out of `his place, his place schal denye it, and schal seie, Y knowe thee not.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 For this is the gladnesse of his weie, that eft othere ruschis springe out of the erthe.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Forsothe God schal not caste a wei a symple man, nethir schal dresse hond to wickid men;
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 til thi mouth be fillid with leiytir, and thi lippis with hertli song.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Thei that haten thee schulen be clothid with schenschip; and the tabernacle of wickid men schal not stonde.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >